Afilipi 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kutsanzira Kudzichepetsa kwa Khristu
2 Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2 tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3 Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4 Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.
5 Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:
6 Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,
sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.
7 Koma anadzichepetsa kotheratu
nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo
ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.
8 Ndipo pokhala munthu choncho
anadzichepetsa yekha
ndipo anamvera mpaka imfa yake,
imfa yake ya pamtanda!
9 Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,
ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse
10 kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,
kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,
11 ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye
kuchitira ulemu Mulungu Atate.
Kuwala monga Nyenyezi
12 Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13 pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.
14 Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15 kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16 powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17 Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18 Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.
Timoteyo ndi Epafrodito
19 Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20 Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21 Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22 Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23 Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24 Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.
25 Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26 Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27 Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28 Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29 Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30 Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.
Philippians 2
New International Version
Imitating Christ’s Humility
2 Therefore if you have any encouragement from being united with Christ, if any comfort from his love, if any common sharing in the Spirit,(A) if any tenderness and compassion,(B) 2 then make my joy complete(C) by being like-minded,(D) having the same love, being one(E) in spirit and of one mind. 3 Do nothing out of selfish ambition or vain conceit.(F) Rather, in humility value others above yourselves,(G) 4 not looking to your own interests but each of you to the interests of the others.(H)
5 In your relationships with one another, have the same mindset as Christ Jesus:(I)
6 Who, being in very nature[a] God,(J)
did not consider equality with God(K) something to be used to his own advantage;
7 rather, he made himself nothing(L)
by taking the very nature[b] of a servant,(M)
being made in human likeness.(N)
8 And being found in appearance as a man,
he humbled himself
by becoming obedient to death(O)—
even death on a cross!(P)
9 Therefore God exalted him(Q) to the highest place
and gave him the name that is above every name,(R)
10 that at the name of Jesus every knee should bow,(S)
in heaven and on earth and under the earth,(T)
11 and every tongue acknowledge that Jesus Christ is Lord,(U)
to the glory of God the Father.
Do Everything Without Grumbling
12 Therefore, my dear friends, as you have always obeyed—not only in my presence, but now much more in my absence—continue to work out your salvation with fear and trembling,(V) 13 for it is God who works in you(W) to will and to act in order to fulfill his good purpose.(X)
14 Do everything without grumbling(Y) or arguing, 15 so that you may become blameless(Z) and pure, “children of God(AA) without fault in a warped and crooked generation.”[c](AB) Then you will shine among them like stars in the sky 16 as you hold firmly to the word of life. And then I will be able to boast on the day of Christ(AC) that I did not run(AD) or labor in vain.(AE) 17 But even if I am being poured out like a drink offering(AF) on the sacrifice(AG) and service coming from your faith, I am glad and rejoice with all of you.(AH) 18 So you too should be glad and rejoice with me.
Timothy and Epaphroditus
19 I hope in the Lord Jesus to send Timothy(AI) to you soon,(AJ) that I also may be cheered when I receive news about you. 20 I have no one else like him,(AK) who will show genuine concern for your welfare. 21 For everyone looks out for their own interests,(AL) not those of Jesus Christ. 22 But you know that Timothy has proved himself, because as a son with his father(AM) he has served with me in the work of the gospel. 23 I hope, therefore, to send him as soon as I see how things go with me.(AN) 24 And I am confident(AO) in the Lord that I myself will come soon.
25 But I think it is necessary to send back to you Epaphroditus, my brother, co-worker(AP) and fellow soldier,(AQ) who is also your messenger, whom you sent to take care of my needs.(AR) 26 For he longs for all of you(AS) and is distressed because you heard he was ill. 27 Indeed he was ill, and almost died. But God had mercy on him, and not on him only but also on me, to spare me sorrow upon sorrow. 28 Therefore I am all the more eager to send him,(AT) so that when you see him again you may be glad and I may have less anxiety. 29 So then, welcome him in the Lord with great joy, and honor people like him,(AU) 30 because he almost died for the work of Christ. He risked his life to make up for the help you yourselves could not give me.(AV)
Footnotes
- Philippians 2:6 Or in the form of
- Philippians 2:7 Or the form
- Philippians 2:15 Deut. 32:5
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.