Add parallel Print Page Options

Ankhondo Amene Anali ndi Davide, Sauli Asanafe

12 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo. Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.

Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti, ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi, Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi; Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora; ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.

Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.

Mtsogoleri wawo anali Ezeri,

wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,

10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,

11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,

12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,

13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.

14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000. 15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.

16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake. 17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”

18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati:

“Inu Davide, ife ndife anu!
    Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese!
Kupambana, Kupambana kwa inu,
    ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani
        pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.”

Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.

19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).” 20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase. 21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo. 22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.

Enanso Abwera kwa Davide ku Hebroni

23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:

24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;

25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;

26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600, 27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700, 28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;

29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;

30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;

31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;

32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.

33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.

34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;

35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.

36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;

37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.

38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu. 39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya. 40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

Warriors Join David

12 These were the men who came to David at Ziklag,(A) while he was banished from the presence of Saul son of Kish (they were among the warriors who helped him in battle; they were armed with bows and were able to shoot arrows or to sling stones right-handed or left-handed;(B) they were relatives of Saul(C) from the tribe of Benjamin):

Ahiezer their chief and Joash the sons of Shemaah the Gibeathite; Jeziel and Pelet the sons of Azmaveth; Berakah, Jehu the Anathothite, and Ishmaiah the Gibeonite, a mighty warrior among the Thirty, who was a leader of the Thirty; Jeremiah, Jahaziel, Johanan, Jozabad the Gederathite,[a](D) Eluzai, Jerimoth, Bealiah, Shemariah and Shephatiah the Haruphite; Elkanah, Ishiah, Azarel, Joezer and Jashobeam the Korahites; and Joelah and Zebadiah the sons of Jeroham from Gedor.(E)

Some Gadites(F) defected to David at his stronghold in the wilderness. They were brave warriors, ready for battle and able to handle the shield and spear. Their faces were the faces of lions,(G) and they were as swift as gazelles(H) in the mountains.

Ezer was the chief,

Obadiah the second in command, Eliab the third,

10 Mishmannah the fourth, Jeremiah the fifth,

11 Attai the sixth, Eliel the seventh,

12 Johanan the eighth, Elzabad the ninth,

13 Jeremiah the tenth and Makbannai the eleventh.

14 These Gadites were army commanders; the least was a match for a hundred,(I) and the greatest for a thousand.(J) 15 It was they who crossed the Jordan in the first month when it was overflowing all its banks,(K) and they put to flight everyone living in the valleys, to the east and to the west.

16 Other Benjamites(L) and some men from Judah also came to David in his stronghold. 17 David went out to meet them and said to them, “If you have come to me in peace to help me, I am ready for you to join me. But if you have come to betray me to my enemies when my hands are free from violence, may the God of our ancestors see it and judge you.”

18 Then the Spirit(M) came on Amasai,(N) chief of the Thirty, and he said:

“We are yours, David!
    We are with you, son of Jesse!
Success,(O) success to you,
    and success to those who help you,
        for your God will help you.”

So David received them and made them leaders of his raiding bands.

19 Some of the tribe of Manasseh defected to David when he went with the Philistines to fight against Saul. (He and his men did not help the Philistines because, after consultation, their rulers sent him away. They said, “It will cost us our heads if he deserts to his master Saul.”)(P) 20 When David went to Ziklag,(Q) these were the men of Manasseh who defected to him: Adnah, Jozabad, Jediael, Michael, Jozabad, Elihu and Zillethai, leaders of units of a thousand in Manasseh. 21 They helped David against raiding bands, for all of them were brave warriors, and they were commanders in his army. 22 Day after day men came to help David, until he had a great army, like the army of God.[b]

Others Join David at Hebron

23 These are the numbers of the men armed for battle who came to David at Hebron(R) to turn(S) Saul’s kingdom over to him, as the Lord had said:(T)

24 from Judah, carrying shield and spear—6,800 armed for battle;

25 from Simeon, warriors ready for battle—7,100;

26 from Levi—4,600, 27 including Jehoiada, leader of the family of Aaron, with 3,700 men, 28 and Zadok,(U) a brave young warrior, with 22 officers from his family;

29 from Benjamin,(V) Saul’s tribe—3,000, most(W) of whom had remained loyal to Saul’s house until then;

30 from Ephraim, brave warriors, famous in their own clans—20,800;

31 from half the tribe of Manasseh, designated by name to come and make David king—18,000;

32 from Issachar, men who understood the times and knew what Israel should do(X)—200 chiefs, with all their relatives under their command;

33 from Zebulun, experienced soldiers prepared for battle with every type of weapon, to help David with undivided loyalty—50,000;

34 from Naphtali—1,000 officers, together with 37,000 men carrying shields and spears;

35 from Dan, ready for battle—28,600;

36 from Asher, experienced soldiers prepared for battle—40,000;

37 and from east of the Jordan, from Reuben, Gad and the half-tribe of Manasseh, armed with every type of weapon—120,000.

38 All these were fighting men who volunteered to serve in the ranks. They came to Hebron fully determined to make David king over all Israel.(Y) All the rest of the Israelites were also of one mind to make David king. 39 The men spent three days there with David, eating and drinking,(Z) for their families had supplied provisions for them. 40 Also, their neighbors from as far away as Issachar, Zebulun and Naphtali came bringing food on donkeys, camels, mules and oxen. There were plentiful supplies(AA) of flour, fig cakes, raisin(AB) cakes, wine, olive oil, cattle and sheep, for there was joy(AC) in Israel.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 12:4 In Hebrew texts the second half of this verse (Jeremiah … Gederathite) is numbered 12:5, and 12:5-40 is numbered 12:6-41.
  2. 1 Chronicles 12:22 Or a great and mighty army