Add parallel Print Page Options

Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.

Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.

Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli.

Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;

wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti;

wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;

ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide.

Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.

Abineri Agwirizana ndi Davide

Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli. Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”

Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu! Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro. 10 Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.” 11 Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.

12 Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”

13 Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.” 14 Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”

15 Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi. 16 Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.

17 Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu. 18 Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’ ”

19 Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita. 20 Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake. 21 Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.

Yowabu Apha Abineri

22 Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere. 23 Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.

24 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi! 25 Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”

26 Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi. 27 Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.

28 Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri. 29 Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”

30 (Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).

31 Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho. 32 Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.

33 Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri:

“Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34     Manja ako anali osamanga,
    mapazi ako anali osakulungidwa.
Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.”

Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.

35 Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”

36 Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa. 37 Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.

38 Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu? 39 Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

The war between the house of Saul and the house of David lasted a long time.(A) David grew stronger and stronger,(B) while the house of Saul grew weaker and weaker.(C)

Sons were born to David in Hebron:

His firstborn was Amnon(D) the son of Ahinoam(E) of Jezreel;

his second, Kileab the son of Abigail(F) the widow of Nabal of Carmel;

the third, Absalom(G) the son of Maakah daughter of Talmai king of Geshur;(H)

the fourth, Adonijah(I) the son of Haggith;

the fifth, Shephatiah the son of Abital;

and the sixth, Ithream the son of David’s wife Eglah.

These were born to David in Hebron.

Abner Goes Over to David

During the war between the house of Saul and the house of David, Abner(J) had been strengthening his own position in the house of Saul. Now Saul had had a concubine(K) named Rizpah(L) daughter of Aiah. And Ish-Bosheth said to Abner, “Why did you sleep with my father’s concubine?”

Abner was very angry because of what Ish-Bosheth said. So he answered, “Am I a dog’s head(M)—on Judah’s side? This very day I am loyal to the house of your father Saul and to his family and friends. I haven’t handed you over to David. Yet now you accuse me of an offense involving this woman! May God deal with Abner, be it ever so severely, if I do not do for David what the Lord promised(N) him on oath 10 and transfer the kingdom from the house of Saul and establish David’s throne over Israel and Judah from Dan to Beersheba.”(O) 11 Ish-Bosheth did not dare to say another word to Abner, because he was afraid of him.

12 Then Abner sent messengers on his behalf to say to David, “Whose land is it? Make an agreement with me, and I will help you bring all Israel over to you.”

13 “Good,” said David. “I will make an agreement with you. But I demand one thing of you: Do not come into my presence unless you bring Michal daughter of Saul when you come to see me.”(P) 14 Then David sent messengers to Ish-Bosheth son of Saul, demanding, “Give me my wife Michal,(Q) whom I betrothed to myself for the price of a hundred Philistine foreskins.”

15 So Ish-Bosheth gave orders and had her taken away from her husband(R) Paltiel(S) son of Laish. 16 Her husband, however, went with her, weeping behind her all the way to Bahurim.(T) Then Abner said to him, “Go back home!” So he went back.

17 Abner conferred with the elders(U) of Israel and said, “For some time you have wanted to make David your king. 18 Now do it! For the Lord promised David, ‘By my servant David I will rescue my people Israel from the hand of the Philistines(V) and from the hand of all their enemies.(W)’”

19 Abner also spoke to the Benjamites in person. Then he went to Hebron to tell David everything that Israel and the whole tribe of Benjamin(X) wanted to do. 20 When Abner, who had twenty men with him, came to David at Hebron, David prepared a feast(Y) for him and his men. 21 Then Abner said to David, “Let me go at once and assemble all Israel for my lord the king, so that they may make a covenant(Z) with you, and that you may rule over all that your heart desires.”(AA) So David sent Abner away, and he went in peace.

Joab Murders Abner

22 Just then David’s men and Joab returned from a raid and brought with them a great deal of plunder. But Abner was no longer with David in Hebron, because David had sent him away, and he had gone in peace. 23 When Joab and all the soldiers with him arrived, he was told that Abner son of Ner had come to the king and that the king had sent him away and that he had gone in peace.

24 So Joab went to the king and said, “What have you done? Look, Abner came to you. Why did you let him go? Now he is gone! 25 You know Abner son of Ner; he came to deceive you and observe your movements and find out everything you are doing.”

26 Joab then left David and sent messengers after Abner, and they brought him back from the cistern at Sirah. But David did not know it. 27 Now when Abner(AB) returned to Hebron, Joab took him aside into an inner chamber, as if to speak with him privately. And there, to avenge the blood of his brother Asahel, Joab stabbed him(AC) in the stomach, and he died.(AD)

28 Later, when David heard about this, he said, “I and my kingdom are forever innocent(AE) before the Lord concerning the blood of Abner son of Ner. 29 May his blood(AF) fall on the head of Joab and on his whole family!(AG) May Joab’s family never be without someone who has a running sore(AH) or leprosy[a] or who leans on a crutch or who falls by the sword or who lacks food.”

30 (Joab and his brother Abishai murdered Abner because he had killed their brother Asahel in the battle at Gibeon.)

31 Then David said to Joab and all the people with him, “Tear your clothes and put on sackcloth(AI) and walk in mourning(AJ) in front of Abner.” King David himself walked behind the bier. 32 They buried Abner in Hebron, and the king wept(AK) aloud at Abner’s tomb. All the people wept also.

33 The king sang this lament(AL) for Abner:

“Should Abner have died as the lawless die?
34     Your hands were not bound,
    your feet were not fettered.(AM)
You fell as one falls before the wicked.”

And all the people wept over him again.

35 Then they all came and urged David to eat something while it was still day; but David took an oath, saying, “May God deal with me, be it ever so severely,(AN) if I taste bread(AO) or anything else before the sun sets!”

36 All the people took note and were pleased; indeed, everything the king did pleased them. 37 So on that day all the people there and all Israel knew that the king had no part(AP) in the murder of Abner son of Ner.

38 Then the king said to his men, “Do you not realize that a commander and a great man has fallen(AQ) in Israel this day? 39 And today, though I am the anointed king, I am weak, and these sons of Zeruiah(AR) are too strong(AS) for me.(AT) May the Lord repay(AU) the evildoer according to his evil deeds!”

Footnotes

  1. 2 Samuel 3:29 The Hebrew for leprosy was used for various diseases affecting the skin.