Add parallel Print Page Options

Aisraeli Apempha kuti Akhale ndi Mfumu

Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli. Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba. Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.

Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama. Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”

Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova. Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo. Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe. Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”

10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova. 11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo. 12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake. 13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi. 14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake. 15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake. 16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito. 17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake. 18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”

19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira. 20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”

21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova. 22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.”

Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

Israel Asks for a King

When Samuel grew old, he appointed(A) his sons as Israel’s leaders.[a] The name of his firstborn was Joel and the name of his second was Abijah,(B) and they served at Beersheba.(C) But his sons(D) did not follow his ways. They turned aside(E) after dishonest gain and accepted bribes(F) and perverted(G) justice.

So all the elders(H) of Israel gathered together and came to Samuel at Ramah.(I) They said to him, “You are old, and your sons do not follow your ways; now appoint a king(J) to lead[b](K) us, such as all the other nations(L) have.”

But when they said, “Give us a king(M) to lead us,” this displeased(N) Samuel; so he prayed to the Lord. And the Lord told him: “Listen(O) to all that the people are saying to you; it is not you they have rejected,(P) but they have rejected me as their king.(Q) As they have done from the day I brought them up out of Egypt until this day, forsaking(R) me and serving other gods, so they are doing to you. Now listen to them; but warn them solemnly and let them know(S) what the king who will reign over them will claim as his rights.”

10 Samuel told(T) all the words of the Lord to the people who were asking him for a king. 11 He said, “This is what the king who will reign over you will claim as his rights: He will take(U) your sons and make them serve(V) with his chariots and horses, and they will run in front of his chariots.(W) 12 Some he will assign to be commanders(X) of thousands and commanders of fifties, and others to plow his ground and reap his harvest, and still others to make weapons of war and equipment for his chariots. 13 He will take your daughters to be perfumers and cooks and bakers. 14 He will take the best of your(Y) fields and vineyards(Z) and olive groves and give them to his attendants.(AA) 15 He will take a tenth(AB) of your grain and of your vintage and give it to his officials and attendants. 16 Your male and female servants and the best of your cattle[c] and donkeys he will take for his own use. 17 He will take a tenth of your flocks, and you yourselves will become his slaves. 18 When that day comes, you will cry out for relief from the king you have chosen, but the Lord will not answer(AC) you in that day.(AD)

19 But the people refused(AE) to listen to Samuel. “No!” they said. “We want(AF) a king(AG) over us. 20 Then we will be like all the other nations,(AH) with a king to lead us and to go out before us and fight our battles.”

21 When Samuel heard all that the people said, he repeated(AI) it before the Lord. 22 The Lord answered, “Listen(AJ) to them and give them a king.”

Then Samuel said to the Israelites, “Everyone go back to your own town.”

Footnotes

  1. 1 Samuel 8:1 Traditionally judges
  2. 1 Samuel 8:5 Traditionally judge; also in verses 6 and 20
  3. 1 Samuel 8:16 Septuagint; Hebrew young men