Add parallel Print Page Options

Zipangizo za mʼNyumba ya Mulungu

Solomoni anapanga guwa lamkuwa limene mulitali mwake linali mamita asanu ndi anayi, mulifupi mwakenso mamita asanu ndi anayi ndipo msinkhu wake unali mamita anayi ndi theka. Kenaka iye anapanga mbiya yayikulu yachitsulo. Inali yozungulira ndipo pakamwa pake panali pa mamita anayi ndi theka, poyeza modutsa pakati pake. Msinkhu wake unali wopitirirapo mamita awiri. Thunthu lake linali mamita 13. Mʼmunsi mwa mkombero wa mbiyayo anajambulamo zithunzi zangʼombe zazimuna mozungulira, zithunzi khumi pa theka la mita. Ngʼombezo zimajambulidwa mʼmizere iwiri ndipo anazipangira kumodzi ndi mbiyayo.

Mbiyayo anayisanjika pa ngʼombe zamkuwa khumi ndi ziwiri, zitatu zoyangʼana kumpoto, zitatu zoyangʼana kumadzulo, zitatu zoyangʼana kummwera ndipo zitatu zoyangʼana kummawa. Mbiyayo inakhazikika pamwamba pa ngʼombezo, ndipo miyendo yake yonse yakumbuyo ya ngʼombezo inkaloza mʼkati. Mbiyayo inali yochindikala ngati chikhatho ndipo mkombero wake unali ngati mkombero wa chikho, ngati duwa lokongola kwambiri. Mʼmbiyamo munkalowa madzi okwana malita 60,000.

Kenaka anapanga mabeseni khumi otsukira zinthu ndipo asanu amawayika mbali ya kummwera, asanu mbali ya kumpoto. Mʼmenemo amatsukiramo zinthu zimene zimagwiritsidwa ntchito pa nsembe zopsereza koma mbiyamo ndi mʼmene ankasambiramo ansembe.

Solomoni anapanga zoyikapo nyale khumi zagolide monga momwe kunalembedwera ndipo anaziyika mʼNyumba ya Mulungu, zisanu mbali ya kummwera, ndi zisanu mbali ya kumpoto.

Iye anapanga matebulo khumi ndipo anawayika mʼNyumba ya Mulungu, asanu mbali ya kummwera ndi asanu mbali ya kumpoto. Iye anapanganso mabeseni agolide okwanira 100.

Iye anapanga bwalo la ansembe, bwalo lalikulu ndi zitseko za bwalolo ndipo anakuta zitsekozo ndi mkuwa. 10 Anayika mbiya ija mbali yakummwera pamene mbali ya kummawa ndi kummwera zimakumana.

11 Iye anapanganso miphika ndi mafosholo ndi mabeseni owazira magazi.

Kotero Hiramu anatsiriza ntchito yonse ya ku Nyumba ya Mulungu imene ankagwirira Mfumu Solomoni:

12 Nsanamira ziwiri;

mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

maukonde awiri okongoletsera mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

13 makangadza 400 a maukonde awiri okongoletserawo (mizere iwiri ya makangadza pa ukonde uliwonse, kukongoletsa mbale za mitu yapamwamba pa nsanamira);

14 miyendo pamodzi ndi mabeseni ake;

15 mbiya pamodzi ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri zazimuna zosanjikapo mbiyayo.

16 Miphika, mafosholo, mafoloko otengera nyama ndi ziwiya zina zonse.

Zipangizo zonse zimene Hiramu Abi anapangira Mfumu Solomoni za mʼNyumba ya Yehova zinali zamkuwa wonyezimira. 17 Mfumu inapangitsa zimenezi mʼchigwa cha Yorodani, ku malo amtapo amene anali pakati pa Sukoti ndi Zaretani. 18 Zinthu zonse zimene Solomoni anapanga zinali zochuluka kwambiri kotero kuti kulemera kwa mkuwa sikunadziwike.

