Add parallel Print Page Options

Matupi Atsopano

Popeza tikudziwa kuti ngati msasa wa dziko lapansi umene tikukhalamo uwonongeka, tili ndi nyumba yochokera kwa Mulungu, nyumba yamuyaya yakumwamba, osati yomangidwa ndi manja a anthu. Pakali pano tibuwula, ndi kulakalaka kuvala nyumba yathu ya kumwambayo, chifukwa tikavala, sitidzapezekanso amaliseche. Pamene tili mu msasa uno, timalemedwa ndipo timabuwula, chifukwa sitifuna kukhala amaliseche koma ovala nyumba yathu ya kumwamba, kuti chimene chili chakufa chimezedwe ndi moyo. Tsono ndi Mulungu amene anatikonzeratu ife kuti tilandire zimenezi. Iye anatipatsa Mzimu ngati chikole, kutsimikizira zimene zikubwera.

Nʼchifukwa chake nthawi zonse timalimba mtima, ndipo timadziwa kuti pamene tikukhala mʼthupi, ndiye kuti tili kutali ndi Ambuye. Ife timakhala mwachikhulupiriro, osati mwa zooneka ndi maso. Inde, ife tikulimba mtima, ndipo tikanakonda kulekana nalo thupi lathu ndi kukhala ndi Ambuye. Choncho timayesetsa kukondweretsa Ambuye, ngakhale tikhale mʼthupi, kapena tichokemo. 10 Pakuti tonsefe tiyenera kukaonekera pa mpando woweruza wa Khristu, kuti aliyense wa ife akalandire zomuyenera molingana ndi zimene anachita ali mʼthupi; zabwino kapena zoyipa.

Ntchito Yoyanjanitsa

11 Tsono popeza tikudziwa tanthauzo la kuopa Ambuye, ife timayesetsa kukopa anthu. Mulungu amatidziwa bwino lomwe, ndipo tikukhulupirira kuti inunso mumatidziwa bwino mʼmitima mwanu. 12 Sitikudzichitiranso tokha umboni kwa inu, koma tikukupatsani mwayi oti muzitinyadira. Tikufuna kuti muwayankhe amene amanyadira zinthu zooneka ndi maso osati zimene zili mu mtima. 13 Ngati ndife amisala, monga amanenera ena, nʼchifukwa chofuna kuti Mulungu alemekezedwe. Ngati si ife amisala, nʼkuti inu muthandizike. 14 Pakuti chikondi cha Khristu ndicho chimatikakamiza, chifukwa tikutsimikiza kuti mmodzi anafera anthu onse, kotero kuti anthu onse anafanso. 15 Ndipo Iye anafera anthu onse kuti amene ali ndi moyo, asakhale ndi moyo wofuna kudzikondweretsa okha, koma azikondweretsa amene anawafera naukitsidwa chifukwa cha iwowo.

16 Choncho, kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ife sitiganizirapo za munthu aliyense monga mwanzeru za umunthu, ngakhale kuti poyamba tinkaganiza za Khristu mʼnjira imeneyi, koma tsopano sititeronso. 17 Nʼchifukwa chake, ngati munthu aliyense ali mwa Khristu, ndi wolengedwa kwatsopano; zinthu zakale zapita taonani, zakhala zatsopano. 18 Zonsezi zichokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa ndi Iye mwini kudzera mwa Khristu ndipo anatipatsa ife utumiki wa chiyanjanitso. 19 Mulungu ankayanjanitsa dziko lapansi kwa Iye mwini kudzera mwa Khristu, osawerengera anthu monga mwa zochimwa zawo. Ndipo watisungitsa ife uthenga uwu wa chiyanjanitso. 20 Choncho ife ndi akazembe a Khristu, monga ngati Mulungu akudandaulira anthu kudzera mwa ife. Ife tikukupemphani inu mʼmalo mwa Khristu kuti, yanjanitsidwani ndi Mulungu. 21 Chifukwa cha ife, Mulungu anasandutsa wopanda tchimoyo kukhala tchimo, kuti mwa Iye ife tikakhale chilungamo cha Mulungu.

Awaiting the New Body

For we know that if the earthly(A) tent(B) we live in is destroyed, we have a building from God, an eternal house in heaven, not built by human hands. Meanwhile we groan,(C) longing to be clothed instead with our heavenly dwelling,(D) because when we are clothed, we will not be found naked. For while we are in this tent, we groan(E) and are burdened, because we do not wish to be unclothed but to be clothed instead with our heavenly dwelling,(F) so that what is mortal may be swallowed up by life. Now the one who has fashioned us for this very purpose is God, who has given us the Spirit as a deposit, guaranteeing what is to come.(G)

Therefore we are always confident and know that as long as we are at home in the body we are away from the Lord. For we live by faith, not by sight.(H) We are confident, I say, and would prefer to be away from the body and at home with the Lord.(I) So we make it our goal to please him,(J) whether we are at home in the body or away from it. 10 For we must all appear before the judgment seat of Christ, so that each of us may receive what is due us(K) for the things done while in the body, whether good or bad.

The Ministry of Reconciliation

11 Since, then, we know what it is to fear the Lord,(L) we try to persuade others. What we are is plain to God, and I hope it is also plain to your conscience.(M) 12 We are not trying to commend ourselves to you again,(N) but are giving you an opportunity to take pride in us,(O) so that you can answer those who take pride in what is seen rather than in what is in the heart. 13 If we are “out of our mind,”(P) as some say, it is for God; if we are in our right mind, it is for you. 14 For Christ’s love compels us, because we are convinced that one died for all, and therefore all died.(Q) 15 And he died for all, that those who live should no longer live for themselves(R) but for him who died for them(S) and was raised again.

16 So from now on we regard no one from a worldly(T) point of view. Though we once regarded Christ in this way, we do so no longer. 17 Therefore, if anyone is in Christ,(U) the new creation(V) has come:[a] The old has gone, the new is here!(W) 18 All this is from God,(X) who reconciled us to himself through Christ(Y) and gave us the ministry of reconciliation: 19 that God was reconciling the world to himself in Christ, not counting people’s sins against them.(Z) And he has committed to us the message of reconciliation. 20 We are therefore Christ’s ambassadors,(AA) as though God were making his appeal through us.(AB) We implore you on Christ’s behalf: Be reconciled to God.(AC) 21 God made him who had no sin(AD) to be sin[b] for us, so that in him we might become the righteousness of God.(AE)

Footnotes

  1. 2 Corinthians 5:17 Or Christ, that person is a new creation.
  2. 2 Corinthians 5:21 Or be a sin offering