Add parallel Print Page Options

Davide Awerenga Ankhondo Ake

21 Satana anafuna kuvutitsa Aisraeli choncho anawutsa mtima wa Davide kuti awerenge Aisraeli. Choncho Davide anati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, “Pitani mukawerenge Aisraeli kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani. Ndipo mudzandiwuze kuti ndidziwe chiwerengero chawo.”

Yowabu anayankha kuti, “Yehova achulukitse ankhondo ake kukhala miyandamiyanda. Mbuye wanga mfumu, kodi anthu onsewa sali pansi panu? Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukufuna kuchita zimenezi? Nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwitsa Israeli?”

Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu, kotero Yowabu anapita mu Israeli monse ndipo kenaka anabwera ku Yerusalemu. Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda.

Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira. Lamulo limeneli silinakomerenso Mulungu. Kotero Iye analanga Israeli.

Choncho Davide anati kwa Mulungu, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”

Yehova anati kwa Gadi, mlosi wa Davide, 10 “Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’ ”

11 Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa Iye, “Yehova akuti, ‘Musankhepo chimene mungakonde kuti chichitike: 12 mʼdziko mukhale njala zaka zitatu, mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu, akukukanthani ndi lupanga la Yehova, kapena mʼdziko mukhale mliri kwa masiku atatu, mngelo wa Yehova akuwononga Israeli yense.’ Ndipo tsono ganizirani bwino chomwe ndikamuyankhe amene wandituma.”

13 Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ine andilange ndi Yehova, pakuti chifundo chake ndi chachikulu kwambiri; koma ndisalangidwe ndi anthu.”

14 Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000. 15 Ndipo Mulungu anatumiza mngelo kuti awononge Yerusalemu. Koma pamene mngeloyo amachita zimenezi, Yehova anaona ndipo anavutika mu mtima chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.

16 Davide anakweza maso ake ndipo anaona mngelo wa Yehova atayima pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, mʼdzanja lake muli lupanga lotambalitsa kuloza ku Yerusalemu. Ndipo Davide ndi akuluakulu, atavala ziguduli, anadzigwetsa pansi chafufumimba.

17 Davide anati kwa Mulungu, “Kodi si ine amene ndinalamula kuti ankhondo awerengedwe? Ine mʼbusa ndi amene ndachimwa, ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Inu Yehova Mulungu wanga, langani ineyo pamodzi ndi banja langa, koma musalole kuti mliriwu ukhale pa anthu anuwa.”

18 Pamenepo mngelo wa Yehova analamula Gadi kuti awuze Davide kuti akamange guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi. 19 Ndipo Davide anapita pomvera mawu amene Gadi ananena mʼdzina la Yehova.

20 Pamene Arauna ankapuntha tirigu, anatembenuka ndipo anaona mngelo ndipo ana ake anayi aamuna amene anali naye anabisala. 21 Davide anayandikira, ndipo Arauna atayangʼana ndi kumuona, anachoka popunthira tirigupo ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi pamaso pa Davide.

22 Davide anati kwa Arauna, “Undipatse malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe, kuti mliri uli pa anthuwa usiye. Undigulitse ine pa mtengo woyenera ndithu.”

23 Arauna anati kwa Davide, “Tengani! Mbuye wanga mfumu achite chomukomera. Taonani ine ndidzapereka ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, zopunthira tirigu zidzakhala nkhuni ndipo tiriguyu adzakhala chopereka chachakudya. Ndidzapereka zonsezi.”

24 Koma mfumu Davide inayankha Arauna kuti, “Ayi, ine ndikuti ndipereka mtengo wathunthu. Sindingatenge chinthu chako ndi kuchipereka kwa Yehova, kapena kupereka nsembe imene sindinayigule.”

25 Choncho Davide analipira Arauna masekeli agolide 600 chifukwa cha malowo. 26 Davide anamangira Yehova guwa lansembe pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Iye anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anayankha potumiza moto pa guwa lansembe zopsereza kuchokera kumwamba.

27 Tsono Yehova anayankhula kwa mngelo, ndipo analowetsa lupanga lake mʼchimake. 28 Pa nthawi imeneyo, Davide ataona kuti Yehova wamuyankha pa malo opunthira tirigu a Arauna Myebusi, anapereka nsembe pamenepo. 29 Tenti ya Yehova imene Mose anapanga mʼchipululu, ndi guwa lansembe zopsereza pa nthawi imeneyi zinali pa phiri ku Gibiyoni. 30 Koma Davide sanathe kupita kumeneko kuti akapemphere pamaso pa Yehova, chifukwa amaopa lupanga la mngelo wa Yehova.

