Add parallel Print Page Options

Davide ndi Mefiboseti

Davide anafunsa kuti, “Kodi alipo amene watsala mʼbanja la Sauli kuti ndimuchitire chifundo chifukwa cha Yonatani?”

Tsono panali mtumiki wina wa banja la Sauli wotchedwa Ziba. Iwo anamuyitana kuti aonekere pamaso pa Davide, ndipo mfumu inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe Ziba?”

Iyeyo anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”

Mfumu inafunsa kuti, “Kodi palibe amene watsala wa banja la Sauli amene ndingamuchitire chifundo cha Mulungu?”

Ziba anayankha mfumu kuti, “Alipo mwana wa Yonatani, koma ndi wolumala mapazi ake onse.”

Mfumu inafunsa kuti, “Ali kuti?”

Ziba anayankha kuti, “Iye ali ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli ku Lodebara.”

Kotero mfumu inamubweretsa kuchokera ku Lodebara, ku nyumba ya Makiri mwana wa Amieli.

Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli atafika kwa Davide, anawerama pansi kupereka ulemu kwa iye.

Davide anati, “Mefiboseti!”

Iye anayankha kuti, “Ine mtumiki wanu.”

Davide anati kwa iye, “Usachite mantha, pakuti ndidzakuchitira ndithu chifundo chifukwa cha abambo ako Yonatani. Ine ndidzakubwezera iwe dziko lonse limene linali la agogo ako Sauli, ndipo iweyo udzadya ndi ine nthawi zonse.”

Mefiboseti anawerama pansi ndipo anati, “Mtumiki wanu ndine yani kuti musamale galu wakufa ngati ine?”

Kenaka Davide anayitanitsa Ziba, mtumiki wa Sauli, ndipo anati, “Ine ndapereka kwa chidzukulu cha mbuye wako chilichonse chimene chinali cha Sauli ndi banja lake. 10 Iwe ndi ana ndi antchito anu muzimulimira mʼdziko lake ndipo muzibweretsa zokololazo kuti chidzukulu cha mbuye wako chikhale ndi chakudya. Ndipo Mefiboseti, chidzukulu cha mbuye wako adzadya ndi ine nthawi zonse.” (Tsono Ziba anali ndi ana aamuna khumi ndi asanu ndi antchito makumi awiri).

11 Ndipo Ziba anati kwa mfumu, “Mtumiki wanu adzachita chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mudzalamulire wantchito wanu kuti achite.” Kotero Mefiboseti ankadya ndi Davide monga mmodzi wa ana a mfumu.

12 Mefiboseti anali ndi mwana wamngʼono wamwamuna wotchedwa Mika, ndipo onse a banja la Ziba anali antchito a Mefiboseti. 13 Ndipo Mefiboseti anakhala mu Yerusalemu chifukwa nthawi zonse amadya ndi mfumu. Iye anali wolumala mapazi ake onse.

David and Mephibosheth

David asked, “Is there anyone still left of the house of Saul to whom I can show kindness for Jonathan’s sake?”(A)

Now there was a servant of Saul’s household named Ziba.(B) They summoned him to appear before David, and the king said to him, “Are you Ziba?”

“At your service,” he replied.

The king asked, “Is there no one still alive from the house of Saul to whom I can show God’s kindness?”

Ziba answered the king, “There is still a son of Jonathan;(C) he is lame(D) in both feet.”

“Where is he?” the king asked.

Ziba answered, “He is at the house of Makir(E) son of Ammiel in Lo Debar.”

So King David had him brought from Lo Debar, from the house of Makir son of Ammiel.

When Mephibosheth son of Jonathan, the son of Saul, came to David, he bowed down to pay him honor.(F)

David said, “Mephibosheth!”

“At your service,” he replied.

“Don’t be afraid,” David said to him, “for I will surely show you kindness for the sake of your father Jonathan.(G) I will restore to you all the land that belonged to your grandfather Saul, and you will always eat at my table.(H)

Mephibosheth(I) bowed down and said, “What is your servant, that you should notice a dead dog(J) like me?”

Then the king summoned Ziba, Saul’s steward, and said to him, “I have given your master’s grandson everything that belonged to Saul and his family. 10 You and your sons and your servants are to farm the land for him and bring in the crops, so that your master’s grandson(K) may be provided for. And Mephibosheth, grandson of your master, will always eat at my table.” (Now Ziba had fifteen sons and twenty servants.)

11 Then Ziba said to the king, “Your servant will do whatever my lord the king commands his servant to do.” So Mephibosheth ate at David’s[a] table like one of the king’s sons.(L)

12 Mephibosheth had a young son named Mika, and all the members of Ziba’s household were servants of Mephibosheth.(M) 13 And Mephibosheth lived in Jerusalem, because he always ate at the king’s table; he was lame in both feet.

Footnotes

  1. 2 Samuel 9:11 Septuagint; Hebrew my