Add parallel Print Page Options

Dengu la Zipatso Zakupsa

Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa. Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?”

Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.”

Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.

“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”

Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa
    ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.

Mumanena kuti,

“Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti
    kuti tigulitse zinthu?
Ndipo tsiku la Sabata litha liti
    kuti tigulitse tirigu,
kuti tichepetse miyeso,
    kukweza mitengo
    kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
tigule osauka ndi ndalama zasiliva
    ndi osowa powapatsa nsapato,
    tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”

Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.

“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi,
    ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni?
Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo;
    lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata
    ngati mtsinje wa ku Igupto.

“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti,

“Ndidzadetsa dzuwa masana
    ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni
    ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro.
Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu
    ndi kumeta mipala mitu yanu.
Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo,
    ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.

11 “Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti,
    “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse;
osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi,
    koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina.
    Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa,
kufunafuna mawu a Yehova,
    koma sadzawapeza.

13 “Tsiku limenelo

“anamwali okongola ndi anyamata amphamvu
    adzakomoka ndi ludzu.
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya,
    kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’
    kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’
Iwowo adzagwa
    ndipo sadzadzukanso.”

A Basket of Ripe Fruit

This is what the Sovereign Lord showed me:(A) a basket of ripe fruit. “What do you see,(B) Amos?(C)” he asked.

“A basket(D) of ripe fruit,” I answered.

Then the Lord said to me, “The time is ripe for my people Israel; I will spare them no longer.(E)

“In that day,” declares the Sovereign Lord, “the songs in the temple will turn to wailing.[a](F) Many, many bodies—flung everywhere! Silence!(G)

Hear this, you who trample the needy
    and do away with the poor(H) of the land,(I)

saying,

“When will the New Moon(J) be over
    that we may sell grain,
and the Sabbath be ended
    that we may market(K) wheat?”(L)
skimping on the measure,
    boosting the price
    and cheating(M) with dishonest scales,(N)
buying the poor(O) with silver
    and the needy for a pair of sandals,
    selling even the sweepings with the wheat.(P)

The Lord has sworn by himself, the Pride of Jacob:(Q) “I will never forget(R) anything they have done.(S)

“Will not the land tremble(T) for this,
    and all who live in it mourn?
The whole land will rise like the Nile;
    it will be stirred up and then sink
    like the river of Egypt.(U)

“In that day,” declares the Sovereign Lord,

“I will make the sun go down at noon
    and darken the earth in broad daylight.(V)
10 I will turn your religious festivals(W) into mourning
    and all your singing into weeping.(X)
I will make all of you wear sackcloth(Y)
    and shave(Z) your heads.
I will make that time like mourning for an only son(AA)
    and the end of it like a bitter day.(AB)

11 “The days are coming,”(AC) declares the Sovereign Lord,
    “when I will send a famine through the land—
not a famine of food or a thirst for water,
    but a famine(AD) of hearing the words of the Lord.(AE)
12 People will stagger from sea to sea
    and wander from north to east,
searching for the word of the Lord,
    but they will not find it.(AF)

13 “In that day

“the lovely young women and strong young men(AG)
    will faint because of thirst.(AH)
14 Those who swear by the sin of Samaria(AI)
    who say, ‘As surely as your god lives, Dan,’(AJ)
    or, ‘As surely as the god[b] of Beersheba(AK) lives’—
    they will fall,(AL) never to rise again.(AM)

Footnotes

  1. Amos 8:3 Or “the temple singers will wail
  2. Amos 8:14 Hebrew the way