Add parallel Print Page Options

Akhristu ndi Kalata Yochokera kwa Khristu

Kodi tayambanso kudzichitira umboni tokha? Kapena kodi ifenso tikufuna makalata otivomereza kwa inu, kapena ochokera kwa inu monga anthu ena? Inu ndinu kalata yathu, yolembedwa pa mitima yathu, yodziwika ndi yowerengedwa ndi aliyense. Inu mukuonetsa kuti ndinu kalata yochokera kwa Khristu, zotsatira za utumiki wathu, osati yolembedwa ndi inki koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo, osati pa miyala yosemedwa koma mʼmitima ya anthu.

Kulimba mtima kumeneku tili nako pamaso pa Mulungu kudzera mwa Khristu. Sikuti mwa ife muli kanthu kotiganizitsa kuti tingathe kugwira ntchitoyi patokha, koma kulimba mtima kwathu kumachokera kwa Mulungu. Iye watipatsa kulimba mtima kuti tikhale atumiki a pangano latsopano, osati malamulo olembedwa koma a Mzimu; pakuti malamulo olembedwa amapha koma Mzimu amapereka moyo.

Ulemerero wa Pangano Latsopano

Koma ngati utumiki umene unabweretsa imfa uja, wolembedwa ndi malemba pa mwalawu, unabwera ndi ulemerero mwakuti Aisraeli sanathe kuyangʼanitsitsa nkhope ya Mose chifukwa cha ulemerero wa pa nkhopeyo, ngakhale kuti unali kunka nuzilala, kodi nanga utumiki wa Mzimu sudzaposa apa? Ngati utumiki umene umatsutsa anthu unali ndi ulemerero, nanga koposa kotani ulemerero wa utumiki wobweretsa chilungamo! 10 Pakuti zimene zinali ndi ulemerero, tsopano zilibenso ulemerero pofananitsa ndi ulemerero wopambanawo. 11 Ndipo ngati zosakhalitsa zinabwera ndi ulemerero, koposa kotani ulemerero wamuyayawo!

12 Choncho, popeza tili ndi chiyembekezo chotere, ndife olimba mtima kwambiri. 13 Ife sitili ngati Mose amene amaphimba nkhope yake kuopa kuti Aisraeli angaone kuti kunyezimira kwa nkhope yake kumazilala. 14 Koma nzeru zawo zinawumitsidwa, pakuti mpaka lero chophimbira chomwecho chikanalipo pamene akuwerenga Chipangano Chakale. Sichinachotsedwebe, chifukwa chimachotsedwa ngati munthuyo ali mwa Khristu yekha. 15 Ngakhale lero lomwe lino akuwerenga mabuku a Mose pali chophimbabe mitima yawo. 16 Koma pamene aliyense atembenukira kwa Ambuye, “chophimbacho chimachotsedwa.” 17 Tsono Ambuye ndi Mzimu, ndipo pamene pali Mzimu wa Ambuye, pali ufulu. 18 Ife tonse, amene ndi nkhope zosaphimba timaonetsera ulemerero wa Ambuye, tikusinthika kufanana ndi ulemerero wake, umene ukunka nuchulukirachulukira, wochokera kwa Ambuye, amene ndi Mzimu.

Are we beginning to commend ourselves(A) again? Or do we need, like some people, letters of recommendation(B) to you or from you? You yourselves are our letter, written on our hearts, known and read by everyone.(C) You show that you are a letter from Christ, the result of our ministry, written not with ink but with the Spirit of the living God,(D) not on tablets of stone(E) but on tablets of human hearts.(F)

Such confidence(G) we have through Christ before God. Not that we are competent in ourselves(H) to claim anything for ourselves, but our competence comes from God.(I) He has made us competent as ministers of a new covenant(J)—not of the letter(K) but of the Spirit; for the letter kills, but the Spirit gives life.(L)

The Greater Glory of the New Covenant

Now if the ministry that brought death,(M) which was engraved in letters on stone, came with glory, so that the Israelites could not look steadily at the face of Moses because of its glory,(N) transitory though it was, will not the ministry of the Spirit be even more glorious? If the ministry that brought condemnation(O) was glorious, how much more glorious is the ministry that brings righteousness!(P) 10 For what was glorious has no glory now in comparison with the surpassing glory. 11 And if what was transitory came with glory, how much greater is the glory of that which lasts!

12 Therefore, since we have such a hope,(Q) we are very bold.(R) 13 We are not like Moses, who would put a veil over his face(S) to prevent the Israelites from seeing the end of what was passing away. 14 But their minds were made dull,(T) for to this day the same veil remains when the old covenant(U) is read.(V) It has not been removed, because only in Christ is it taken away. 15 Even to this day when Moses is read, a veil covers their hearts. 16 But whenever anyone turns to the Lord,(W) the veil is taken away.(X) 17 Now the Lord is the Spirit,(Y) and where the Spirit of the Lord is, there is freedom.(Z) 18 And we all, who with unveiled faces contemplate[a](AA) the Lord’s glory,(AB) are being transformed into his image(AC) with ever-increasing glory, which comes from the Lord, who is the Spirit.

Footnotes

  1. 2 Corinthians 3:18 Or reflect