Add parallel Print Page Options

Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu.

Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.

Kudziwa za Mayitanidwe ndi za Kusankhidwa Kwathu

Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake. Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.

Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru. Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu. Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi. Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu. Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.

10 Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse. 11 Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

Kukhala Oyera Mtima

12 Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano. 13 Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani, 14 chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu. 15 Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.

16 Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake. 17 Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.” 18 Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.

19 Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu. 20 Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha. 21 Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

Simon Peter, a servant(A) and apostle of Jesus Christ,(B)

To those who through the righteousness(C) of our God and Savior Jesus Christ(D) have received a faith as precious as ours:

Grace and peace be yours in abundance(E) through the knowledge of God and of Jesus our Lord.(F)

Confirming One’s Calling and Election

His divine power(G) has given us everything we need for a godly life through our knowledge of him(H) who called us(I) by his own glory and goodness. Through these he has given us his very great and precious promises,(J) so that through them you may participate in the divine nature,(K) having escaped the corruption in the world caused by evil desires.(L)

For this very reason, make every effort to add to your faith goodness; and to goodness, knowledge;(M) and to knowledge, self-control;(N) and to self-control, perseverance;(O) and to perseverance, godliness;(P) and to godliness, mutual affection; and to mutual affection, love.(Q) For if you possess these qualities in increasing measure, they will keep you from being ineffective and unproductive(R) in your knowledge of our Lord Jesus Christ.(S) But whoever does not have them is nearsighted and blind,(T) forgetting that they have been cleansed from their past sins.(U)

10 Therefore, my brothers and sisters,[a] make every effort to confirm your calling(V) and election. For if you do these things, you will never stumble,(W) 11 and you will receive a rich welcome into the eternal kingdom(X) of our Lord and Savior Jesus Christ.(Y)

Prophecy of Scripture

12 So I will always remind you of these things,(Z) even though you know them and are firmly established in the truth(AA) you now have. 13 I think it is right to refresh your memory(AB) as long as I live in the tent of this body,(AC) 14 because I know that I will soon put it aside,(AD) as our Lord Jesus Christ has made clear to me.(AE) 15 And I will make every effort to see that after my departure(AF) you will always be able to remember these things.

16 For we did not follow cleverly devised stories when we told you about the coming of our Lord Jesus Christ in power,(AG) but we were eyewitnesses of his majesty.(AH) 17 He received honor and glory from God the Father when the voice came to him from the Majestic Glory, saying, “This is my Son, whom I love; with him I am well pleased.”[b](AI) 18 We ourselves heard this voice that came from heaven when we were with him on the sacred mountain.(AJ)

19 We also have the prophetic message as something completely reliable,(AK) and you will do well to pay attention to it, as to a light(AL) shining in a dark place, until the day dawns(AM) and the morning star(AN) rises in your hearts.(AO) 20 Above all, you must understand(AP) that no prophecy of Scripture came about by the prophet’s own interpretation of things. 21 For prophecy never had its origin in the human will, but prophets, though human, spoke from God(AQ) as they were carried along by the Holy Spirit.(AR)

Footnotes

  1. 2 Peter 1:10 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family.
  2. 2 Peter 1:17 Matt. 17:5; Mark 9:7; Luke 9:35