Add parallel Print Page Options

Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15 Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16 ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17 Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18 Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19 Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20 imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21 Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22 Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23 umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

Paul, an apostle(A) of Christ Jesus by the will of God,(B)

To God’s holy people(C) in Ephesus,[a](D) the faithful(E) in Christ Jesus:

Grace and peace to you from God our Father and the Lord Jesus Christ.(F)

Praise for Spiritual Blessings in Christ

Praise be to the God and Father of our Lord Jesus Christ,(G) who has blessed us in the heavenly realms(H) with every spiritual blessing in Christ. For he chose us(I) in him before the creation of the world(J) to be holy and blameless(K) in his sight. In love(L) he[b] predestined(M) us for adoption to sonship[c](N) through Jesus Christ, in accordance with his pleasure(O) and will— to the praise of his glorious grace,(P) which he has freely given us in the One he loves.(Q) In him we have redemption(R) through his blood,(S) the forgiveness of sins, in accordance with the riches(T) of God’s grace that he lavished on us. With all wisdom and understanding, he[d] made known to us the mystery(U) of his will according to his good pleasure, which he purposed(V) in Christ, 10 to be put into effect when the times reach their fulfillment(W)—to bring unity to all things in heaven and on earth under Christ.(X)

11 In him we were also chosen,[e] having been predestined(Y) according to the plan of him who works out everything in conformity with the purpose(Z) of his will, 12 in order that we, who were the first to put our hope in Christ, might be for the praise of his glory.(AA) 13 And you also were included in Christ(AB) when you heard the message of truth,(AC) the gospel of your salvation. When you believed, you were marked in him with a seal,(AD) the promised Holy Spirit,(AE) 14 who is a deposit guaranteeing our inheritance(AF) until the redemption(AG) of those who are God’s possession—to the praise of his glory.(AH)

Thanksgiving and Prayer

15 For this reason, ever since I heard about your faith in the Lord Jesus(AI) and your love for all God’s people,(AJ) 16 I have not stopped giving thanks for you,(AK) remembering you in my prayers.(AL) 17 I keep asking that the God of our Lord Jesus Christ, the glorious Father,(AM) may give you the Spirit[f] of wisdom(AN) and revelation, so that you may know him better. 18 I pray that the eyes of your heart may be enlightened(AO) in order that you may know the hope to which he has called(AP) you, the riches(AQ) of his glorious inheritance(AR) in his holy people,(AS) 19 and his incomparably great power for us who believe. That power(AT) is the same as the mighty strength(AU) 20 he exerted when he raised Christ from the dead(AV) and seated him at his right hand(AW) in the heavenly realms,(AX) 21 far above all rule and authority, power and dominion,(AY) and every name(AZ) that is invoked, not only in the present age but also in the one to come.(BA) 22 And God placed all things under his feet(BB) and appointed him to be head(BC) over everything for the church, 23 which is his body,(BD) the fullness of him(BE) who fills everything in every way.(BF)

Footnotes

  1. Ephesians 1:1 Some early manuscripts do not have in Ephesus.
  2. Ephesians 1:5 Or sight in love. He
  3. Ephesians 1:5 The Greek word for adoption to sonship is a legal term referring to the full legal standing of an adopted male heir in Roman culture.
  4. Ephesians 1:9 Or us with all wisdom and understanding. And he
  5. Ephesians 1:11 Or were made heirs
  6. Ephesians 1:17 Or a spirit