David Counts the Fighting Men(A)

21 Satan(B) rose up against Israel and incited David to take a census(C) of Israel. So David said to Joab and the commanders of the troops, “Go and count(D) the Israelites from Beersheba to Dan. Then report back to me so that I may know how many there are.”

But Joab replied, “May the Lord multiply his troops a hundred times over.(E) My lord the king, are they not all my lord’s subjects? Why does my lord want to do this? Why should he bring guilt on Israel?”

The king’s word, however, overruled Joab; so Joab left and went throughout Israel and then came back to Jerusalem. Joab reported the number of the fighting men to David: In all Israel(F) there were one million one hundred thousand men who could handle a sword, including four hundred and seventy thousand in Judah.

But Joab did not include Levi and Benjamin in the numbering, because the king’s command was repulsive to him. This command was also evil in the sight of God; so he punished Israel.

Then David said to God, “I have sinned greatly by doing this. Now, I beg you, take away the guilt of your servant. I have done a very foolish thing.”

The Lord said to Gad,(G) David’s seer,(H) 10 “Go and tell David, ‘This is what the Lord says: I am giving you three options. Choose one of them for me to carry out against you.’”

11 So Gad went to David and said to him, “This is what the Lord says: ‘Take your choice: 12 three years of famine,(I) three months of being swept away[a] before your enemies, with their swords overtaking you, or three days of the sword(J) of the Lord(K)—days of plague in the land, with the angel of the Lord ravaging every part of Israel.’ Now then, decide how I should answer the one who sent me.”

13 David said to Gad, “I am in deep distress. Let me fall into the hands of the Lord, for his mercy(L) is very great; but do not let me fall into human hands.”

14 So the Lord sent a plague on Israel, and seventy thousand men of Israel fell dead.(M) 15 And God sent an angel(N) to destroy Jerusalem.(O) But as the angel was doing so, the Lord saw it and relented(P) concerning the disaster and said to the angel who was destroying(Q) the people, “Enough! Withdraw your hand.” The angel of the Lord was then standing at the threshing floor of Araunah[b] the Jebusite.

16 David looked up and saw the angel of the Lord standing between heaven and earth, with a drawn sword in his hand extended over Jerusalem. Then David and the elders, clothed in sackcloth, fell facedown.(R)

17 David said to God, “Was it not I who ordered the fighting men to be counted? I, the shepherd,[c] have sinned and done wrong. These are but sheep.(S) What have they done? Lord my God, let your hand fall on me and my family,(T) but do not let this plague remain on your people.”

David Builds an Altar

18 Then the angel of the Lord ordered Gad to tell David to go up and build an altar to the Lord on the threshing floor(U) of Araunah the Jebusite. 19 So David went up in obedience to the word that Gad had spoken in the name of the Lord.

20 While Araunah was threshing wheat,(V) he turned and saw the angel; his four sons who were with him hid themselves. 21 Then David approached, and when Araunah looked and saw him, he left the threshing floor and bowed down before David with his face to the ground.

22 David said to him, “Let me have the site of your threshing floor so I can build an altar to the Lord, that the plague on the people may be stopped. Sell it to me at the full price.”

23 Araunah said to David, “Take it! Let my lord the king do whatever pleases him. Look, I will give the oxen for the burnt offerings, the threshing sledges for the wood, and the wheat for the grain offering. I will give all this.”

24 But King David replied to Araunah, “No, I insist on paying the full price. I will not take for the Lord what is yours, or sacrifice a burnt offering that costs me nothing.”

25 So David paid Araunah six hundred shekels[d] of gold for the site. 26 David built an altar to the Lord there and sacrificed burnt offerings and fellowship offerings. He called on the Lord, and the Lord answered him with fire(W) from heaven on the altar of burnt offering.

27 Then the Lord spoke to the angel, and he put his sword back into its sheath. 28 At that time, when David saw that the Lord had answered him on the threshing floor of Araunah the Jebusite, he offered sacrifices there. 29 The tabernacle of the Lord, which Moses had made in the wilderness, and the altar of burnt offering were at that time on the high place at Gibeon.(X) 30 But David could not go before it to inquire of God, because he was afraid of the sword of the angel of the Lord.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 21:12 Hebrew; Septuagint and Vulgate (see also 2 Samuel 24:13) of fleeing
  2. 1 Chronicles 21:15 Hebrew Ornan, a variant of Araunah; also in verses 18-28
  3. 1 Chronicles 21:17 Probable reading of the original Hebrew text (see 2 Samuel 24:17 and note); Masoretic Text does not have the shepherd.
  4. 1 Chronicles 21:25 That is, about 15 pounds or about 6.9 kilograms