Add parallel Print Page Options

Fuko la Levi

23 Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.

Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi. Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000. Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza. Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”

Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.

Banja la Geresoni

Ana a Geresoni:

Ladani ndi Simei.

Ana a Ladani:

Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.

Ana a Simei:

Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu.

Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.

10 Ndipo ana a Simei anali:

Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya.

Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.

11 Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.

Banja la Kohati

12 Ana a Kohati:

Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.

13 Ana a Amramu:

Aaroni ndi Mose.

Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya. 14 Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.

15 Ana a Mose:

Geresomu ndi Eliezara.

16 Zidzukulu za Geresomu:

Mtsogoleri anali Subaeli.

17 Zidzukulu za Eliezara:

Mtsogoleri anali Rehabiya.

Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.

18 Ana a Izihari:

Mtsogoleri anali Selomiti.

19 Ana a Hebroni:

Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.

20 Ana a Uzieli:

Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.

Banja la Merari

21 Ana a Merari:

Mahili ndi Musi.

Ana a Mahili:

Eliezara ndi Kisi.

22 Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.

23 Ana a Musi:

Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.

24 Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova. 25 Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya, 26 sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.” 27 Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.

28 Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu. 29 Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake. 30 Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo, 31 ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.

32 Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.

The Levites

23 When David was old and full of years, he made his son Solomon(A) king over Israel.(B)

He also gathered together all the leaders of Israel, as well as the priests and Levites. The Levites thirty years old or more(C) were counted,(D) and the total number of men was thirty-eight thousand.(E) David said, “Of these, twenty-four thousand are to be in charge(F) of the work(G) of the temple of the Lord and six thousand are to be officials and judges.(H) Four thousand are to be gatekeepers and four thousand are to praise the Lord with the musical instruments(I) I have provided for that purpose.”(J)

David separated(K) the Levites into divisions corresponding to the sons of Levi:(L) Gershon, Kohath and Merari.

Gershonites

Belonging to the Gershonites:(M)

Ladan and Shimei.

The sons of Ladan:

Jehiel the first, Zetham and Joel—three in all.

The sons of Shimei:

Shelomoth, Haziel and Haran—three in all.

These were the heads of the families of Ladan.

10 And the sons of Shimei:

Jahath, Ziza,[a] Jeush and Beriah.

These were the sons of Shimei—four in all.

11 Jahath was the first and Ziza the second, but Jeush and Beriah did not have many sons; so they were counted as one family with one assignment.

Kohathites

12 The sons of Kohath:(N)

Amram, Izhar, Hebron and Uzziel—four in all.

13 The sons of Amram:(O)

Aaron and Moses.

Aaron was set apart,(P) he and his descendants forever, to consecrate the most holy things, to offer sacrifices before the Lord, to minister(Q) before him and to pronounce blessings(R) in his name forever. 14 The sons of Moses the man(S) of God were counted as part of the tribe of Levi.

15 The sons of Moses:

Gershom and Eliezer.(T)

16 The descendants of Gershom:(U)

Shubael was the first.

17 The descendants of Eliezer:

Rehabiah(V) was the first.

Eliezer had no other sons, but the sons of Rehabiah were very numerous.

18 The sons of Izhar:

Shelomith(W) was the first.

19 The sons of Hebron:(X)

Jeriah the first, Amariah the second, Jahaziel the third and Jekameam the fourth.

20 The sons of Uzziel:

Micah the first and Ishiah the second.

Merarites

21 The sons of Merari:(Y)

Mahli and Mushi.(Z)

The sons of Mahli:

Eleazar and Kish.

22 Eleazar died without having sons: he had only daughters. Their cousins, the sons of Kish, married them.(AA)

23 The sons of Mushi:

Mahli, Eder and Jerimoth—three in all.

24 These were the descendants of Levi by their families—the heads of families as they were registered under their names and counted individually, that is, the workers twenty years old or more(AB) who served in the temple of the Lord. 25 For David had said, “Since the Lord, the God of Israel, has granted rest(AC) to his people and has come to dwell in Jerusalem forever, 26 the Levites no longer need to carry the tabernacle or any of the articles used in its service.”(AD) 27 According to the last instructions of David, the Levites were counted from those twenty years old or more.

28 The duty of the Levites was to help Aaron’s descendants in the service of the temple of the Lord: to be in charge of the courtyards, the side rooms, the purification(AE) of all sacred things and the performance of other duties at the house of God. 29 They were in charge of the bread set out on the table,(AF) the special flour for the grain offerings,(AG) the thin loaves made without yeast, the baking and the mixing, and all measurements of quantity and size.(AH) 30 They were also to stand every morning to thank and praise the Lord. They were to do the same in the evening(AI) 31 and whenever burnt offerings were presented to the Lord on the Sabbaths, at the New Moon(AJ) feasts and at the appointed festivals.(AK) They were to serve before the Lord regularly in the proper number and in the way prescribed for them.

32 And so the Levites(AL) carried out their responsibilities for the tent of meeting,(AM) for the Holy Place and, under their relatives the descendants of Aaron, for the service of the temple of the Lord.(AN)

Footnotes

  1. 1 Chronicles 23:10 One Hebrew manuscript, Septuagint and Vulgate (see also verse 11); most Hebrew manuscripts Zina