Add parallel Print Page Options

Samueli Atsanzika Anthu

12 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani. Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero. Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”

Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”

Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.”

Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”

Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.

“Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.

“Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu. 10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’ 11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.

12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu. 13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu. 14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino. 15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.

16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu! 17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”

18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.

19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”

20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse. 21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe. 22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake. 23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo. 24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani. 25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”

Samuel’s Farewell Speech

12 Samuel said to all Israel, “I have listened(A) to everything you said to me and have set a king(B) over you. Now you have a king as your leader.(C) As for me, I am old and gray, and my sons(D) are here with you. I have been your leader from my youth until this day. Here I stand. Testify against me in the presence of the Lord and his anointed.(E) Whose ox have I taken? Whose donkey(F) have I taken? Whom have I cheated? Whom have I oppressed? From whose hand have I accepted a bribe(G) to make me shut my eyes? If I have done(H) any of these things, I will make it right.”(I)

“You have not cheated or oppressed us,” they replied. “You have not taken anything from anyone’s hand.”

Samuel said to them, “The Lord is witness(J) against you, and also his anointed is witness this day, that you have not found anything(K) in my hand.(L)

“He is witness,” they said.

Then Samuel said to the people, “It is the Lord who appointed Moses and Aaron and brought(M) your ancestors up out of Egypt. Now then, stand(N) here, because I am going to confront(O) you with evidence before the Lord as to all the righteous acts(P) performed by the Lord for you and your ancestors.

“After Jacob(Q) entered Egypt, they cried(R) to the Lord for help, and the Lord sent(S) Moses and Aaron, who brought your ancestors out of Egypt and settled them in this place.

“But they forgot(T) the Lord their God; so he sold them(U) into the hand of Sisera,(V) the commander of the army of Hazor,(W) and into the hands of the Philistines(X) and the king of Moab,(Y) who fought against them. 10 They cried(Z) out to the Lord and said, ‘We have sinned; we have forsaken(AA) the Lord and served the Baals and the Ashtoreths.(AB) But now deliver us from the hands of our enemies, and we will serve you.’ 11 Then the Lord sent Jerub-Baal,[a](AC) Barak,[b](AD) Jephthah(AE) and Samuel,[c](AF) and he delivered you from the hands of your enemies all around you, so that you lived in safety.

12 “But when you saw that Nahash(AG) king(AH) of the Ammonites was moving against you, you said to me, ‘No, we want a king to rule(AI) over us’—even though the Lord your God was your king. 13 Now here is the king(AJ) you have chosen, the one you asked(AK) for; see, the Lord has set a king over you. 14 If you fear(AL) the Lord and serve and obey him and do not rebel(AM) against his commands, and if both you and the king who reigns over you follow the Lord your God—good! 15 But if you do not obey the Lord, and if you rebel against(AN) his commands, his hand will be against you, as it was against your ancestors.

16 “Now then, stand still(AO) and see(AP) this great thing the Lord is about to do before your eyes! 17 Is it not wheat harvest(AQ) now? I will call(AR) on the Lord to send thunder(AS) and rain.(AT) And you will realize what an evil(AU) thing you did in the eyes of the Lord when you asked for a king.”

18 Then Samuel called on the Lord,(AV) and that same day the Lord sent thunder and rain. So all the people stood in awe(AW) of the Lord and of Samuel.

19 The people all said to Samuel, “Pray(AX) to the Lord your God for your servants so that we will not die,(AY) for we have added to all our other sins the evil of asking for a king.”

20 “Do not be afraid,” Samuel replied. “You have done all this evil;(AZ) yet do not turn away from the Lord, but serve the Lord with all your heart. 21 Do not turn away after useless(BA) idols.(BB) They can do you no good, nor can they rescue you, because they are useless. 22 For the sake(BC) of his great name(BD) the Lord will not reject(BE) his people, because the Lord was pleased to make(BF) you his own. 23 As for me, far be it from me that I should sin against the Lord by failing to pray(BG) for you. And I will teach(BH) you the way that is good and right. 24 But be sure to fear(BI) the Lord and serve him faithfully with all your heart;(BJ) consider(BK) what great(BL) things he has done for you. 25 Yet if you persist(BM) in doing evil, both you and your king(BN) will perish.”(BO)

Footnotes

  1. 1 Samuel 12:11 Also called Gideon
  2. 1 Samuel 12:11 Some Septuagint manuscripts and Syriac; Hebrew Bedan
  3. 1 Samuel 12:11 Hebrew; some Septuagint manuscripts and Syriac Samson