Add parallel Print Page Options

Kuyesa Mizimu

Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi. Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu, koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.

Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi. Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera. Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.

Mulungu ndiye Chikondi

Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu. Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi. Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo. 10 Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu. 11 Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake. 12 Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.

13 Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake. 14 Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi. 15 Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu. 16 Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife.

Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye. 17 Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu. 18 Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.

19 Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda. 20 Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone. 21 Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.

On Denying the Incarnation

Dear friends,(A) do not believe every spirit,(B) but test the spirits to see whether they are from God, because many false prophets have gone out into the world.(C) This is how you can recognize the Spirit of God: Every spirit that acknowledges that Jesus Christ has come in the flesh(D) is from God,(E) but every spirit that does not acknowledge Jesus is not from God. This is the spirit of the antichrist,(F) which you have heard is coming and even now is already in the world.(G)

You, dear children,(H) are from God and have overcome them,(I) because the one who is in you(J) is greater than the one who is in the world.(K) They are from the world(L) and therefore speak from the viewpoint of the world, and the world listens to them. We are from God, and whoever knows God listens to us; but whoever is not from God does not listen to us.(M) This is how we recognize the Spirit[a] of truth(N) and the spirit of falsehood.(O)

God’s Love and Ours

Dear friends, let us love one another,(P) for love comes from God. Everyone who loves has been born of God(Q) and knows God.(R) Whoever does not love does not know God, because God is love.(S) This is how God showed his love among us: He sent his one and only Son(T) into the world that we might live through him.(U) 10 This is love: not that we loved God, but that he loved us(V) and sent his Son as an atoning sacrifice for our sins.(W) 11 Dear friends,(X) since God so loved us,(Y) we also ought to love one another.(Z) 12 No one has ever seen God;(AA) but if we love one another, God lives in us and his love is made complete in us.(AB)

13 This is how we know(AC) that we live in him and he in us: He has given us of his Spirit.(AD) 14 And we have seen and testify(AE) that the Father has sent his Son to be the Savior of the world.(AF) 15 If anyone acknowledges that Jesus is the Son of God,(AG) God lives in them and they in God.(AH) 16 And so we know and rely on the love God has for us.

God is love.(AI) Whoever lives in love lives in God, and God in them.(AJ) 17 This is how love is made complete(AK) among us so that we will have confidence(AL) on the day of judgment:(AM) In this world we are like Jesus. 18 There is no fear in love. But perfect love drives out fear,(AN) because fear has to do with punishment. The one who fears is not made perfect in love.

19 We love because he first loved us.(AO) 20 Whoever claims to love God yet hates a brother or sister(AP) is a liar.(AQ) For whoever does not love their brother and sister, whom they have seen,(AR) cannot love God, whom they have not seen.(AS) 21 And he has given us this command:(AT) Anyone who loves God must also love their brother and sister.(AU)

Footnotes

  1. 1 John 4:6 Or spirit