Amosi 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,
mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.
Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,
mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 Ndidzawononga wolamulira wake
ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”
akutero Yehova.
4 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo akana lamulo la Yehova
ndipo sanasunge malangizo ake,
popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,
milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,
umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
Chilango cha Anthu a ku Israeli
6 Yehova akuti,
“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,
Ine sindileka kuwalanga.
Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,
ndi osauka ndi nsapato.
7 Amapondereza anthu osauka
ngati akuponda fumbi,
ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.
Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,
ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe
pa zovala zimene anatenga ngati chikole.
Mʼnyumba ya mulungu wawo
amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,
ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza
ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.
Ndinawononga zipatso zawo
ndiponso mizu yawo.
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto,
ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,
kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,
ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.
Kodi si choncho, inu Aisraeli?”
akutero Yehova.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,
ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani
monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,
munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,
wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Munthu wa uta sadzalimbika,
msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,
ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri
adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”
akutero Yehova.
Amos 2
New International Version
2 This is what the Lord says:
“For three sins of Moab,(A)
even for four, I will not relent.
Because he burned to ashes(B)
the bones of Edom’s king,
2 I will send fire on Moab
that will consume the fortresses of Kerioth.[a](C)
Moab will go down in great tumult
amid war cries(D) and the blast of the trumpet.(E)
3 I will destroy her ruler(F)
and kill all her officials with him,”(G)
says the Lord.(H)
4 This is what the Lord says:
“For three sins of Judah,(I)
even for four, I will not relent.
Because they have rejected the law(J) of the Lord
and have not kept his decrees,(K)
because they have been led astray(L) by false gods,[b](M)
the gods[c] their ancestors followed,(N)
5 I will send fire(O) on Judah
that will consume the fortresses(P) of Jerusalem.(Q)”
Judgment on Israel
6 This is what the Lord says:
“For three sins of Israel,
even for four, I will not relent.(R)
They sell the innocent for silver,
and the needy for a pair of sandals.(S)
7 They trample on the heads of the poor
as on the dust of the ground
and deny justice to the oppressed.
Father and son use the same girl
and so profane my holy name.(T)
8 They lie down beside every altar
on garments taken in pledge.(U)
In the house of their god
they drink wine(V) taken as fines.(W)
9 “Yet I destroyed the Amorites(X) before them,
though they were tall(Y) as the cedars
and strong as the oaks.(Z)
I destroyed their fruit above
and their roots(AA) below.
10 I brought you up out of Egypt(AB)
and led(AC) you forty years in the wilderness(AD)
to give you the land of the Amorites.(AE)
11 “I also raised up prophets(AF) from among your children
and Nazirites(AG) from among your youths.
Is this not true, people of Israel?”
declares the Lord.
12 “But you made the Nazirites drink wine
and commanded the prophets not to prophesy.(AH)
13 “Now then, I will crush you
as a cart crushes when loaded with grain.(AI)
14 The swift will not escape,(AJ)
the strong(AK) will not muster their strength,
and the warrior will not save his life.(AL)
15 The archer(AM) will not stand his ground,
the fleet-footed soldier will not get away,
and the horseman(AN) will not save his life.(AO)
16 Even the bravest warriors(AP)
will flee naked on that day,”
declares the Lord.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.