Add parallel Print Page Options

16 Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu. Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova. Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.

Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli. Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga, ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.

Nyimbo Yotamanda ya Davide

Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:

Yamikani Yehova, itanani dzina lake;
    lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando;
    nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Nyadirani dzina lake loyera;
    ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;
    funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita,
    zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake,
    inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.

14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;
    chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse,
    mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 pangano limene anachita ndi Abrahamu,
    lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo,
    kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 “Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani
    monga cholowa chimene udzachilandira.”

19 Ali anthu owerengeka,
    ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,
    ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze;
    chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 “Musakhudze odzozedwa anga;
    musawachitire choyipa aneneri anga.”

23 Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi;
    lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse,
    ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
    Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake,
    koma Yehova analenga kumwamba.
27 Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake;
    mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina,
    perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29     perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake.
Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake;
    pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi!
    Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere;
    anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
    minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba,
    idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova,
    pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;
    chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,
    mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina,
kuti tiyamike dzina lanu loyera,
    kuti tikutamandeni.”
36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli,
    kuyambira muyaya mpaka muyaya.

Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”

37 Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse. 38 Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.

39 Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni 40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli. 41 Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.” 42 Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.

43 Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

Ministering Before the Ark(A)(B)(C)

16 They brought the ark of God and set it inside the tent that David had pitched(D) for it, and they presented burnt offerings and fellowship offerings before God. After David had finished sacrificing the burnt offerings and fellowship offerings, he blessed(E) the people in the name of the Lord. Then he gave a loaf of bread, a cake of dates and a cake of raisins(F) to each Israelite man and woman.

He appointed some of the Levites to minister(G) before the ark of the Lord, to extol,[a] thank, and praise the Lord, the God of Israel: Asaph was the chief, and next to him in rank were Zechariah, then Jaaziel,[b] Shemiramoth, Jehiel, Mattithiah, Eliab, Benaiah, Obed-Edom and Jeiel. They were to play the lyres and harps, Asaph was to sound the cymbals, and Benaiah and Jahaziel the priests were to blow the trumpets regularly before the ark of the covenant of God.

That day David first appointed Asaph and his associates to give praise(H) to the Lord in this manner:

Give praise(I) to the Lord, proclaim his name;
    make known among the nations(J) what he has done.
Sing to him, sing praise(K) to him;
    tell of all his wonderful acts.
10 Glory in his holy name;(L)
    let the hearts of those who seek the Lord rejoice.
11 Look to the Lord and his strength;
    seek(M) his face always.

12 Remember(N) the wonders(O) he has done,
    his miracles,(P) and the judgments he pronounced,
13 you his servants, the descendants of Israel,
    his chosen ones, the children of Jacob.
14 He is the Lord our God;
    his judgments(Q) are in all the earth.

15 He remembers[c](R) his covenant forever,
    the promise he made, for a thousand generations,
16 the covenant(S) he made with Abraham,
    the oath he swore to Isaac.
17 He confirmed it to Jacob(T) as a decree,
    to Israel as an everlasting covenant:
18 “To you I will give the land of Canaan(U)
    as the portion you will inherit.”

19 When they were but few in number,(V)
    few indeed, and strangers in it,
20 they[d] wandered(W) from nation to nation,
    from one kingdom to another.
21 He allowed no one to oppress them;
    for their sake he rebuked kings:(X)
22 “Do not touch my anointed ones;
    do my prophets(Y) no harm.”

23 Sing to the Lord, all the earth;
    proclaim his salvation day after day.
24 Declare his glory(Z) among the nations,
    his marvelous deeds among all peoples.

25 For great is the Lord and most worthy of praise;(AA)
    he is to be feared(AB) above all gods.(AC)
26 For all the gods of the nations are idols,
    but the Lord made the heavens.(AD)
27 Splendor and majesty are before him;
    strength and joy are in his dwelling place.

28 Ascribe to the Lord, all you families of nations,
    ascribe to the Lord glory and strength.(AE)
29 Ascribe to the Lord the glory due his name;(AF)
    bring an offering and come before him.
Worship the Lord in the splendor of his[e] holiness.(AG)
30     Tremble(AH) before him, all the earth!
    The world is firmly established; it cannot be moved.(AI)

31 Let the heavens rejoice, let the earth be glad;(AJ)
    let them say among the nations, “The Lord reigns!(AK)
32 Let the sea resound, and all that is in it;(AL)
    let the fields be jubilant, and everything in them!
33 Let the trees(AM) of the forest sing,
    let them sing for joy before the Lord,
    for he comes to judge(AN) the earth.

34 Give thanks(AO) to the Lord, for he is good;(AP)
    his love endures forever.(AQ)
35 Cry out, “Save us, God our Savior;(AR)
    gather us and deliver us from the nations,
that we may give thanks to your holy name,
    and glory in your praise.”
36 Praise be to the Lord, the God of Israel,(AS)
    from everlasting to everlasting.

Then all the people said “Amen” and “Praise the Lord.”

37 David left Asaph and his associates before the ark of the covenant of the Lord to minister there regularly, according to each day’s requirements.(AT) 38 He also left Obed-Edom(AU) and his sixty-eight associates to minister with them. Obed-Edom son of Jeduthun, and also Hosah,(AV) were gatekeepers.

39 David left Zadok(AW) the priest and his fellow priests before the tabernacle of the Lord at the high place in Gibeon(AX) 40 to present burnt offerings to the Lord on the altar of burnt offering regularly, morning and evening, in accordance with everything written in the Law(AY) of the Lord, which he had given Israel. 41 With them were Heman(AZ) and Jeduthun and the rest of those chosen and designated by name to give thanks to the Lord, “for his love endures forever.” 42 Heman and Jeduthun were responsible for the sounding of the trumpets and cymbals and for the playing of the other instruments for sacred song.(BA) The sons of Jeduthun(BB) were stationed at the gate.

43 Then all the people left, each for their own home, and David returned home to bless his family.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 16:4 Or petition; or invoke
  2. 1 Chronicles 16:5 See 15:18,20; Hebrew Jeiel, possibly another name for Jaaziel.
  3. 1 Chronicles 16:15 Some Septuagint manuscripts (see also Psalm 105:8); Hebrew Remember
  4. 1 Chronicles 16:20 One Hebrew manuscript, Septuagint and Vulgate (see also Psalm 105:12); most Hebrew manuscripts inherit, / 19 though you are but few in number, / few indeed, and strangers in it.” / 20 They
  5. 1 Chronicles 16:29 Or Lord with the splendor of