Add parallel Print Page Options

Eliya Athawira ku Phiri la Horebu

19 Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga. Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”

Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko, ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.” Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko.

Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.” Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.

Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.” Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu. Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko.

Ambuye Aonekera Eliya

Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”

10 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”

11 Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.”

Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho. 12 Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi. 13 Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga.

Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”

14 Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”

15 Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu. 16 Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako. 17 Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu. 18 Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”

Kuyitanidwa kwa Elisa

19 Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake. 20 Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.”

Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”

21 Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.

Elijah Flees to Horeb

19 Now Ahab told Jezebel(A) everything Elijah had done and how he had killed(B) all the prophets with the sword. So Jezebel sent a messenger to Elijah to say, “May the gods deal with me, be it ever so severely,(C) if by this time tomorrow I do not make your life like that of one of them.”(D)

Elijah was afraid[a] and ran(E) for his life.(F) When he came to Beersheba(G) in Judah, he left his servant there, while he himself went a day’s journey into the wilderness. He came to a broom bush,(H) sat down under it and prayed that he might die. “I have had enough, Lord,” he said. “Take my life;(I) I am no better than my ancestors.” Then he lay down under the bush and fell asleep.(J)

All at once an angel(K) touched him and said, “Get up and eat.” He looked around, and there by his head was some bread baked over hot coals, and a jar of water. He ate and drank and then lay down again.

The angel of the Lord came back a second time and touched him and said, “Get up and eat, for the journey is too much for you.” So he got up and ate and drank. Strengthened by that food, he traveled forty(L) days and forty nights until he reached Horeb,(M) the mountain of God. There he went into a cave(N) and spent the night.

The Lord Appears to Elijah

And the word of the Lord came to him: “What are you doing here, Elijah?”(O)

10 He replied, “I have been very zealous(P) for the Lord God Almighty. The Israelites have rejected your covenant,(Q) torn down your altars,(R) and put your prophets to death with the sword. I am the only one left,(S) and now they are trying to kill me too.”

11 The Lord said, “Go out and stand on the mountain(T) in the presence of the Lord, for the Lord is about to pass by.”(U)

Then a great and powerful wind(V) tore the mountains apart and shattered(W) the rocks before the Lord, but the Lord was not in the wind. After the wind there was an earthquake, but the Lord was not in the earthquake. 12 After the earthquake came a fire,(X) but the Lord was not in the fire. And after the fire came a gentle whisper.(Y) 13 When Elijah heard it, he pulled his cloak over his face(Z) and went out and stood at the mouth of the cave.

Then a voice said to him, “What are you doing here, Elijah?”

14 He replied, “I have been very zealous for the Lord God Almighty. The Israelites have rejected your covenant, torn down your altars, and put your prophets to death with the sword. I am the only one left,(AA) and now they are trying to kill me too.”

15 The Lord said to him, “Go back the way you came, and go to the Desert of Damascus. When you get there, anoint Hazael(AB) king over Aram. 16 Also, anoint(AC) Jehu son of Nimshi king over Israel, and anoint Elisha(AD) son of Shaphat from Abel Meholah(AE) to succeed you as prophet. 17 Jehu will put to death any who escape the sword of Hazael,(AF) and Elisha will put to death any who escape the sword of Jehu.(AG) 18 Yet I reserve(AH) seven thousand in Israel—all whose knees have not bowed down to Baal and whose mouths have not kissed(AI) him.”

The Call of Elisha

19 So Elijah went from there and found Elisha son of Shaphat. He was plowing with twelve yoke of oxen, and he himself was driving the twelfth pair. Elijah went up to him and threw his cloak(AJ) around him. 20 Elisha then left his oxen and ran after Elijah. “Let me kiss my father and mother goodbye,”(AK) he said, “and then I will come with you.”

“Go back,” Elijah replied. “What have I done to you?”

21 So Elisha left him and went back. He took his yoke of oxen(AL) and slaughtered them. He burned the plowing equipment to cook the meat and gave it to the people, and they ate. Then he set out to follow Elijah and became his servant.(AM)

Footnotes

  1. 1 Kings 19:3 Or Elijah saw