Add parallel Print Page Options

Alonda a pa Zipata

26 Magulu a alonda a pa zipata:

Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.

Meselemiya anali ndi ana awa:

woyamba Zekariya,

wachiwiri Yediaeli,

wachitatu Zebadiya,

wachinayi Yatinieli,

wachisanu Elamu,

wachisanu ndi chimodzi Yehohanani,

ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.

Obedi-Edomu analinso ndi ana awa:

woyamba Semaya,

wachiwiri Yehozabadi,

wachitatu Yowa,

wachinayi Sakara,

wachisanu Netaneli,

wachisanu ndi chimodzi Amieli,

wachisanu ndi chiwiri Isakara

ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi.

(Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).

Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu. Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu. Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.

Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.

10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri), 11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.

12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo. 13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.

14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye. 15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake. 16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa.

Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake: 17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu. 18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.

19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.

Asungichuma ndi Akuluakulu Ena

20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.

21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli, 22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.

23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:

24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma. 25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake. 26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena. 27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova. 28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.

29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.

30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani. 31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi. 32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.

The Gatekeepers

26 The divisions of the gatekeepers:(A)

From the Korahites: Meshelemiah son of Kore, one of the sons of Asaph.

Meshelemiah had sons:

Zechariah(B) the firstborn,

Jediael the second,

Zebadiah the third,

Jathniel the fourth,

Elam the fifth,

Jehohanan the sixth

and Eliehoenai the seventh.

Obed-Edom also had sons:

Shemaiah the firstborn,

Jehozabad the second,

Joah the third,

Sakar the fourth,

Nethanel the fifth,

Ammiel the sixth,

Issachar the seventh

and Peullethai the eighth.

(For God had blessed Obed-Edom.(C))

Obed-Edom’s son Shemaiah also had sons, who were leaders in their father’s family because they were very capable men. The sons of Shemaiah: Othni, Rephael, Obed and Elzabad; his relatives Elihu and Semakiah were also able men. All these were descendants of Obed-Edom; they and their sons and their relatives were capable men with the strength to do the work—descendants of Obed-Edom, 62 in all.

Meshelemiah had sons and relatives, who were able men—18 in all.

10 Hosah the Merarite had sons: Shimri the first (although he was not the firstborn, his father had appointed him the first),(D) 11 Hilkiah the second, Tabaliah the third and Zechariah the fourth. The sons and relatives of Hosah were 13 in all.

12 These divisions of the gatekeepers, through their leaders, had duties for ministering(E) in the temple of the Lord, just as their relatives had. 13 Lots(F) were cast for each gate, according to their families, young and old alike.

14 The lot for the East Gate(G) fell to Shelemiah.[a] Then lots were cast for his son Zechariah,(H) a wise counselor, and the lot for the North Gate fell to him. 15 The lot for the South Gate fell to Obed-Edom,(I) and the lot for the storehouse fell to his sons. 16 The lots for the West Gate and the Shalleketh Gate on the upper road fell to Shuppim and Hosah.

Guard was alongside of guard: 17 There were six Levites a day on the east, four a day on the north, four a day on the south and two at a time at the storehouse. 18 As for the court[b] to the west, there were four at the road and two at the court[c] itself.

19 These were the divisions of the gatekeepers who were descendants of Korah and Merari.(J)

The Treasurers and Other Officials

20 Their fellow Levites(K) were[d] in charge of the treasuries of the house of God and the treasuries for the dedicated things.(L)

21 The descendants of Ladan, who were Gershonites through Ladan and who were heads of families belonging to Ladan the Gershonite,(M) were Jehieli, 22 the sons of Jehieli, Zetham and his brother Joel. They were in charge of the treasuries(N) of the temple of the Lord.

23 From the Amramites, the Izharites, the Hebronites and the Uzzielites:(O)

24 Shubael,(P) a descendant of Gershom son of Moses, was the official in charge of the treasuries. 25 His relatives through Eliezer: Rehabiah his son, Jeshaiah his son, Joram his son, Zikri his son and Shelomith(Q) his son. 26 Shelomith and his relatives were in charge of all the treasuries for the things dedicated(R) by King David, by the heads of families who were the commanders of thousands and commanders of hundreds, and by the other army commanders. 27 Some of the plunder taken in battle they dedicated for the repair of the temple of the Lord. 28 And everything dedicated by Samuel the seer(S) and by Saul son of Kish, Abner son of Ner and Joab son of Zeruiah, and all the other dedicated things were in the care of Shelomith and his relatives.

29 From the Izharites: Kenaniah and his sons were assigned duties away from the temple, as officials and judges(T) over Israel.

30 From the Hebronites: Hashabiah(U) and his relatives—seventeen hundred able men—were responsible in Israel west of the Jordan for all the work of the Lord and for the king’s service. 31 As for the Hebronites,(V) Jeriah was their chief according to the genealogical records of their families. In the fortieth(W) year of David’s reign a search was made in the records, and capable men among the Hebronites were found at Jazer in Gilead. 32 Jeriah had twenty-seven hundred relatives, who were able men and heads of families, and King David put them in charge of the Reubenites, the Gadites and the half-tribe of Manasseh for every matter pertaining to God and for the affairs of the king.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 26:14 A variant of Meshelemiah
  2. 1 Chronicles 26:18 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. 1 Chronicles 26:18 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  4. 1 Chronicles 26:20 Septuagint; Hebrew As for the Levites, Ahijah was