Add parallel Print Page Options

25 Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo. Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya. Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya. Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba, koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika. Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo. Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.

Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu. Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika. 10 Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu. 11 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 12 Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.

13 Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni. 14 Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo. 15 Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.

16 Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka. 17 Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.

18 Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo. 19 Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo. 20 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula. 21 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha.

Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.

22 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda. 23 Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo. 24 Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”

25 Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa. 26 Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.

Kumasulidwa kwa Yehoyakini

27 Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27. 28 Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni. 29 Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake. 30 Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

25 So in the ninth(A) year of Zedekiah’s reign, on the tenth day of the tenth month, Nebuchadnezzar(B) king of Babylon marched against Jerusalem with his whole army. He encamped outside the city and built siege works(C) all around it. The city was kept under siege until the eleventh year of King Zedekiah.

By the ninth day of the fourth[a] month the famine(D) in the city had become so severe that there was no food for the people to eat. Then the city wall was broken through,(E) and the whole army fled at night through the gate between the two walls near the king’s garden, though the Babylonians[b] were surrounding(F) the city. They fled toward the Arabah,[c] but the Babylonian[d] army pursued the king and overtook him in the plains of Jericho. All his soldiers were separated from him and scattered,(G) and he was captured.(H)

He was taken to the king of Babylon at Riblah,(I) where sentence was pronounced on him. They killed the sons of Zedekiah before his eyes. Then they put out his eyes, bound him with bronze shackles and took him to Babylon.(J)

On the seventh day of the fifth month, in the nineteenth year of Nebuchadnezzar king of Babylon, Nebuzaradan commander of the imperial guard, an official of the king of Babylon, came to Jerusalem. He set fire(K) to the temple of the Lord, the royal palace and all the houses of Jerusalem. Every important building he burned down.(L) 10 The whole Babylonian army under the commander of the imperial guard broke down the walls(M) around Jerusalem. 11 Nebuzaradan the commander of the guard carried into exile(N) the people who remained in the city, along with the rest of the populace and those who had deserted to the king of Babylon.(O) 12 But the commander left behind some of the poorest people(P) of the land to work the vineyards and fields.

13 The Babylonians broke(Q) up the bronze pillars, the movable stands and the bronze Sea that were at the temple of the Lord and they carried the bronze to Babylon. 14 They also took away the pots, shovels, wick trimmers, dishes(R) and all the bronze articles(S) used in the temple service. 15 The commander of the imperial guard took away the censers and sprinkling bowls—all that were made of pure gold or silver.(T)

16 The bronze from the two pillars, the Sea and the movable stands, which Solomon had made for the temple of the Lord, was more than could be weighed. 17 Each pillar(U) was eighteen cubits[e] high. The bronze capital on top of one pillar was three cubits[f] high and was decorated with a network and pomegranates of bronze all around. The other pillar, with its network, was similar.

18 The commander of the guard took as prisoners Seraiah(V) the chief priest, Zephaniah(W) the priest next in rank and the three doorkeepers.(X) 19 Of those still in the city, he took the officer in charge of the fighting men, and five royal advisers. He also took the secretary who was chief officer in charge of conscripting the people of the land and sixty of the conscripts who were found in the city. 20 Nebuzaradan the commander took them all and brought them to the king of Babylon at Riblah. 21 There at Riblah,(Y) in the land of Hamath, the king had them executed.(Z)

So Judah went into captivity,(AA) away from her land.(AB)

22 Nebuchadnezzar king of Babylon appointed Gedaliah(AC) son of Ahikam,(AD) the son of Shaphan, to be over the people he had left behind in Judah. 23 When all the army officers and their men heard that the king of Babylon had appointed Gedaliah as governor, they came to Gedaliah at Mizpah—Ishmael son of Nethaniah, Johanan son of Kareah, Seraiah son of Tanhumeth the Netophathite, Jaazaniah the son of the Maakathite, and their men. 24 Gedaliah took an oath to reassure them and their men. “Do not be afraid of the Babylonian officials,” he said. “Settle down in the land and serve the king of Babylon, and it will go well with you.”

25 In the seventh month, however, Ishmael son of Nethaniah, the son of Elishama, who was of royal blood, came with ten men and assassinated(AE) Gedaliah and also the men of Judah and the Babylonians who were with him at Mizpah.(AF) 26 At this, all the people from the least to the greatest, together with the army officers, fled to Egypt(AG) for fear of the Babylonians.

Jehoiachin Released(AH)

27 In the thirty-seventh year of the exile of Jehoiachin king of Judah, in the year Awel-Marduk became king of Babylon, he released Jehoiachin(AI) king of Judah from prison. He did this on the twenty-seventh day of the twelfth month. 28 He spoke kindly(AJ) to him and gave him a seat of honor(AK) higher than those of the other kings who were with him in Babylon. 29 So Jehoiachin put aside his prison clothes and for the rest of his life ate regularly at the king’s table.(AL) 30 Day by day the king gave Jehoiachin a regular allowance as long as he lived.(AM)

Footnotes

  1. 2 Kings 25:3 Probable reading of the original Hebrew text (see Jer. 52:6); Masoretic Text does not have fourth.
  2. 2 Kings 25:4 Or Chaldeans; also in verses 13, 25 and 26
  3. 2 Kings 25:4 Or the Jordan Valley
  4. 2 Kings 25:5 Or Chaldean; also in verses 10 and 24
  5. 2 Kings 25:17 That is, about 27 feet or about 8.1 meters
  6. 2 Kings 25:17 That is, about 4 1/2 feet or about 1.4 meters