19 Solomoni anapanganso ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Mulungu:

guwa lansembe lagolide;

matebulo pamene ankayikapo buledi woperekedwa kwa Mulungu;

20 zoyikapo nyale zagolide ndi nyale zake zagolide weniweni, kuti ziziyaka mʼkati mwenimweni mwa malo opatulika monga analembera,

21 maluwa agolide, nyale ndi mbaniro. (Zinali zagolide mmodzi);

22 zozimitsira nyale zagolide weniweni, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zitseko zagolide za Nyumba ya Mulungu, chitseko cha ku Malo Opatulika Kwambiri ndi zitseko za ku chipinda chachikulu.

The Temple’s Furnishings(A)

He made a bronze altar(B) twenty cubits long, twenty cubits wide and ten cubits high.[a] He made the Sea(C) of cast metal, circular in shape, measuring ten cubits from rim to rim and five cubits[b] high. It took a line of thirty cubits[c] to measure around it. Below the rim, figures of bulls encircled it—ten to a cubit.[d] The bulls were cast in two rows in one piece with the Sea.

The Sea stood on twelve bulls, three facing north, three facing west, three facing south and three facing east.(D) The Sea rested on top of them, and their hindquarters were toward the center. It was a handbreadth[e] in thickness, and its rim was like the rim of a cup, like a lily blossom. It held three thousand baths.[f]

He then made ten basins(E) for washing and placed five on the south side and five on the north. In them the things to be used for the burnt offerings(F) were rinsed, but the Sea was to be used by the priests for washing.

He made ten gold lampstands(G) according to the specifications(H) for them and placed them in the temple, five on the south side and five on the north.

He made ten tables(I) and placed them in the temple, five on the south side and five on the north. He also made a hundred gold sprinkling bowls.(J)

He made the courtyard(K) of the priests, and the large court and the doors for the court, and overlaid the doors with bronze. 10 He placed the Sea on the south side, at the southeast corner.

11 And Huram also made the pots and shovels and sprinkling bowls.

So Huram finished(L) the work he had undertaken for King Solomon in the temple of God:

12 the two pillars;

the two bowl-shaped capitals on top of the pillars;

the two sets of network decorating the two bowl-shaped capitals on top of the pillars;

13 the four hundred pomegranates for the two sets of network (two rows of pomegranates for each network, decorating the bowl-shaped capitals on top of the pillars);

14 the stands(M) with their basins;

15 the Sea and the twelve bulls under it;

16 the pots, shovels, meat forks and all related articles.

All the objects that Huram-Abi(N) made for King Solomon for the temple of the Lord were of polished bronze. 17 The king had them cast in clay molds in the plain of the Jordan between Sukkoth(O) and Zarethan.[g] 18 All these things that Solomon made amounted to so much that the weight of the bronze(P) could not be calculated.

19 Solomon also made all the furnishings that were in God’s temple:

the golden altar;

the tables(Q) on which was the bread of the Presence;

20 the lampstands(R) of pure gold with their lamps, to burn in front of the inner sanctuary as prescribed;

21 the gold floral work and lamps and tongs (they were solid gold);

22 the pure gold wick trimmers, sprinkling bowls, dishes(S) and censers;(T) and the gold doors of the temple: the inner doors to the Most Holy Place and the doors of the main hall.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 4:1 That is, about 30 feet long and wide and 15 feet high or about 9 meters long and wide and 4.5 meters high
  2. 2 Chronicles 4:2 That is, about 7 1/2 feet or about 2.3 meters
  3. 2 Chronicles 4:2 That is, about 45 feet or about 14 meters
  4. 2 Chronicles 4:3 That is, about 18 inches or about 45 centimeters
  5. 2 Chronicles 4:5 That is, about 3 inches or about 7.5 centimeters
  6. 2 Chronicles 4:5 That is, about 18,000 gallons or about 66,000 liters
  7. 2 Chronicles 4:17 Hebrew Zeredatha, a variant of Zarethan