Add parallel Print Page Options

Solomoni Apempha Nzeru

Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.

Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja. Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja. Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu. Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko. Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.

Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake. Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi. 10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo, 12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”

13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.

14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu. 15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe. 17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.

Solomon Asks for Wisdom(A)(B)

Solomon son of David established(C) himself firmly over his kingdom, for the Lord his God was with(D) him and made him exceedingly great.(E)

Then Solomon spoke to all Israel(F)—to the commanders of thousands and commanders of hundreds, to the judges and to all the leaders in Israel, the heads of families— and Solomon and the whole assembly went to the high place at Gibeon,(G) for God’s tent of meeting(H) was there, which Moses(I) the Lord’s servant had made in the wilderness. Now David had brought up the ark(J) of God from Kiriath Jearim to the place he had prepared for it, because he had pitched a tent(K) for it in Jerusalem. But the bronze altar(L) that Bezalel(M) son of Uri, the son of Hur, had made was in Gibeon in front of the tabernacle of the Lord; so Solomon and the assembly inquired(N) of him there. Solomon went up to the bronze altar before the Lord in the tent of meeting and offered a thousand burnt offerings on it.

That night God appeared(O) to Solomon and said to him, “Ask for whatever you want me to give you.”

Solomon answered God, “You have shown great kindness to David my father and have made me(P) king in his place. Now, Lord God, let your promise(Q) to my father David be confirmed, for you have made me king over a people who are as numerous as the dust of the earth.(R) 10 Give me wisdom and knowledge, that I may lead(S) this people, for who is able to govern this great people of yours?”

11 God said to Solomon, “Since this is your heart’s desire and you have not asked for wealth,(T) possessions or honor, nor for the death of your enemies, and since you have not asked for a long life but for wisdom and knowledge to govern my people over whom I have made you king, 12 therefore wisdom and knowledge will be given you. And I will also give you wealth, possessions and honor,(U) such as no king who was before you ever had and none after you will have.(V)

13 Then Solomon went to Jerusalem from the high place at Gibeon, from before the tent of meeting. And he reigned over Israel.

14 Solomon accumulated chariots(W) and horses; he had fourteen hundred chariots and twelve thousand horses,[a] which he kept in the chariot cities and also with him in Jerusalem. 15 The king made silver and gold(X) as common in Jerusalem as stones, and cedar as plentiful as sycamore-fig trees in the foothills. 16 Solomon’s horses were imported from Egypt and from Kue[b]—the royal merchants purchased them from Kue at the current price. 17 They imported a chariot(Y) from Egypt for six hundred shekels[c] of silver, and a horse for a hundred and fifty.[d] They also exported them to all the kings of the Hittites and of the Arameans.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 1:14 Or charioteers
  2. 2 Chronicles 1:16 Probably Cilicia
  3. 2 Chronicles 1:17 That is, about 15 pounds or about 6.9 kilograms
  4. 2 Chronicles 1:17 That is, about 3 3/4 pounds or about 1.7 kilograms