Add parallel Print Page Options

Malangizo Achipembedzo

Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

Instructions on Worship

I urge, then, first of all, that petitions, prayers,(A) intercession and thanksgiving be made for all people— for kings and all those in authority,(B) that we may live peaceful and quiet lives in all godliness(C) and holiness. This is good, and pleases(D) God our Savior,(E) who wants(F) all people(G) to be saved(H) and to come to a knowledge of the truth.(I) For there is one God(J) and one mediator(K) between God and mankind, the man Christ Jesus,(L) who gave himself as a ransom(M) for all people. This has now been witnessed to(N) at the proper time.(O) And for this purpose I was appointed a herald and an apostle—I am telling the truth, I am not lying(P)—and a true and faithful teacher(Q) of the Gentiles.(R)

Therefore I want the men everywhere to pray, lifting up holy hands(S) without anger or disputing. I also want the women to dress modestly, with decency and propriety, adorning themselves, not with elaborate hairstyles or gold or pearls or expensive clothes,(T) 10 but with good deeds,(U) appropriate for women who profess to worship God.

11 A woman[a] should learn in quietness and full submission.(V) 12 I do not permit a woman to teach or to assume authority over a man;[b] she must be quiet.(W) 13 For Adam was formed first, then Eve.(X) 14 And Adam was not the one deceived; it was the woman who was deceived and became a sinner.(Y) 15 But women[c] will be saved through childbearing—if they continue in faith, love(Z) and holiness with propriety.

Footnotes

  1. 1 Timothy 2:11 Or wife; also in verse 12
  2. 1 Timothy 2:12 Or over her husband
  3. 1 Timothy 2:15 Greek she