Add parallel Print Page Options

16 Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti, “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo. Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati. Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”

Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.

Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.

Ela Mfumu ya Israeli

Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.

Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza. 10 Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.

11 Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake. 12 Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu, 13 chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.

14 Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Zimuri Mfumu ya Israeli

15 Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti. 16 Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli. 17 Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza. 18 Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa, 19 chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.

20 Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Omuri Mfumu ya Israeli

21 Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri. 22 Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.

23 Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza. 24 Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.

25 Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu. 26 Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.

27 Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 28 Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahabu Akhala Mfumu ya Israeli

29 Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22. 30 Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale. 31 Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza. 32 Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya. 33 Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.

34 Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

16 Then the word of the Lord came to Jehu(A) son of Hanani(B) concerning Baasha: “I lifted you up from the dust(C) and appointed you ruler(D) over my people Israel, but you followed the ways of Jeroboam and caused(E) my people Israel to sin and to arouse my anger by their sins. So I am about to wipe out Baasha(F) and his house,(G) and I will make your house like that of Jeroboam son of Nebat. Dogs(H) will eat those belonging to Baasha who die in the city, and birds(I) will feed on those who die in the country.”

As for the other events of Baasha’s reign, what he did and his achievements, are they not written in the book of the annals(J) of the kings of Israel? Baasha rested with his ancestors and was buried in Tirzah.(K) And Elah his son succeeded him as king.

Moreover, the word of the Lord came(L) through the prophet Jehu(M) son of Hanani to Baasha and his house, because of all the evil he had done in the eyes of the Lord, arousing his anger by the things he did, becoming like the house of Jeroboam—and also because he destroyed it.

Elah King of Israel

In the twenty-sixth year of Asa king of Judah, Elah son of Baasha became king of Israel, and he reigned in Tirzah two years.

Zimri, one of his officials, who had command of half his chariots, plotted against him. Elah was in Tirzah at the time, getting drunk(N) in the home of Arza, the palace administrator(O) at Tirzah. 10 Zimri came in, struck him down and killed him in the twenty-seventh year of Asa king of Judah. Then he succeeded him as king.(P)

11 As soon as he began to reign and was seated on the throne, he killed off Baasha’s whole family.(Q) He did not spare a single male, whether relative or friend. 12 So Zimri destroyed the whole family of Baasha, in accordance with the word of the Lord spoken against Baasha through the prophet Jehu— 13 because of all the sins Baasha and his son Elah had committed and had caused Israel to commit, so that they aroused the anger of the Lord, the God of Israel, by their worthless idols.(R)

14 As for the other events of Elah’s reign, and all he did, are they not written in the book of the annals of the kings of Israel?

Zimri King of Israel

15 In the twenty-seventh year of Asa king of Judah, Zimri reigned in Tirzah seven days. The army was encamped near Gibbethon,(S) a Philistine town. 16 When the Israelites in the camp heard that Zimri had plotted against the king and murdered him, they proclaimed Omri, the commander of the army, king over Israel that very day there in the camp. 17 Then Omri and all the Israelites with him withdrew from Gibbethon and laid siege to Tirzah. 18 When Zimri saw that the city was taken, he went into the citadel of the royal palace and set the palace on fire around him. So he died, 19 because of the sins he had committed, doing evil in the eyes of the Lord and following the ways of Jeroboam and committing the same sin Jeroboam had caused Israel to commit.

20 As for the other events of Zimri’s reign, and the rebellion he carried out, are they not written in the book of the annals of the kings of Israel?

Omri King of Israel

21 Then the people of Israel were split into two factions; half supported Tibni son of Ginath for king, and the other half supported Omri. 22 But Omri’s followers proved stronger than those of Tibni son of Ginath. So Tibni died and Omri became king.

23 In the thirty-first year of Asa king of Judah, Omri became king of Israel, and he reigned twelve years, six of them in Tirzah.(T) 24 He bought the hill of Samaria from Shemer for two talents[a] of silver and built a city on the hill, calling it Samaria,(U) after Shemer, the name of the former owner of the hill.

25 But Omri did evil(V) in the eyes of the Lord and sinned more than all those before him. 26 He followed completely the ways of Jeroboam son of Nebat, committing the same sin Jeroboam had caused(W) Israel to commit, so that they aroused the anger of the Lord, the God of Israel, by their worthless idols.(X)

27 As for the other events of Omri’s reign, what he did and the things he achieved, are they not written in the book of the annals of the kings of Israel? 28 Omri rested with his ancestors and was buried in Samaria.(Y) And Ahab his son succeeded him as king.

Ahab Becomes King of Israel

29 In the thirty-eighth year of Asa king of Judah, Ahab son of Omri became king of Israel, and he reigned in Samaria over Israel twenty-two years. 30 Ahab son of Omri did more(Z) evil in the eyes of the Lord than any of those before him. 31 He not only considered it trivial to commit the sins of Jeroboam son of Nebat, but he also married(AA) Jezebel daughter(AB) of Ethbaal king of the Sidonians, and began to serve Baal(AC) and worship him. 32 He set up an altar(AD) for Baal in the temple(AE) of Baal that he built in Samaria. 33 Ahab also made an Asherah pole(AF) and did more(AG) to arouse the anger of the Lord, the God of Israel, than did all the kings of Israel before him.

34 In Ahab’s time, Hiel of Bethel rebuilt Jericho. He laid its foundations at the cost of his firstborn son Abiram, and he set up its gates at the cost of his youngest son Segub, in accordance with the word of the Lord spoken by Joshua son of Nun.(AH)

Footnotes

  1. 1 Kings 16:24 That is, about 150 pounds or about 68 kilograms