Add parallel Print Page Options

Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10 Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11 Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12 Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13 Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14 Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15 Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16 Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17 Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18 Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Paul, an apostle(A) of Christ Jesus by the will of God,(B) in keeping with the promise of life that is in Christ Jesus,(C)

To Timothy,(D) my dear son:(E)

Grace, mercy and peace from God the Father and Christ Jesus our Lord.(F)

Thanksgiving

I thank God,(G) whom I serve, as my ancestors did, with a clear conscience,(H) as night and day I constantly remember you in my prayers.(I) Recalling your tears,(J) I long to see you,(K) so that I may be filled with joy. I am reminded of your sincere faith,(L) which first lived in your grandmother Lois and in your mother Eunice(M) and, I am persuaded, now lives in you also.

Appeal for Loyalty to Paul and the Gospel

For this reason I remind you to fan into flame the gift of God, which is in you through the laying on of my hands.(N) For the Spirit God gave us does not make us timid,(O) but gives us power,(P) love and self-discipline. So do not be ashamed(Q) of the testimony about our Lord or of me his prisoner.(R) Rather, join with me in suffering for the gospel,(S) by the power of God. He has saved(T) us and called(U) us to a holy life—not because of anything we have done(V) but because of his own purpose and grace. This grace was given us in Christ Jesus before the beginning of time, 10 but it has now been revealed(W) through the appearing of our Savior, Christ Jesus,(X) who has destroyed death(Y) and has brought life and immortality to light through the gospel. 11 And of this gospel(Z) I was appointed(AA) a herald and an apostle and a teacher.(AB) 12 That is why I am suffering as I am. Yet this is no cause for shame,(AC) because I know whom I have believed, and am convinced that he is able to guard(AD) what I have entrusted to him until that day.(AE)

13 What you heard from me,(AF) keep(AG) as the pattern(AH) of sound teaching,(AI) with faith and love in Christ Jesus.(AJ) 14 Guard(AK) the good deposit that was entrusted to you—guard it with the help of the Holy Spirit who lives in us.(AL)

Examples of Disloyalty and Loyalty

15 You know that everyone in the province of Asia(AM) has deserted me,(AN) including Phygelus and Hermogenes.

16 May the Lord show mercy to the household of Onesiphorus,(AO) because he often refreshed me and was not ashamed(AP) of my chains.(AQ) 17 On the contrary, when he was in Rome, he searched hard for me until he found me. 18 May the Lord grant that he will find mercy from the Lord on that day!(AR) You know very well in how many ways he helped me(AS) in Ephesus.(AT)