Add parallel Print Page Options

Manase Mfumu ya Yuda

33 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli. Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza. Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.” Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga. Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.

Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya. Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.” Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.

10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko. 11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni. 12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake. 13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.

14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.

15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda. 16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli. 17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.

18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli. 19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi. 20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Amoni Mfumu ya Yuda

21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri. 22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase. 23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.

24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu. 25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.

Manasseh King of Judah(A)(B)

33 Manasseh(C) was twelve years old when he became king, and he reigned in Jerusalem fifty-five years. He did evil in the eyes of the Lord,(D) following the detestable(E) practices of the nations the Lord had driven out before the Israelites. He rebuilt the high places his father Hezekiah had demolished; he also erected altars to the Baals and made Asherah poles.(F) He bowed down(G) to all the starry hosts and worshiped them. He built altars in the temple of the Lord, of which the Lord had said, “My Name(H) will remain in Jerusalem forever.” In both courts of the temple of the Lord,(I) he built altars to all the starry hosts. He sacrificed his children(J) in the fire in the Valley of Ben Hinnom, practiced divination and witchcraft, sought omens, and consulted mediums(K) and spiritists.(L) He did much evil in the eyes of the Lord, arousing his anger.

He took the image he had made and put it in God’s temple,(M) of which God had said to David and to his son Solomon, “In this temple and in Jerusalem, which I have chosen out of all the tribes of Israel, I will put my Name forever. I will not again make the feet of the Israelites leave the land(N) I assigned to your ancestors, if only they will be careful to do everything I commanded them concerning all the laws, decrees and regulations given through Moses.” But Manasseh led Judah and the people of Jerusalem astray, so that they did more evil than the nations the Lord had destroyed before the Israelites.(O)

10 The Lord spoke to Manasseh and his people, but they paid no attention. 11 So the Lord brought against them the army commanders of the king of Assyria, who took Manasseh prisoner,(P) put a hook(Q) in his nose, bound him with bronze shackles(R) and took him to Babylon. 12 In his distress he sought the favor of the Lord his God and humbled(S) himself greatly before the God of his ancestors. 13 And when he prayed to him, the Lord was moved by his entreaty and listened to his plea; so he brought him back to Jerusalem and to his kingdom. Then Manasseh knew that the Lord is God.

14 Afterward he rebuilt the outer wall of the City of David, west of the Gihon(T) spring in the valley, as far as the entrance of the Fish Gate(U) and encircling the hill of Ophel;(V) he also made it much higher. He stationed military commanders in all the fortified cities in Judah.

15 He got rid of the foreign gods and removed(W) the image from the temple of the Lord, as well as all the altars he had built on the temple hill and in Jerusalem; and he threw them out of the city. 16 Then he restored the altar of the Lord and sacrificed fellowship offerings and thank offerings(X) on it, and told Judah to serve the Lord, the God of Israel. 17 The people, however, continued to sacrifice at the high places, but only to the Lord their God.

18 The other events of Manasseh’s reign, including his prayer to his God and the words the seers spoke to him in the name of the Lord, the God of Israel, are written in the annals of the kings of Israel.[a] 19 His prayer and how God was moved by his entreaty, as well as all his sins and unfaithfulness, and the sites where he built high places and set up Asherah poles and idols before he humbled(Y) himself—all these are written in the records of the seers.[b](Z) 20 Manasseh rested with his ancestors and was buried(AA) in his palace. And Amon his son succeeded him as king.

Amon King of Judah(AB)

21 Amon(AC) was twenty-two years old when he became king, and he reigned in Jerusalem two years. 22 He did evil in the eyes of the Lord, as his father Manasseh had done. Amon worshiped and offered sacrifices to all the idols Manasseh had made. 23 But unlike his father Manasseh, he did not humble(AD) himself before the Lord; Amon increased his guilt.

24 Amon’s officials conspired against him and assassinated him in his palace. 25 Then the people(AE) of the land killed all who had plotted against King Amon, and they made Josiah his son king in his place.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 33:18 That is, Judah, as frequently in 2 Chronicles
  2. 2 Chronicles 33:19 One Hebrew manuscript and Septuagint; most Hebrew manuscripts of Hozai