Add parallel Print Page Options

10 Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe. Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso. Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu. Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.

Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’ ” (ndiko, kukatsitsa Khristu) “kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’ ” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira, kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka. 10 Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa. 11 Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.” 12 Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye 13 pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”

14 Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo? 15 Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”

16 Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?” 17 Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu. 18 Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti,

“Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi.
    Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”

19 Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti,

“Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake.
    Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”

20 Ndipo Yesaya molimba mtima akuti,

“Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna.
    Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”

21 Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti,

“Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga
    kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

10 Brothers and sisters, my heart’s desire(A) and prayer to God for the Israelites is that they may be saved. For I can testify about them that they are zealous(B) for God, but their zeal is not based on knowledge. Since they did not know the righteousness of God and sought to establish their own, they did not submit to God’s righteousness.(C) Christ is the culmination of the law(D) so that there may be righteousness for everyone who believes.(E)

Moses writes this about the righteousness that is by the law: “The person who does these things will live by them.”[a](F) But the righteousness that is by faith(G) says: “Do not say in your heart, ‘Who will ascend into heaven?’”[b](H) (that is, to bring Christ down) “or ‘Who will descend into the deep?’”[c](I) (that is, to bring Christ up from the dead).(J) But what does it say? “The word is near you; it is in your mouth and in your heart,”[d](K) that is, the message concerning faith that we proclaim: If you declare(L) with your mouth, “Jesus is Lord,”(M) and believe(N) in your heart that God raised him from the dead,(O) you will be saved.(P) 10 For it is with your heart that you believe and are justified, and it is with your mouth that you profess your faith and are saved. 11 As Scripture says, “Anyone who believes in him will never be put to shame.”[e](Q) 12 For there is no difference between Jew and Gentile(R)—the same Lord is Lord of all(S) and richly blesses all who call on him, 13 for, “Everyone who calls on the name of the Lord(T) will be saved.”[f](U)

14 How, then, can they call on the one they have not believed in? And how can they believe in the one of whom they have not heard? And how can they hear without someone preaching to them? 15 And how can anyone preach unless they are sent? As it is written: “How beautiful are the feet of those who bring good news!”[g](V)

16 But not all the Israelites accepted the good news.(W) For Isaiah says, “Lord, who has believed our message?”[h](X) 17 Consequently, faith comes from hearing the message,(Y) and the message is heard through the word about Christ.(Z) 18 But I ask: Did they not hear? Of course they did:

“Their voice has gone out into all the earth,
    their words to the ends of the world.”[i](AA)

19 Again I ask: Did Israel not understand? First, Moses says,

“I will make you envious(AB) by those who are not a nation;
    I will make you angry by a nation that has no understanding.”[j](AC)

20 And Isaiah boldly says,

“I was found by those who did not seek me;
    I revealed myself to those who did not ask for me.”[k](AD)

21 But concerning Israel he says,

“All day long I have held out my hands
    to a disobedient and obstinate people.”[l](AE)

Footnotes

  1. Romans 10:5 Lev. 18:5
  2. Romans 10:6 Deut. 30:12
  3. Romans 10:7 Deut. 30:13
  4. Romans 10:8 Deut. 30:14
  5. Romans 10:11 Isaiah 28:16 (see Septuagint)
  6. Romans 10:13 Joel 2:32
  7. Romans 10:15 Isaiah 52:7
  8. Romans 10:16 Isaiah 53:1
  9. Romans 10:18 Psalm 19:4
  10. Romans 10:19 Deut. 32:21
  11. Romans 10:20 Isaiah 65:1
  12. Romans 10:21 Isaiah 65:2