Add parallel Print Page Options

Mboni Zotsutsa Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:

“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani
    pakati pa mabanja onse a dziko lapansi;
nʼchifukwa chake ndidzakulangani
    chifukwa cha machimo anu onse.”

Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi
    asanapangane?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango
    usanagwire nyama?
Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake
    pamene sunagwire kanthu?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha
    pamene palibe nyambo yake?
Kodi msampha umafwamphuka
    usanakole kanthu?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda,
    anthu sanjenjemera?
Pamene tsoka lafika mu mzinda,
    kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?

Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu
    asanawulule zimene akufuna kuchita
    kwa atumiki ake, aneneri.

Mkango wabangula,
    ndani amene sachita mantha?
Ambuye Yehova wayankhula,
    ndani amene sanganenere?

Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi
    ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto:
“Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya;
    onani chisokonezo pakati pake
    ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”

10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama,
    ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.

11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi:

“Mdani adzalizungulira dzikoli;
    iye adzagwetsa malinga ako,
    ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”

12 Yehova akuti,

“Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango
    miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu,
    moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli
amene amakhala mu Samariya
    pa msonga za mabedi awo,
    ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”

13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake,
    ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli;
nyanga za guwa zidzathyoka
    ndipo zidzagwa pansi.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira
    pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha;
nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa
    ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,”
            akutero Yehova.

Witnesses Summoned Against Israel

Hear this word, people of Israel, the word the Lord has spoken against you(A)—against the whole family I brought up out of Egypt:(B)

“You only have I chosen(C)
    of all the families of the earth;
therefore I will punish(D) you
    for all your sins.(E)

Do two walk together
    unless they have agreed to do so?
Does a lion roar(F) in the thicket
    when it has no prey?(G)
Does it growl in its den
    when it has caught nothing?
Does a bird swoop down to a trap on the ground
    when no bait(H) is there?
Does a trap spring up from the ground
    if it has not caught anything?
When a trumpet(I) sounds in a city,
    do not the people tremble?
When disaster(J) comes to a city,
    has not the Lord caused it?(K)

Surely the Sovereign Lord does nothing
    without revealing his plan(L)
    to his servants the prophets.(M)

The lion(N) has roared(O)
    who will not fear?
The Sovereign Lord has spoken—
    who can but prophesy?(P)

Proclaim to the fortresses of Ashdod(Q)
    and to the fortresses of Egypt:
“Assemble yourselves on the mountains of Samaria;(R)
    see the great unrest within her
    and the oppression among her people.”

10 “They do not know how to do right,(S)” declares the Lord,
    “who store up in their fortresses(T)
    what they have plundered(U) and looted.”

11 Therefore this is what the Sovereign Lord says:

“An enemy will overrun your land,
    pull down your strongholds
    and plunder your fortresses.(V)

12 This is what the Lord says:

“As a shepherd rescues from the lion’s(W) mouth
    only two leg bones or a piece of an ear,
so will the Israelites living in Samaria be rescued,
    with only the head of a bed
    and a piece of fabric[a] from a couch.[b](X)

13 “Hear this and testify(Y) against the descendants of Jacob,” declares the Lord, the Lord God Almighty.

14 “On the day I punish(Z) Israel for her sins,
    I will destroy the altars of Bethel;(AA)
the horns(AB) of the altar will be cut off
    and fall to the ground.
15 I will tear down the winter house(AC)
    along with the summer house;(AD)
the houses adorned with ivory(AE) will be destroyed
    and the mansions(AF) will be demolished,(AG)
declares the Lord.(AH)

Footnotes

  1. Amos 3:12 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  2. Amos 3:12 Or Israelites be rescued, / those who sit in Samaria / on the edge of their beds / and in Damascus on their couches.