Amosi 8
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Dengu la Zipatso Zakupsa
8 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa. 2 Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?”
Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.”
Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa
ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 Mumanena kuti,
“Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti
kuti tigulitse zinthu?
Ndipo tsiku la Sabata litha liti
kuti tigulitse tirigu,
kuti tichepetse miyeso,
kukweza mitengo
kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 tigule osauka ndi ndalama zasiliva
ndi osowa powapatsa nsapato,
tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 “Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi,
ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni?
Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo;
lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata
ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti,
“Ndidzadetsa dzuwa masana
ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni
ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro.
Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu
ndi kumeta mipala mitu yanu.
Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo,
ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 “Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti,
“Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse;
osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi,
koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina.
Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa,
kufunafuna mawu a Yehova,
koma sadzawapeza.
13 “Tsiku limenelo
“anamwali okongola ndi anyamata amphamvu
adzakomoka ndi ludzu.
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya,
kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’
kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’
Iwowo adzagwa
ndipo sadzadzukanso.”
Amos 8
New International Version
A Basket of Ripe Fruit
8 This is what the Sovereign Lord showed me:(A) a basket of ripe fruit. 2 “What do you see,(B) Amos?(C)” he asked.
“A basket(D) of ripe fruit,” I answered.
Then the Lord said to me, “The time is ripe for my people Israel; I will spare them no longer.(E)
3 “In that day,” declares the Sovereign Lord, “the songs in the temple will turn to wailing.[a](F) Many, many bodies—flung everywhere! Silence!(G)”
5 saying,
“When will the New Moon(J) be over
that we may sell grain,
and the Sabbath be ended
that we may market(K) wheat?”(L)—
skimping on the measure,
boosting the price
and cheating(M) with dishonest scales,(N)
6 buying the poor(O) with silver
and the needy for a pair of sandals,
selling even the sweepings with the wheat.(P)
7 The Lord has sworn by himself, the Pride of Jacob:(Q) “I will never forget(R) anything they have done.(S)
8 “Will not the land tremble(T) for this,
and all who live in it mourn?
The whole land will rise like the Nile;
it will be stirred up and then sink
like the river of Egypt.(U)
9 “In that day,” declares the Sovereign Lord,
“I will make the sun go down at noon
and darken the earth in broad daylight.(V)
10 I will turn your religious festivals(W) into mourning
and all your singing into weeping.(X)
I will make all of you wear sackcloth(Y)
and shave(Z) your heads.
I will make that time like mourning for an only son(AA)
and the end of it like a bitter day.(AB)
11 “The days are coming,”(AC) declares the Sovereign Lord,
“when I will send a famine through the land—
not a famine of food or a thirst for water,
but a famine(AD) of hearing the words of the Lord.(AE)
12 People will stagger from sea to sea
and wander from north to east,
searching for the word of the Lord,
but they will not find it.(AF)
13 “In that day
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.