Add parallel Print Page Options

19 Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu. Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”

Yehosafati Asankha Oweruza

Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo. Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda. Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo. Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”

Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu. Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova. 10 Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.

11 “Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

19 When Jehoshaphat king of Judah returned safely to his palace in Jerusalem, Jehu(A) the seer, the son of Hanani, went out to meet him and said to the king, “Should you help the wicked(B) and love[a] those who hate the Lord?(C) Because of this, the wrath(D) of the Lord is on you. There is, however, some good(E) in you, for you have rid the land of the Asherah poles(F) and have set your heart on seeking God.(G)

Jehoshaphat Appoints Judges

Jehoshaphat lived in Jerusalem, and he went out again among the people from Beersheba to the hill country of Ephraim and turned them back to the Lord, the God of their ancestors. He appointed judges(H) in the land, in each of the fortified cities of Judah. He told them, “Consider carefully what you do,(I) because you are not judging for mere mortals(J) but for the Lord, who is with you whenever you give a verdict. Now let the fear of the Lord be on you. Judge carefully, for with the Lord our God there is no injustice(K) or partiality(L) or bribery.”

In Jerusalem also, Jehoshaphat appointed some of the Levites,(M) priests(N) and heads of Israelite families to administer(O) the law of the Lord and to settle disputes. And they lived in Jerusalem. He gave them these orders: “You must serve faithfully and wholeheartedly in the fear of the Lord. 10 In every case that comes before you from your people who live in the cities—whether bloodshed or other concerns of the law, commands, decrees or regulations—you are to warn them not to sin against the Lord;(P) otherwise his wrath will come on you and your people. Do this, and you will not sin.

11 “Amariah the chief priest will be over you in any matter concerning the Lord, and Zebadiah son of Ishmael, the leader of the tribe of Judah, will be over you in any matter concerning the king, and the Levites will serve as officials before you. Act with courage,(Q) and may the Lord be with those who do well.”

Footnotes

  1. 2 Chronicles 19:2 Or and make alliances with