Add parallel Print Page Options

Malangizo kwa Timoteyo

Mzimu akunena momveka bwino kuti mʼmasiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chawo ndi kutsatira mizimu yonyenga ndi zinthu zophunzitsidwa ndi ziwanda. Ziphunzitso zimenezi zimachokera ku chinyengo cha anthu onama, amene chikumbumtima chawo chinamatidwa ndi chitsulo cha moto. Iwo amaletsa anthu ukwati ndi kuwalamula kuti asamadye zakudya zina, zimene Mulungu analenga kuti amene anakhulupirira ndi kudziwa choonadi, azidye moyamika. Pakuti chilichonse chimene Mulungu analenga ndi chabwino, ndipo chilichonse chisasalidwe, akamachilandira moyamika, pakuti chimayeretsedwa ndi mawu a Mulungu ndi pemphero.

Ngati abale uwalangiza zimenezi, udzakhala mtumiki wabwino wa Khristu Yesu, woleredwa mʼchoonadi cha chikhulupiriro ndi mʼchiphunzitso chabwino chimene wakhala ukutsata. Koma upewe nkhani zachabe ndi nthano za amayi okalamba; mʼmalo mwake udziphunzitse kukhala moyo wolemekeza Mulungu. Pakuti kulimbitsa thupi kumapindulitsapo pangʼono, koma moyo woopa Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo umene ukubwerawo.

Amenewa ndi mawu odalirika ndi oyenera kuwalandira kwathunthu. 10 Nʼchifukwa chake timagwira ntchito molimbika ndi kuyesetsa, chifukwa tayika chiyembekezo chathu mwa Mulungu wamoyo, amene ndi Mpulumutsi wa anthu onse, koma makamaka wa amene amakhulupirira.

11 Lamulira ndi kuphunzitsa zinthu zimenezi. 12 Usalole kuti wina akupeputse chifukwa ndiwe wachinyamata, koma khala chitsanzo kwa okhulupirira pa mayankhulidwe, pa makhalidwe, pa chikondi, pa chikhulupiriro ndi pa kuyera mtima. 13 Mpaka nditabwera, udzipereke powerenga mawu a Mulungu kwa anthu, kulalikira ndi kuphunzitsa. 14 Usanyozere mphatso yako yomwe inapatsidwa kwa iwe kudzera mʼmawu auneneri pamene gulu la akulu ampingo linakusanjika manja.

15 Uzichita zimenezi mosamalitsa ndi modzipereka kwathunthu, kuti aliyense aone kuti ukupita mʼtsogolo. 16 Samala kwambiri moyo wako ndi ziphunzitso zako. Uzichitabe zimenezi chifukwa ukatero, udzadzipulumutsa ndiponso udzapulumutsa okumvetsera.

The Spirit(A) clearly says that in later times(B) some will abandon the faith and follow deceiving spirits(C) and things taught by demons. Such teachings come through hypocritical liars, whose consciences have been seared as with a hot iron.(D) They forbid people to marry(E) and order them to abstain from certain foods,(F) which God created(G) to be received with thanksgiving(H) by those who believe and who know the truth. For everything God created is good,(I) and nothing is to be rejected(J) if it is received with thanksgiving, because it is consecrated by the word of God(K) and prayer.

If you point these things out to the brothers and sisters,[a] you will be a good minister of Christ Jesus, nourished on the truths of the faith(L) and of the good teaching that you have followed.(M) Have nothing to do with godless myths and old wives’ tales;(N) rather, train yourself to be godly.(O) For physical training is of some value, but godliness has value for all things,(P) holding promise for both the present life(Q) and the life to come.(R) This is a trustworthy saying(S) that deserves full acceptance. 10 That is why we labor and strive, because we have put our hope in the living God,(T) who is the Savior of all people,(U) and especially of those who believe.

11 Command and teach these things.(V) 12 Don’t let anyone look down on you(W) because you are young, but set an example(X) for the believers in speech, in conduct, in love, in faith(Y) and in purity. 13 Until I come,(Z) devote yourself to the public reading of Scripture,(AA) to preaching and to teaching. 14 Do not neglect your gift, which was given you through prophecy(AB) when the body of elders(AC) laid their hands on you.(AD)

15 Be diligent in these matters; give yourself wholly to them, so that everyone may see your progress. 16 Watch your life and doctrine closely. Persevere in them, because if you do, you will save(AE) both yourself and your hearers.

Footnotes

  1. 1 Timothy 4:6 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family.