Add parallel Print Page Options

Mphatso ya Uneneri ndi ya Malilime

14 Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri. Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi. Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi. Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo. Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.

Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso. Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino? Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo? Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha. 10 Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo. 11 Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine. 12 Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.

13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena. 14 Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu. 15 Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga. 16 Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena? 17 Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.

18 Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu. 19 Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.

20 Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima. 21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti,

“Ndidzayankhula kwa anthu awa,
    kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo
ndiponso ndi milomo yachilendo.
    Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine,
            akutero Ambuye.”

22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira. 23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala? 24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse 25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”

Kupembedza Mwadongosolo

26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo. 27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo. 28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.

29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo. 30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete. 31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa. 32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri. 33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.

Amayi Akhale Chete mu Mpingo

34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera. 35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.

36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha? 37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye. 38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.

39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime. 40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.

Intelligibility in Worship

14 Follow the way of love(A) and eagerly desire(B) gifts of the Spirit,(C) especially prophecy.(D) For anyone who speaks in a tongue[a](E) does not speak to people but to God. Indeed, no one understands them;(F) they utter mysteries(G) by the Spirit. But the one who prophesies speaks to people for their strengthening,(H) encouraging(I) and comfort. Anyone who speaks in a tongue(J) edifies(K) themselves, but the one who prophesies(L) edifies the church. I would like every one of you to speak in tongues,[b] but I would rather have you prophesy.(M) The one who prophesies is greater than the one who speaks in tongues,[c] unless someone interprets, so that the church may be edified.(N)

Now, brothers and sisters, if I come to you and speak in tongues, what good will I be to you, unless I bring you some revelation(O) or knowledge(P) or prophecy or word of instruction?(Q) Even in the case of lifeless things that make sounds, such as the pipe or harp, how will anyone know what tune is being played unless there is a distinction in the notes? Again, if the trumpet does not sound a clear call, who will get ready for battle?(R) So it is with you. Unless you speak intelligible words with your tongue, how will anyone know what you are saying? You will just be speaking into the air. 10 Undoubtedly there are all sorts of languages in the world, yet none of them is without meaning. 11 If then I do not grasp the meaning of what someone is saying, I am a foreigner to the speaker, and the speaker is a foreigner to me.(S) 12 So it is with you. Since you are eager for gifts of the Spirit,(T) try to excel in those that build up(U) the church.

13 For this reason the one who speaks in a tongue should pray that they may interpret what they say.(V) 14 For if I pray in a tongue, my spirit prays,(W) but my mind is unfruitful. 15 So what shall I do? I will pray with my spirit,(X) but I will also pray with my understanding; I will sing(Y) with my spirit, but I will also sing with my understanding. 16 Otherwise when you are praising God in the Spirit, how can someone else, who is now put in the position of an inquirer,[d] say “Amen”(Z) to your thanksgiving,(AA) since they do not know what you are saying? 17 You are giving thanks well enough, but no one else is edified.(AB)

18 I thank God that I speak in tongues more than all of you. 19 But in the church I would rather speak five intelligible words to instruct others than ten thousand words in a tongue.(AC)

20 Brothers and sisters, stop thinking like children.(AD) In regard to evil be infants,(AE) but in your thinking be adults. 21 In the Law(AF) it is written:

“With other tongues
    and through the lips of foreigners
I will speak to this people,
    but even then they will not listen to me,(AG)
says the Lord.”[e]

22 Tongues, then, are a sign, not for believers but for unbelievers; prophecy,(AH) however, is not for unbelievers but for believers. 23 So if the whole church comes together and everyone speaks in tongues, and inquirers or unbelievers come in, will they not say that you are out of your mind?(AI) 24 But if an unbeliever or an inquirer comes in while everyone is prophesying, they are convicted of sin and are brought under judgment by all, 25 as the secrets(AJ) of their hearts are laid bare. So they will fall down and worship God, exclaiming, “God is really among you!”(AK)

Good Order in Worship

26 What then shall we say, brothers and sisters?(AL) When you come together, each of you(AM) has a hymn,(AN) or a word of instruction,(AO) a revelation, a tongue(AP) or an interpretation.(AQ) Everything must be done so that the church may be built up.(AR) 27 If anyone speaks in a tongue, two—or at the most three—should speak, one at a time, and someone must interpret. 28 If there is no interpreter, the speaker should keep quiet in the church and speak to himself and to God.

29 Two or three prophets(AS) should speak, and the others should weigh carefully what is said.(AT) 30 And if a revelation comes to someone who is sitting down, the first speaker should stop. 31 For you can all prophesy in turn so that everyone may be instructed and encouraged. 32 The spirits of prophets are subject to the control of prophets.(AU) 33 For God is not a God of disorder(AV) but of peace(AW)—as in all the congregations(AX) of the Lord’s people.(AY)

34 Women[f] should remain silent in the churches. They are not allowed to speak,(AZ) but must be in submission,(BA) as the law(BB) says. 35 If they want to inquire about something, they should ask their own husbands at home; for it is disgraceful for a woman to speak in the church.[g]

36 Or did the word of God(BC) originate with you? Or are you the only people it has reached? 37 If anyone thinks they are a prophet(BD) or otherwise gifted by the Spirit,(BE) let them acknowledge that what I am writing to you is the Lord’s command.(BF) 38 But if anyone ignores this, they will themselves be ignored.[h]

39 Therefore, my brothers and sisters, be eager(BG) to prophesy,(BH) and do not forbid speaking in tongues. 40 But everything should be done in a fitting and orderly(BI) way.

Footnotes

  1. 1 Corinthians 14:2 Or in another language; also in verses 4, 13, 14, 19, 26 and 27
  2. 1 Corinthians 14:5 Or in other languages; also in verses 6, 18, 22, 23 and 39
  3. 1 Corinthians 14:5 Or in other languages; also in verses 6, 18, 22, 23 and 39
  4. 1 Corinthians 14:16 The Greek word for inquirer is a technical term for someone not fully initiated into a religion; also in verses 23 and 24.
  5. 1 Corinthians 14:21 Isaiah 28:11,12
  6. 1 Corinthians 14:34 Or peace. As in all the congregations of the Lord’s people, 34 women
  7. 1 Corinthians 14:35 In a few manuscripts these verses come after verse 40.
  8. 1 Corinthians 14:38 Some manuscripts But anyone who is ignorant of this will be ignorant