Add parallel Print Page Options

24 Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara. Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake. Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita, kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.

Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.

Yoyakini Mfumu ya Yuda

Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.

10 Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo 11 ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga. 12 Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni.

Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake. 13 Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga. 14 Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.

15 Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo. 16 Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000. 17 Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.

Zedekiya Mfumu ya Yuda

18 Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina. 19 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu. 20 Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake.

Kuwonongeka kwa Yerusalemu

Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.

24 During Jehoiakim’s reign, Nebuchadnezzar(A) king of Babylon invaded(B) the land, and Jehoiakim became his vassal for three years. But then he turned against Nebuchadnezzar and rebelled.(C) The Lord sent Babylonian,[a](D) Aramean,(E) Moabite and Ammonite raiders(F) against him to destroy(G) Judah, in accordance with the word of the Lord proclaimed by his servants the prophets.(H) Surely these things happened to Judah according to the Lord’s command,(I) in order to remove them from his presence(J) because of the sins of Manasseh(K) and all he had done, including the shedding of innocent blood.(L) For he had filled Jerusalem with innocent blood, and the Lord was not willing to forgive.(M)

As for the other events of Jehoiakim’s reign,(N) and all he did, are they not written in the book of the annals of the kings of Judah? Jehoiakim rested(O) with his ancestors. And Jehoiachin(P) his son succeeded him as king.

The king of Egypt(Q) did not march out from his own country again, because the king of Babylon(R) had taken all his territory, from the Wadi of Egypt to the Euphrates River.

Jehoiachin King of Judah(S)

Jehoiachin(T) was eighteen years old when he became king, and he reigned in Jerusalem three months. His mother’s name was Nehushta(U) daughter of Elnathan; she was from Jerusalem. He did evil(V) in the eyes of the Lord, just as his father had done.

10 At that time the officers of Nebuchadnezzar(W) king of Babylon advanced on Jerusalem and laid siege to it, 11 and Nebuchadnezzar himself came up to the city while his officers were besieging it. 12 Jehoiachin king of Judah, his mother, his attendants, his nobles and his officials all surrendered(X) to him.

In the eighth year of the reign of the king of Babylon, he took Jehoiachin prisoner. 13 As the Lord had declared,(Y) Nebuchadnezzar removed the treasures(Z) from the temple of the Lord and from the royal palace, and cut up the gold articles(AA) that Solomon(AB) king of Israel had made for the temple of the Lord. 14 He carried all Jerusalem into exile:(AC) all the officers and fighting men,(AD) and all the skilled workers and artisans—a total of ten thousand. Only the poorest(AE) people of the land were left.

15 Nebuchadnezzar took Jehoiachin(AF) captive to Babylon. He also took from Jerusalem to Babylon the king’s mother,(AG) his wives, his officials and the prominent people(AH) of the land. 16 The king of Babylon also deported to Babylon the entire force of seven thousand fighting men, strong and fit for war, and a thousand skilled workers and artisans.(AI) 17 He made Mattaniah, Jehoiachin’s uncle, king in his place and changed his name to Zedekiah.(AJ)

Zedekiah King of Judah(AK)

18 Zedekiah(AL) was twenty-one years old when he became king, and he reigned in Jerusalem eleven years. His mother’s name was Hamutal(AM) daughter of Jeremiah; she was from Libnah. 19 He did evil(AN) in the eyes of the Lord, just as Jehoiakim had done. 20 It was because of the Lord’s anger that all this happened to Jerusalem and Judah, and in the end he thrust(AO) them from his presence.(AP)

The Fall of Jerusalem(AQ)(AR)(AS)

Now Zedekiah rebelled against the king of Babylon.

Footnotes

  1. 2 Kings 24:2 Or Chaldean