Amosi 9
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Israeli Adzawonongedwa
9 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:
“Kantha mitu ya nsanamira
kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.
Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,
onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,
palibe amene adzapulumuke.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,
dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.
Ngakhale atakwera kumwamba
Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,
Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.
Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,
ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,
ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.
Ndidzawayangʼanitsitsa
kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,
onse amene amakhala mʼmenemo amalira.
Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,
kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,
ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,
Iye amene amayitana madzi a ku nyanja
ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,
dzina lake ndiye Yehova.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli
chimodzimodzi ndi Akusi?”
Akutero Yehova.
“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,
Afilisti ku Kafitori
ndi Aaramu ku Kiri?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova
ali pa ufumu wochimwawu.
Ndidzawufafaniza
pa dziko lapansi.
Komabe sindidzawononga kotheratu
nyumba ya Yakobo,”
akutero Yehova.
9 “Pakuti ndidzalamula,
ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli
pakati pa mitundu yonse ya anthu
monga momwe amasefera ufa mʼsefa,
koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga
adzaphedwa ndi lupanga,
onse amene amanena kuti,
‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
Kubwezeretsedwa kwa Israeli
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa
nyumba ya Davide imene inagwa.
Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,
ndi kuyimanganso
monga inalili poyamba,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu
ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”
akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
13 Yehova akunena kuti
“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola
ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.
Mapiri adzachucha vinyo watsopano
ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;
mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.
Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;
adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,
ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko
limene Ine ndawapatsa,”
akutero Yehova Mulungu wako.
Amos 9
New International Version
Israel to Be Destroyed
9 I saw the Lord standing by the altar, and he said:
“Strike the tops of the pillars
so that the thresholds shake.
Bring them down on the heads(A) of all the people;
those who are left I will kill with the sword.
Not one will get away,
none will escape.(B)
2 Though they dig down to the depths below,(C)
from there my hand will take them.
Though they climb up to the heavens above,(D)
from there I will bring them down.(E)
3 Though they hide themselves on the top of Carmel,(F)
there I will hunt them down and seize them.(G)
Though they hide from my eyes at the bottom of the sea,(H)
there I will command the serpent(I) to bite them.(J)
4 Though they are driven into exile by their enemies,
there I will command the sword(K) to slay them.
5 The Lord, the Lord Almighty—
he touches the earth and it melts,(O)
and all who live in it mourn;
the whole land rises like the Nile,
then sinks like the river of Egypt;(P)
6 he builds his lofty palace[a](Q) in the heavens
and sets its foundation[b] on the earth;
he calls for the waters of the sea
and pours them out over the face of the land—
the Lord is his name.(R)
7 “Are not you Israelites
the same to me as the Cushites[c]?”(S)
declares the Lord.
“Did I not bring Israel up from Egypt,
the Philistines(T) from Caphtor[d](U)
and the Arameans from Kir?(V)
8 “Surely the eyes of the Sovereign Lord
are on the sinful kingdom.
I will destroy(W) it
from the face of the earth.
Yet I will not totally destroy
the descendants of Jacob,”
declares the Lord.(X)
9 “For I will give the command,
and I will shake the people of Israel
among all the nations
as grain(Y) is shaken in a sieve,(Z)
and not a pebble will reach the ground.(AA)
10 All the sinners among my people
will die by the sword,(AB)
all those who say,
‘Disaster will not overtake or meet us.’(AC)
Israel’s Restoration
11 “In that day
“I will restore David’s(AD) fallen shelter(AE)—
I will repair its broken walls
and restore its ruins(AF)—
and will rebuild it as it used to be,(AG)
12 so that they may possess the remnant of Edom(AH)
and all the nations that bear my name,[e](AI)”
declares the Lord, who will do these things.(AJ)
13 “The days are coming,”(AK) declares the Lord,
“when the reaper(AL) will be overtaken by the plowman(AM)
and the planter by the one treading(AN) grapes.
New wine(AO) will drip from the mountains
and flow from all the hills,(AP)
14 and I will bring(AQ) my people Israel back from exile.[f](AR)
“They will rebuild the ruined cities(AS) and live in them.
They will plant vineyards(AT) and drink their wine;
they will make gardens and eat their fruit.(AU)
15 I will plant(AV) Israel in their own land,(AW)
never again to be uprooted(AX)
from the land I have given them,”(AY)
says the Lord your God.(AZ)
Footnotes
- Amos 9:6 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
- Amos 9:6 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
- Amos 9:7 That is, people from the upper Nile region
- Amos 9:7 That is, Crete
- Amos 9:12 Hebrew; Septuagint so that the remnant of people / and all the nations that bear my name may seek me
- Amos 9:14 Or will restore the fortunes of my people Israel
Amos 9
King James Version
9 I saw the Lord standing upon the altar: and he said, Smite the lintel of the door, that the posts may shake: and cut them in the head, all of them; and I will slay the last of them with the sword: he that fleeth of them shall not flee away, and he that escapeth of them shall not be delivered.
2 Though they dig into hell, thence shall mine hand take them; though they climb up to heaven, thence will I bring them down:
3 And though they hide themselves in the top of Carmel, I will search and take them out thence; and though they be hid from my sight in the bottom of the sea, thence will I command the serpent, and he shall bite them:
4 And though they go into captivity before their enemies, thence will I command the sword, and it shall slay them: and I will set mine eyes upon them for evil, and not for good.
5 And the Lord God of hosts is he that toucheth the land, and it shall melt, and all that dwell therein shall mourn: and it shall rise up wholly like a flood; and shall be drowned, as by the flood of Egypt.
6 It is he that buildeth his stories in the heaven, and hath founded his troop in the earth; he that calleth for the waters of the sea, and poureth them out upon the face of the earth: The Lord is his name.
7 Are ye not as children of the Ethiopians unto me, O children of Israel? saith the Lord. Have not I brought up Israel out of the land of Egypt? and the Philistines from Caphtor, and the Syrians from Kir?
8 Behold, the eyes of the Lord God are upon the sinful kingdom, and I will destroy it from off the face of the earth; saving that I will not utterly destroy the house of Jacob, saith the Lord.
9 For, lo, I will command, and I will sift the house of Israel among all nations, like as corn is sifted in a sieve, yet shall not the least grain fall upon the earth.
10 All the sinners of my people shall die by the sword, which say, The evil shall not overtake nor prevent us.
11 In that day will I raise up the tabernacle of David that is fallen, and close up the breaches thereof; and I will raise up his ruins, and I will build it as in the days of old:
12 That they may possess the remnant of Edom, and of all the heathen, which are called by my name, saith the Lord that doeth this.
13 Behold, the days come, saith the Lord, that the plowman shall overtake the reaper, and the treader of grapes him that soweth seed; and the mountains shall drop sweet wine, and all the hills shall melt.
14 And I will bring again the captivity of my people of Israel, and they shall build the waste cities, and inhabit them; and they shall plant vineyards, and drink the wine thereof; they shall also make gardens, and eat the fruit of them.
15 And I will plant them upon their land, and they shall no more be pulled up out of their land which I have given them, saith the Lord thy God.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.