Add parallel Print Page Options

22 Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu. Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza. Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.

Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.

Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli. Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga. Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga. Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake. 10 Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’ ”

11 “Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero. 12 Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako. 13 Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.

14 “Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi. 15 Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana, 16 zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”

17 Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake. 18 Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake. 19 Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

22 Then David said, “The house of the Lord God(A) is to be here, and also the altar of burnt offering for Israel.”

Preparations for the Temple

So David gave orders to assemble the foreigners(B) residing in Israel, and from among them he appointed stonecutters(C) to prepare dressed stone for building the house of God. He provided a large amount of iron to make nails for the doors of the gateways and for the fittings, and more bronze than could be weighed.(D) He also provided more cedar logs(E) than could be counted, for the Sidonians and Tyrians had brought large numbers of them to David.

David said, “My son Solomon is young(F) and inexperienced, and the house to be built for the Lord should be of great magnificence and fame and splendor(G) in the sight of all the nations. Therefore I will make preparations for it.” So David made extensive preparations before his death.

Then he called for his son Solomon and charged him to build(H) a house for the Lord, the God of Israel. David said to Solomon: “My son, I had it in my heart(I) to build(J) a house for the Name(K) of the Lord my God. But this word of the Lord came to me: ‘You have shed much blood and have fought many wars.(L) You are not to build a house for my Name,(M) because you have shed much blood on the earth in my sight. But you will have a son who will be a man of peace(N) and rest,(O) and I will give him rest from all his enemies on every side. His name will be Solomon,[a](P) and I will grant Israel peace and quiet(Q) during his reign. 10 He is the one who will build a house for my Name.(R) He will be my son,(S) and I will be his father. And I will establish(T) the throne of his kingdom over Israel forever.’(U)

11 “Now, my son, the Lord be with(V) you, and may you have success and build the house of the Lord your God, as he said you would. 12 May the Lord give you discretion and understanding(W) when he puts you in command over Israel, so that you may keep the law of the Lord your God. 13 Then you will have success(X) if you are careful to observe the decrees and laws(Y) that the Lord gave Moses for Israel. Be strong and courageous.(Z) Do not be afraid or discouraged.

14 “I have taken great pains to provide for the temple of the Lord a hundred thousand talents[b] of gold, a million talents[c] of silver, quantities of bronze and iron too great to be weighed, and wood and stone. And you may add to them.(AA) 15 You have many workers: stonecutters, masons and carpenters,(AB) as well as those skilled in every kind of work 16 in gold and silver, bronze and iron—craftsmen(AC) beyond number. Now begin the work, and the Lord be with you.”

17 Then David ordered(AD) all the leaders of Israel to help his son Solomon. 18 He said to them, “Is not the Lord your God with you? And has he not granted you rest(AE) on every side?(AF) For he has given the inhabitants of the land into my hands, and the land is subject to the Lord and to his people. 19 Now devote your heart and soul to seeking the Lord your God.(AG) Begin to build the sanctuary of the Lord God, so that you may bring the ark of the covenant of the Lord and the sacred articles belonging to God into the temple that will be built for the Name of the Lord.”

Footnotes

  1. 1 Chronicles 22:9 Solomon sounds like and may be derived from the Hebrew for peace.
  2. 1 Chronicles 22:14 That is, about 3,750 tons or about 3,400 metric tons
  3. 1 Chronicles 22:14 That is, about 37,500 tons or about 34,000 metric tons