Add parallel Print Page Options

Yehosafati Mfumu ya Yuda

17 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli. Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.

Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala. Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli. Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri. Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.

Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda. Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu. Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.

10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati. 11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.

12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda 13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu. 14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere:

kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000;

mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;

15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;

16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.

17 Kuchokera ku Benjamini:

Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;

18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.

19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.

Jehoshaphat King of Judah

17 Jehoshaphat his son succeeded him as king and strengthened(A) himself against Israel. He stationed troops in all the fortified cities(B) of Judah and put garrisons in Judah and in the towns of Ephraim that his father Asa had captured.(C)

The Lord was with Jehoshaphat because he followed the ways of his father David(D) before him. He did not consult the Baals but sought(E) the God of his father and followed his commands rather than the practices of Israel. The Lord established the kingdom under his control; and all Judah brought gifts(F) to Jehoshaphat, so that he had great wealth and honor.(G) His heart was devoted(H) to the ways of the Lord; furthermore, he removed the high places(I) and the Asherah poles(J) from Judah.(K)

In the third year of his reign he sent his officials Ben-Hail, Obadiah, Zechariah, Nethanel and Micaiah to teach(L) in the towns of Judah. With them were certain Levites(M)—Shemaiah, Nethaniah, Zebadiah, Asahel, Shemiramoth, Jehonathan, Adonijah, Tobijah and Tob-Adonijah—and the priests Elishama and Jehoram. They taught throughout Judah, taking with them the Book of the Law(N) of the Lord; they went around to all the towns of Judah and taught the people.

10 The fear(O) of the Lord fell on all the kingdoms of the lands surrounding Judah, so that they did not go to war against Jehoshaphat. 11 Some Philistines brought Jehoshaphat gifts and silver as tribute, and the Arabs(P) brought him flocks:(Q) seven thousand seven hundred rams and seven thousand seven hundred goats.

12 Jehoshaphat became more and more powerful; he built forts and store cities in Judah 13 and had large supplies in the towns of Judah. He also kept experienced fighting men in Jerusalem. 14 Their enrollment(R) by families was as follows:

From Judah, commanders of units of 1,000:

Adnah the commander, with 300,000 fighting men;

15 next, Jehohanan the commander, with 280,000;

16 next, Amasiah son of Zikri, who volunteered(S) himself for the service of the Lord, with 200,000.

17 From Benjamin:(T)

Eliada, a valiant soldier, with 200,000 men armed with bows and shields;

18 next, Jehozabad, with 180,000 men armed for battle.

19 These were the men who served the king, besides those he stationed in the fortified cities(U) throughout Judah.(V)