Add parallel Print Page Options

Mawu Otsiriza ndi Ochenjeza

13 Uwu ndi ulendo wachitatu ndikubwera kudzakuyenderani. “Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.” Ndinakuchenjezani kale pamene ndinali nanu ulendo wachiwiri uja. Tsopano ndikubwereza ndisanafike. Ndikabweranso sindidzachitira chifundo amene anachimwa poyamba paja kapena wina aliyense amene anachimwa, popeza mufuna chitsimikizo chakuti Khristu akuyankhula kudzera mwa ine. Iye siwofowoka pofuna kuchita nanu koma ndi wamphamvu pakati panu. Pofuna kutsimikizira, anapachikidwa ali wofowoka koma ali ndi moyo mwamphamvu ya Mulungu. Chomwechonso, ife ndife ofowoka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, potumikira pakati panu.

Tadzisanthulani nokha kuti muone ngati muli mʼchikhulupiriro; dziyeseni nokha. Kodi simuzindikira kuti Khristu Yesu ali mwa inu, ngati si choncho mwalephera mayesowa? Ndipo ndikhulupirira kuti mudzazindikira kuti ife sitinalephere mayesowo. Tsopano tikupemphera kwa Mulungu kuti musadzachite kanthu kena kalikonse kolakwa. Osati chifukwa choti anthu aone kuti ife tapambana mayesowo koma kuti mudzachite zokhoza ngakhale anthu atamationa ngati olephera. Pakuti sitingachite chilichonse chotsutsana ndi choonadi, koma chokhacho chovomerezana ndi choonadi. Ife timasangalala kuti pamene tafowoka, inu muli amphamvu; ndipo pemphero lathu ndi lakuti mukhale angwiro. 10 Nʼchifukwa chake ndimalemba zinthu zoterezi pamene ndili kutali, kuti ndikabwera ndisadzagwiritse ntchito ulamuliro wanga mokalipa, uwu ndi ulamuliro umene Ambuye anandipatsa kuti ndikukuzeni inu osati kukuwonongani.

Malonje Otsiriza

11 Potsiriza abale, ndikuti tsalani bwino. Yesetsani kukhala angwiro, mvetsetsani pempho langa, khalani a mtima umodzi, khalani mwamtendere. Ndipo Mulungu wachikondi ndi mtendere adzakhala nanu.

12 Lonjeranani ndi mpsopsono wachiyero. 13 Anthu onse a Mulungu akupereka moni.

14 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.

Final Warnings

13 This will be my third visit to you.(A) “Every matter must be established by the testimony of two or three witnesses.”[a](B) I already gave you a warning when I was with you the second time. I now repeat it while absent:(C) On my return I will not spare(D) those who sinned earlier(E) or any of the others, since you are demanding proof that Christ is speaking through me.(F) He is not weak in dealing with you, but is powerful among you. For to be sure, he was crucified in weakness,(G) yet he lives by God’s power.(H) Likewise, we are weak(I) in him, yet by God’s power we will live with him(J) in our dealing with you.

Examine yourselves(K) to see whether you are in the faith; test yourselves.(L) Do you not realize that Christ Jesus is in you(M)—unless, of course, you fail the test? And I trust that you will discover that we have not failed the test. Now we pray to God that you will not do anything wrong—not so that people will see that we have stood the test but so that you will do what is right even though we may seem to have failed. For we cannot do anything against the truth, but only for the truth. We are glad whenever we are weak(N) but you are strong;(O) and our prayer is that you may be fully restored.(P) 10 This is why I write these things when I am absent, that when I come I may not have to be harsh(Q) in my use of authority—the authority the Lord gave me for building you up, not for tearing you down.(R)

Final Greetings

11 Finally, brothers and sisters,(S) rejoice! Strive for full restoration, encourage one another, be of one mind, live in peace.(T) And the God of love(U) and peace(V) will be with you.

12 Greet one another with a holy kiss.(W) 13 All God’s people here send their greetings.(X)

14 May the grace of the Lord Jesus Christ,(Y) and the love of God,(Z) and the fellowship of the Holy Spirit(AA) be with you all.

Footnotes

  1. 2 Corinthians 13:1 Deut. 19:15