Add parallel Print Page Options

Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo. Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.

Chikondi ndi Chidani

Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake. Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi. Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye. Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.

Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale. Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.

Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima. 10 Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa. 11 Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.

12 Inu ana okondedwa, ndikukulemberani
    popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.
13 Inu abambo, ndikukulemberani
    popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.
Inu anyamata, ndikukulemberani
    popeza kuti munagonjetsa woyipayo.
14 Ana okondedwa, ndikukulemberani
    chifukwa mumawadziwa Atate.
Abambo, ndikukulemberani
    chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi.
Inu anyamata, ndikukulemberani
    chifukwa ndinu amphamvu.
    Mawu a Mulungu amakhala mwa inu
    ndipo mumamugonjetsa woyipayo.

Musakonde Dziko Lapansi

15 Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate. 16 Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi. 17 Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya.

Anthu Okana Khristu

18 Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza. 19 Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.

20 Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi. 21 Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi. 22 Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana. 23 Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.

24 Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate. 25 Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha.

26 Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani. 27 Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.

Ana a Mulungu

28 Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.

29 Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.

My dear children,(A) I write this to you so that you will not sin. But if anybody does sin, we have an advocate(B) with the Father—Jesus Christ, the Righteous One. He is the atoning sacrifice for our sins,(C) and not only for ours but also for the sins of the whole world.(D)

Love and Hatred for Fellow Believers

We know(E) that we have come to know him(F) if we keep his commands.(G) Whoever says, “I know him,”(H) but does not do what he commands is a liar, and the truth is not in that person.(I) But if anyone obeys his word,(J) love for God[a] is truly made complete in them.(K) This is how we know(L) we are in him: Whoever claims to live in him must live as Jesus did.(M)

Dear friends,(N) I am not writing you a new command but an old one, which you have had since the beginning.(O) This old command is the message you have heard. Yet I am writing you a new command;(P) its truth is seen in him and in you, because the darkness is passing(Q) and the true light(R) is already shining.(S)

Anyone who claims to be in the light but hates a brother or sister[b](T) is still in the darkness.(U) 10 Anyone who loves their brother and sister[c] lives in the light,(V) and there is nothing in them to make them stumble.(W) 11 But anyone who hates a brother or sister(X) is in the darkness and walks around in the darkness.(Y) They do not know where they are going, because the darkness has blinded them.(Z)

Reasons for Writing

12 I am writing to you, dear children,(AA)
    because your sins have been forgiven on account of his name.(AB)
13 I am writing to you, fathers,
    because you know him who is from the beginning.(AC)
I am writing to you, young men,
    because you have overcome(AD) the evil one.(AE)

14 I write to you, dear children,(AF)
    because you know the Father.
I write to you, fathers,
    because you know him who is from the beginning.(AG)
I write to you, young men,
    because you are strong,(AH)
    and the word of God(AI) lives in you,(AJ)
    and you have overcome the evil one.(AK)

On Not Loving the World

15 Do not love the world or anything in the world.(AL) If anyone loves the world, love for the Father[d] is not in them.(AM) 16 For everything in the world—the lust of the flesh,(AN) the lust of the eyes,(AO) and the pride of life—comes not from the Father but from the world. 17 The world and its desires pass away,(AP) but whoever does the will of God(AQ) lives forever.

Warnings Against Denying the Son

18 Dear children, this is the last hour;(AR) and as you have heard that the antichrist is coming,(AS) even now many antichrists have come.(AT) This is how we know it is the last hour. 19 They went out from us,(AU) but they did not really belong to us. For if they had belonged to us, they would have remained with us; but their going showed that none of them belonged to us.(AV)

20 But you have an anointing(AW) from the Holy One,(AX) and all of you know the truth.[e](AY) 21 I do not write to you because you do not know the truth, but because you do know it(AZ) and because no lie comes from the truth. 22 Who is the liar? It is whoever denies that Jesus is the Christ. Such a person is the antichrist—denying the Father and the Son.(BA) 23 No one who denies the Son has the Father; whoever acknowledges the Son has the Father also.(BB)

24 As for you, see that what you have heard from the beginning(BC) remains in you. If it does, you also will remain in the Son and in the Father.(BD) 25 And this is what he promised us—eternal life.(BE)

26 I am writing these things to you about those who are trying to lead you astray.(BF) 27 As for you, the anointing(BG) you received from him remains in you, and you do not need anyone to teach you. But as his anointing teaches you about all things(BH) and as that anointing is real, not counterfeit—just as it has taught you, remain in him.(BI)

God’s Children and Sin

28 And now, dear children,(BJ) continue in him, so that when he appears(BK) we may be confident(BL) and unashamed before him at his coming.(BM)

29 If you know that he is righteous,(BN) you know that everyone who does what is right has been born of him.(BO)

Footnotes

  1. 1 John 2:5 Or word, God’s love
  2. 1 John 2:9 The Greek word for brother or sister (adelphos) refers here to a believer, whether man or woman, as part of God’s family; also in verse 11; and in 3:15, 17; 4:20; 5:16.
  3. 1 John 2:10 The Greek word for brother and sister (adelphos) refers here to a believer, whether man or woman, as part of God’s family; also in 3:10; 4:20, 21.
  4. 1 John 2:15 Or world, the Father’s love
  5. 1 John 2:20 Some manuscripts and you know all things