Add parallel Print Page Options

Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuchokera pakati pa anthu ndipo amayikidwa kuti aziwayimirira pamaso pa Mulungu, kuti azipereka mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo. Popeza kuti iye mwini ali ndi zofowoka zake, amatha kuwalezera mtima amene ali osadziwa ndi osochera. Chifukwa cha ichi, iye amadziperekera nsembe chifukwa cha machimo ake omwe ndiponso chifukwa cha machimo a anthu ena.

Palibe amene amadzipatsa yekha ulemu wotere, koma amachita kuyitanidwa ndi Mulungu monga momwe anayitanidwira Aaroni. Nʼchifukwa chake Khristu sanadzipatse yekha ulemu wokhala Mkulu wa ansembe. Koma Mulungu anamuwuza kuti,

“Iwe ndiwe Mwana wanga;
    Ine lero ndakhala Atate ako.”

Ndipo penanso anati,

“Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya,
    monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

Yesu, pa nthawi imene anali munthu pa dziko lapansi pano, anapereka mapemphero ake ndi zopempha mofuwula ndi misozi kwa Iye amene akanamupulumutsa ku imfa, ndipo anamumvera chifukwa anagonjera modzipereka. Ngakhale Iye anali Mwana wa Mulungu anaphunzira kumvera pomva zowawa. Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. 10 Ndipo Mulungu anamuyika kukhala Mkulu wa ansembe, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.

Awachenjeza kuti Asataye Chikhulupiriro

11 Tili ndi zambiri zoti tinganene pa zimenezi, koma ndi zovuta kukufotokozerani chifukwa ndinu ochedwa kuphunzira. 12 Ngakhale kuti pa nthawi ino munayenera kukhala aphunzitsi, pakufunikabe munthu wina kuti abwerezenso kudzakuphunzitsani maphunziro oyambira a choonadi cha Mulungu. Ndinu ofunika mkaka osati chakudya cholimba! 13 Aliyense amene amangodya mkaka okha, akanali mwana wakhanda, sakudziwa bwino chiphunzitso cha chilungamo. 14 Koma chakudya cholimba ndi cha anthu okhwima msinkhu, amene pogwiritsa ntchito nzeru zawo, aphunzira kusiyanitsa chabwino ndi choyipa.

Every high priest is selected from among the people and is appointed to represent the people in matters related to God,(A) to offer gifts and sacrifices(B) for sins.(C) He is able to deal gently with those who are ignorant and are going astray,(D) since he himself is subject to weakness.(E) This is why he has to offer sacrifices for his own sins, as well as for the sins of the people.(F) And no one takes this honor on himself, but he receives it when called by God, just as Aaron was.(G)

In the same way, Christ did not take on himself the glory(H) of becoming a high priest.(I) But God said(J) to him,

“You are my Son;
    today I have become your Father.”[a](K)

And he says in another place,

“You are a priest forever,
    in the order of Melchizedek.(L)[b](M)

During the days of Jesus’ life on earth, he offered up prayers and petitions(N) with fervent cries and tears(O) to the one who could save him from death, and he was heard(P) because of his reverent submission.(Q) Son(R) though he was, he learned obedience from what he suffered(S) and, once made perfect,(T) he became the source of eternal salvation for all who obey him 10 and was designated by God to be high priest(U) in the order of Melchizedek.(V)

Warning Against Falling Away(W)

11 We have much to say about this, but it is hard to make it clear to you because you no longer try to understand. 12 In fact, though by this time you ought to be teachers, you need someone to teach you the elementary truths(X) of God’s word all over again. You need milk, not solid food!(Y) 13 Anyone who lives on milk, being still an infant,(Z) is not acquainted with the teaching about righteousness. 14 But solid food is for the mature,(AA) who by constant use have trained themselves to distinguish good from evil.(AB)

Footnotes

  1. Hebrews 5:5 Psalm 2:7
  2. Hebrews 5:6 Psalm 110:4