Add parallel Print Page Options

Tsoka kwa Osalabadira Kanthu

Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,
    ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya,
inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka,
    kumene Aisraeli amafikako!
Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;
    mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja,
    ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti.
Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa?
    Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,
    zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,
    mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu.
Mumadya ana ankhosa onona
    ndi ana angʼombe onenepa.
Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka
    nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza
    ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri,
    koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;
    maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.

Yehova Amanyansidwa ndi Kunyada kwa Israeli

Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,

“Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo,
    ndimadana ndi nyumba zake zaufumu;
Ine ndidzawupereka mzindawu
    pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”

Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu. 10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”

11 Pakuti Yehova walamula kuti
    nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula,
    ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.

12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?
    Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja?
Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha
    ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara
    ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”

14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,
    “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu
umene udzakuzunzani
    kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”

Woe to the Complacent

Woe to you(A) who are complacent(B) in Zion,
    and to you who feel secure(C) on Mount Samaria,(D)
you notable men of the foremost nation,
    to whom the people of Israel come!(E)
Go to Kalneh(F) and look at it;
    go from there to great Hamath,(G)
    and then go down to Gath(H) in Philistia.
Are they better off than(I) your two kingdoms?
    Is their land larger than yours?
You put off the day of disaster
    and bring near a reign of terror.(J)
You lie on beds adorned with ivory
    and lounge on your couches.(K)
You dine on choice lambs
    and fattened calves.(L)
You strum away on your harps(M) like David
    and improvise on musical instruments.(N)
You drink wine(O) by the bowlful
    and use the finest lotions,
    but you do not grieve(P) over the ruin of Joseph.(Q)
Therefore you will be among the first to go into exile;(R)
    your feasting and lounging will end.(S)

The Lord Abhors the Pride of Israel

The Sovereign Lord has sworn by himself(T)—the Lord God Almighty declares:

“I abhor(U) the pride of Jacob(V)
    and detest his fortresses;(W)
I will deliver up(X) the city
    and everything in it.(Y)

If ten(Z) people are left in one house, they too will die. 10 And if the relative who comes to carry the bodies out of the house to burn them[a](AA) asks anyone who might be hiding there, “Is anyone else with you?” and he says, “No,” then he will go on to say, “Hush!(AB) We must not mention the name of the Lord.”

11 For the Lord has given the command,
    and he will smash(AC) the great house(AD) into pieces
    and the small house into bits.(AE)

12 Do horses run on the rocky crags?
    Does one plow the sea[b] with oxen?
But you have turned justice into poison(AF)
    and the fruit of righteousness(AG) into bitterness(AH)
13 you who rejoice in the conquest of Lo Debar[c]
    and say, “Did we not take Karnaim[d] by our own strength?(AI)

14 For the Lord God Almighty declares,
    “I will stir up a nation(AJ) against you, Israel,
that will oppress you all the way
    from Lebo Hamath(AK) to the valley of the Arabah.(AL)

Footnotes

  1. Amos 6:10 Or to make a funeral fire in honor of the dead
  2. Amos 6:12 With a different word division of the Hebrew; Masoretic Text plow there
  3. Amos 6:13 Lo Debar means nothing.
  4. Amos 6:13 Karnaim means horns; horn here symbolizes strength.