Add parallel Print Page Options

Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu. Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse. Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana. 10 Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni. 11 Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.

12 Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.

13 Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

The elder,(A)

To the lady chosen by God(B) and to her children, whom I love in the truth(C)—and not I only, but also all who know the truth(D) because of the truth,(E) which lives in us(F) and will be with us forever:

Grace, mercy and peace from God the Father and from Jesus Christ,(G) the Father’s Son, will be with us in truth and love.

It has given me great joy to find some of your children walking in the truth,(H) just as the Father commanded us. And now, dear lady, I am not writing you a new command but one we have had from the beginning.(I) I ask that we love one another. And this is love:(J) that we walk in obedience to his commands.(K) As you have heard from the beginning,(L) his command is that you walk in love.

I say this because many deceivers, who do not acknowledge Jesus Christ(M) as coming in the flesh,(N) have gone out into the world.(O) Any such person is the deceiver and the antichrist.(P) Watch out that you do not lose what we[a] have worked for, but that you may be rewarded fully.(Q) Anyone who runs ahead and does not continue in the teaching of Christ(R) does not have God; whoever continues in the teaching has both the Father and the Son.(S) 10 If anyone comes to you and does not bring this teaching, do not take them into your house or welcome them.(T) 11 Anyone who welcomes them shares(U) in their wicked work.

12 I have much to write to you, but I do not want to use paper and ink. Instead, I hope to visit you and talk with you face to face,(V) so that our joy may be complete.(W)

13 The children of your sister, who is chosen by God,(X) send their greetings.

Footnotes

  1. 2 John 1:8 Some manuscripts you