Add parallel Print Page Options

Osakhulupirira za Thupi

Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.

Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.

Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.

Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10 Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11 kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.

Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro

12 Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13 Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14 Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.

Kutsanzira Paulo

15 Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16 Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

17 Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18 Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19 Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20 Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21 Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.

No Confidence in the Flesh

Further, my brothers and sisters, rejoice in the Lord! It is no trouble for me to write the same things to you again,(A) and it is a safeguard for you. Watch out for those dogs,(B) those evildoers, those mutilators of the flesh. For it is we who are the circumcision,(C) we who serve God by his Spirit, who boast in Christ Jesus,(D) and who put no confidence in the flesh— though I myself have reasons for such confidence.(E)

If someone else thinks they have reasons to put confidence in the flesh, I have more: circumcised(F) on the eighth day, of the people of Israel,(G) of the tribe of Benjamin,(H) a Hebrew of Hebrews; in regard to the law, a Pharisee;(I) as for zeal,(J) persecuting the church;(K) as for righteousness based on the law,(L) faultless.

But whatever were gains to me I now consider loss(M) for the sake of Christ. What is more, I consider everything a loss because of the surpassing worth of knowing(N) Christ Jesus my Lord, for whose sake I have lost all things. I consider them garbage, that I may gain Christ(O) and be found in him, not having a righteousness of my own that comes from the law,(P) but that which is through faith in[a] Christ—the righteousness(Q) that comes from God on the basis of faith.(R) 10 I want to know(S) Christ—yes, to know the power of his resurrection and participation in his sufferings,(T) becoming like him in his death,(U) 11 and so, somehow, attaining to the resurrection(V) from the dead.

12 Not that I have already obtained all this, or have already arrived at my goal,(W) but I press on to take hold(X) of that for which Christ Jesus took hold of me.(Y) 13 Brothers and sisters, I do not consider myself yet to have taken hold of it. But one thing I do: Forgetting what is behind(Z) and straining toward what is ahead, 14 I press on(AA) toward the goal to win the prize(AB) for which God has called(AC) me heavenward in Christ Jesus.

Following Paul’s Example

15 All of us, then, who are mature(AD) should take such a view of things.(AE) And if on some point you think differently, that too God will make clear to you.(AF) 16 Only let us live up to what we have already attained.

17 Join together in following my example,(AG) brothers and sisters, and just as you have us as a model, keep your eyes on those who live as we do.(AH) 18 For, as I have often told you before and now tell you again even with tears,(AI) many live as enemies of the cross of Christ.(AJ) 19 Their destiny(AK) is destruction, their god is their stomach,(AL) and their glory is in their shame.(AM) Their mind is set on earthly things.(AN) 20 But our citizenship(AO) is in heaven.(AP) And we eagerly await a Savior from there, the Lord Jesus Christ,(AQ) 21 who, by the power(AR) that enables him to bring everything under his control, will transform our lowly bodies(AS) so that they will be like his glorious body.(AT)

Footnotes

  1. Philippians 3:9 Or through the faithfulness of