Add parallel Print Page Options

Manase Mfumu ya Yuda

21 Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli. Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga. Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.” Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga. Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.

Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya. Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.” Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.

10 Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti, 11 “Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake. 12 Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru. 13 Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi. 14 Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse 15 chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’ ”

16 Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.

17 Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 18 Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Amoni Mfumu ya Yuda

19 Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba. 20 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake. 21 Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira. 22 Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.

23 Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake. 24 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.

25 Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 26 Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Manasseh King of Judah(A)(B)

21 Manasseh was twelve years old when he became king, and he reigned in Jerusalem fifty-five years. His mother’s name was Hephzibah.(C) He did evil(D) in the eyes of the Lord, following the detestable practices(E) of the nations the Lord had driven out before the Israelites. He rebuilt the high places(F) his father Hezekiah had destroyed; he also erected altars to Baal(G) and made an Asherah pole,(H) as Ahab king of Israel had done. He bowed down to all the starry hosts(I) and worshiped them. He built altars(J) in the temple of the Lord, of which the Lord had said, “In Jerusalem I will put my Name.”(K) In the two courts(L) of the temple of the Lord, he built altars to all the starry hosts. He sacrificed his own son(M) in the fire, practiced divination,(N) sought omens, and consulted mediums and spiritists.(O) He did much evil in the eyes of the Lord, arousing(P) his anger.

He took the carved Asherah pole(Q) he had made and put it in the temple,(R) of which the Lord had said to David and to his son Solomon, “In this temple and in Jerusalem, which I have chosen out of all the tribes of Israel, I will put my Name(S) forever. I will not again(T) make the feet of the Israelites wander from the land I gave their ancestors, if only they will be careful to do everything I commanded them and will keep the whole Law that my servant Moses(U) gave them.” But the people did not listen. Manasseh led them astray, so that they did more evil(V) than the nations(W) the Lord had destroyed before the Israelites.

10 The Lord said through his servants the prophets: 11 “Manasseh king of Judah has committed these detestable sins. He has done more evil(X) than the Amorites(Y) who preceded him and has led Judah into sin with his idols.(Z) 12 Therefore this is what the Lord, the God of Israel, says: I am going to bring such disaster(AA) on Jerusalem and Judah that the ears of everyone who hears of it will tingle.(AB) 13 I will stretch out over Jerusalem the measuring line used against Samaria and the plumb line(AC) used against the house of Ahab. I will wipe(AD) out Jerusalem as one wipes a dish, wiping it and turning it upside down. 14 I will forsake(AE) the remnant(AF) of my inheritance and give them into the hands of enemies. They will be looted and plundered by all their enemies; 15 they have done evil(AG) in my eyes and have aroused(AH) my anger from the day their ancestors came out of Egypt until this day.”

16 Moreover, Manasseh also shed so much innocent blood(AI) that he filled Jerusalem from end to end—besides the sin that he had caused Judah(AJ) to commit, so that they did evil in the eyes of the Lord.

17 As for the other events of Manasseh’s reign, and all he did, including the sin he committed, are they not written in the book of the annals of the kings of Judah? 18 Manasseh rested with his ancestors and was buried in his palace garden,(AK) the garden of Uzza. And Amon his son succeeded him as king.

Amon King of Judah(AL)

19 Amon was twenty-two years old when he became king, and he reigned in Jerusalem two years. His mother’s name was Meshullemeth daughter of Haruz; she was from Jotbah. 20 He did evil(AM) in the eyes of the Lord, as his father Manasseh had done. 21 He followed completely the ways of his father, worshiping the idols his father had worshiped, and bowing down to them. 22 He forsook(AN) the Lord, the God of his ancestors, and did not walk(AO) in obedience to him.

23 Amon’s officials conspired against him and assassinated(AP) the king in his palace. 24 Then the people of the land killed(AQ) all who had plotted against King Amon, and they made Josiah(AR) his son king in his place.

25 As for the other events of Amon’s reign, and what he did, are they not written in the book of the annals of the kings of Judah? 26 He was buried in his tomb in the garden(AS) of Uzza. And Josiah his son succeeded him as king.