Add parallel Print Page Options

Milandu Pakati pa Anthu Okhulupirira

Pamene wina wa inu ali ndi mlandu ndi mnzake, nʼchifukwa chiyani amatengera nkhaniyo kwa anthu akunja kuti akawaweruze mʼmalo mopita nayo kwa oyera mtima? Kodi inu simukudziwa kuti anthu a Mulungu adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati inu mungaweruze dziko lapansi, kodi sindinu oyenera kuweruza milandu ingʼonoyingʼono? Kodi simukudziwa kuti mudzaweruza angelo? Nanga bwanji zinthu za mʼmoyo uno! Nʼchifukwa chake, ngati pali milandu pa zinthu zotere, sankhani anthu ena kuti akhale oweruza ngakhale alibe udindo mu mpingo. Ndikunena izi kuti ndikuchititseni manyazi. Moti nʼkutheka kuti pakati panu palibe wina wanzeru zokwanira kuti aziweruza mlandu pakati pa Akhristu? Koma mʼmalo mwake mʼbale atengera ku bwalo la mlandu mʼbale mnzake kukaweruzidwa. Zonsezi pamaso pa akunja!

Chokha choti mwakasumirana chikuonetseratu kuti mwagonjetsedwa kale. Bwanji osangolola kuti ena akulakwireni? Bwanji osangolola kuti ena akubereni? Mʼmalo mwake, inuyo ndiye mumabera ena ndi kuwalakwira, ndipo mumachita izi kwa abale anu. Kodi simukudziwa kuti munthu woyipa sadzalowa mu ufumu wa Mulungu? Musanyengedwe: achigololo, kapena opembedza mafano, kapena achiwerewere, kapena amuna adama, kapena ogonana ndi amuna okhaokha; 10 kapena akuba, kapena aumbombo, kapena oledzera, kapena achipongwe, kapena opeza ndalama mwachinyengo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu. 11 Ndipo umu ndi mmene ena mwa inu munalili. Koma munatsukidwa, munayeretsedwa, munalungamitsidwa mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu ndi Mzimu wa Mulungu wathu.

Chigololo

12 Inu mumati, “Ine ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Komatu si zonse zimene nʼzothandiza. “Ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Koma sindidzagonjetsedwa ndi chilichonse. 13 Inu mumati, “Chakudya, kwake nʼkulowa mʼmimba ndipo mimba ntchito yake nʼkulandira chakudyacho.” Koma Mulungu adzawononga zonsezi. Thupi silochitira chigololo, koma la Ambuye, ndipo Ambuye ndiye mwini thupilo. 14 Mwamphamvu zake Mulungu anaukitsa Ambuye kwa akufa, ndipo ifenso adzatiukitsa. 15 Kodi simukudziwa kuti matupi anuwo ndi ziwalo za Khristu mwini? Kodi tsono ndingatenge ziwalo za Khristu nʼkuzisandutsa ziwalo za mkazi wadama? Zosatheka! 16 Kodi simukudziwa kuti amene amadzipereka kwa mkazi wadama, iyeyo ndi mkaziyo amasanduka thupi limodzi? Paja kunalembedwa kuti, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.” 17 Koma amene amadzipereka kwa Ambuye, iyeyo ndi Ambuye amakhala mzimu umodzi.

18 Thawani dama. Machimo onse amene munthu amachita amakhala kunja kwa thupi lake, koma amene amachita machimo okhudza chigololo, amachimwira thupi lake lomwe. 19 Kodi simukudziwa kuti thupi lanu ndi Nyumba ya Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene mwalandira kuchokera kwa Mulungu? Inu simuli panokha ayi. 20 Ndinu ochita kugulidwa. Nʼchifukwa chake lemekezani Mulungu mʼthupi lanu.

Lawsuits Among Believers

If any of you has a dispute with another, do you dare to take it before the ungodly for judgment instead of before the Lord’s people?(A) Or do you not know that the Lord’s people will judge the world?(B) And if you are to judge the world, are you not competent to judge trivial cases? Do you not know that we will judge angels? How much more the things of this life! Therefore, if you have disputes about such matters, do you ask for a ruling from those whose way of life is scorned in the church? I say this to shame you.(C) Is it possible that there is nobody among you wise enough to judge a dispute between believers?(D) But instead, one brother(E) takes another to court—and this in front of unbelievers!(F)

The very fact that you have lawsuits among you means you have been completely defeated already. Why not rather be wronged? Why not rather be cheated?(G) Instead, you yourselves cheat and do wrong, and you do this to your brothers and sisters.(H) Or do you not know that wrongdoers will not inherit the kingdom of God?(I) Do not be deceived:(J) Neither the sexually immoral nor idolaters nor adulterers(K) nor men who have sex with men[a](L) 10 nor thieves nor the greedy nor drunkards nor slanderers nor swindlers(M) will inherit the kingdom of God. 11 And that is what some of you were.(N) But you were washed,(O) you were sanctified,(P) you were justified(Q) in the name of the Lord Jesus Christ and by the Spirit of our God.

Sexual Immorality

12 “I have the right to do anything,” you say—but not everything is beneficial.(R) “I have the right to do anything”—but I will not be mastered by anything. 13 You say, “Food for the stomach and the stomach for food, and God will destroy them both.”(S) The body, however, is not meant for sexual immorality but for the Lord,(T) and the Lord for the body. 14 By his power God raised the Lord from the dead,(U) and he will raise us also.(V) 15 Do you not know that your bodies are members of Christ himself?(W) Shall I then take the members of Christ and unite them with a prostitute? Never! 16 Do you not know that he who unites himself with a prostitute is one with her in body? For it is said, “The two will become one flesh.”[b](X) 17 But whoever is united with the Lord is one with him in spirit.[c](Y)

18 Flee from sexual immorality.(Z) All other sins a person commits are outside the body, but whoever sins sexually, sins against their own body.(AA) 19 Do you not know that your bodies are temples(AB) of the Holy Spirit, who is in you, whom you have received from God? You are not your own;(AC) 20 you were bought at a price.(AD) Therefore honor God with your bodies.(AE)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 6:9 The words men who have sex with men translate two Greek words that refer to the passive and active participants in homosexual acts.
  2. 1 Corinthians 6:16 Gen. 2:24
  3. 1 Corinthians 6:17 Or in the Spirit