Add parallel Print Page Options

Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa, pamodzi ndi abale onse amene ali nane,

Kulembera mipingo ya ku Galatiya:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu. Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni.

Uthenga Wabwino ndi Umodzi Wokha

Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana, umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu. Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa! Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”

10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.

Paulo Woyitanidwa ndi Mulungu

11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi. 12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.

13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga. 14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu. 15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa 16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense. 17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.

18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu. 19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye. 20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi. 21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya. 22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu. 23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.” 24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

Paul, an apostle(A)—sent not from men nor by a man,(B) but by Jesus Christ(C) and God the Father,(D) who raised him from the dead(E) and all the brothers and sisters[a] with me,(F)

To the churches in Galatia:(G)

Grace and peace to you from God our Father and the Lord Jesus Christ,(H) who gave himself for our sins(I) to rescue us from the present evil age,(J) according to the will of our God and Father,(K) to whom be glory for ever and ever. Amen.(L)

No Other Gospel

I am astonished that you are so quickly deserting the one who called(M) you to live in the grace of Christ and are turning to a different gospel(N) which is really no gospel at all. Evidently some people are throwing you into confusion(O) and are trying to pervert(P) the gospel of Christ. But even if we or an angel from heaven should preach a gospel other than the one we preached to you,(Q) let them be under God’s curse!(R) As we have already said, so now I say again: If anybody is preaching to you a gospel other than what you accepted,(S) let them be under God’s curse!

10 Am I now trying to win the approval of human beings, or of God? Or am I trying to please people?(T) If I were still trying to please people, I would not be a servant of Christ.

Paul Called by God

11 I want you to know, brothers and sisters,(U) that the gospel I preached(V) is not of human origin. 12 I did not receive it from any man,(W) nor was I taught it; rather, I received it by revelation(X) from Jesus Christ.(Y)

13 For you have heard of my previous way of life in Judaism,(Z) how intensely I persecuted the church of God(AA) and tried to destroy it.(AB) 14 I was advancing in Judaism beyond many of my own age among my people and was extremely zealous(AC) for the traditions of my fathers.(AD) 15 But when God, who set me apart from my mother’s womb(AE) and called me(AF) by his grace, was pleased 16 to reveal his Son in me so that I might preach him among the Gentiles,(AG) my immediate response was not to consult any human being.(AH) 17 I did not go up to Jerusalem to see those who were apostles before I was, but I went into Arabia. Later I returned to Damascus.(AI)

18 Then after three years,(AJ) I went up to Jerusalem(AK) to get acquainted with Cephas[b] and stayed with him fifteen days. 19 I saw none of the other apostles—only James,(AL) the Lord’s brother. 20 I assure you before God(AM) that what I am writing you is no lie.(AN)

21 Then I went to Syria(AO) and Cilicia.(AP) 22 I was personally unknown to the churches of Judea(AQ) that are in Christ.(AR) 23 They only heard the report: “The man who formerly persecuted us is now preaching the faith(AS) he once tried to destroy.”(AT) 24 And they praised God(AU) because of me.

Footnotes

  1. Galatians 1:2 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family; also in verse 11; and in 3:15; 4:12, 28, 31; 5:11, 13; 6:1, 18.
  2. Galatians 1:18 That is, Peter