Add parallel Print Page Options

Mawu Olawirana

16 Ine ndikupereka kwa inu mlongo wathu Febe, mtumiki wa mpingo wa ku Kenkreya. Ine ndikukupemphani kuti mumulandire mwa Ambuye mʼnjira yoyenera oyera mtima ndi kumupatsa thandizo lililonse limene akulifuna kuchokera kwa inu, pakuti iye wakhala thandizo lalikulu kwa anthu ambiri kuphatikiza ine.

Perekani moni kwa Prisila ndi Akura, atumiki anzanga mwa Khristu Yesu. Iwo anapereka miyoyo yawo chifukwa cha ine. Osati ine ndekha komanso mipingo yonse ya a mitundu ina ikuyamika.

Perekaninso moni kwa mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwawo.

Perekani moni kwa mʼbale wanga wokondedwa Epeneto, amene ndi woyamba kukhulupirira Khristu mʼchigawo cha Asiya.

Perekani moni kwa Mariya, amene wakhala akukugwirirani ntchito kwambiri.

Perekani moni kwa Androniko ndi Yuniya abale anga amene anali mʼndende pamodzi ndi ine. Iwo amadziwika ndi atumwi, ndipo iwo anali mwa Khristu ine ndisanakhale.

Perekani moni kwa Ampliato, amene ine ndimamukonda mwa Ambuye.

Perekani moni kwa Urbano, mtumiki mnzathu mwa Khristu ndi wokondedwa wanga Staku.

10 Perekani moni kwa Apele, woyesedwa ndi wovomerezeka mwa Khristu.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Aristobulo.

11 Perekani moni kwa Herodiona, mʼbale wanga.

Perekani moni kwa a mʼbanja la Narkiso amene ali mwa Ambuye.

12 Perekani moni kwa Trufena ndi Trufosa, amayi aja amene amagwira ntchito ya Ambuye molimbika.

Perekani moni kwa mnzanga wokondedwa Persida, mayi winanso amene wagwira ntchito kwambiri mwa Ambuye.

13 Perekani moni kwa Rufo, wosankhidwa mwa Ambuye, ndi amayi ake, amene akhala amayi anganso.

14 Perekani moni kwa Asunkrito, Felego, Herima, Patroba, Herima ndi abale amene ali nawo pamodzi.

15 Perekani moni kwa Filologo, Yuliya, Neriya ndi mlongo wake, ndi Olumpa ndi oyera mtima onse amene ali nawo pamodzi.

16 Mupatsane moni wina ndi mnzake mwachikondi choona.

Mipingo yonse ya Khristu ikupereka moni.

17 Abale, ine ndikukupemphani kuti musamale chifukwa cha amene ayambitsa mipatuko ndi kuyika zokhumudwitsa panjira yanu, motsutsana ndi chiphunzitso chimene mwachiphunzira. Muwapewe iwo. 18 Pakuti otero sakutumikira Ambuye athu Khristu koma zilakolako zawo. Ndi mawu okoma ndi oshashalika iwo amanamiza anthu osalakwa. 19 Aliyense anamva za kumvera kwanu, choncho ndine odzaza ndi chimwemwe chifukwa cha inu. Koma ine ndikufuna kuti inu mukhale anzeru pa zabwino, ndi wopanda cholakwa pa zimene zili zoyipa.

20 Mulungu wamtendere adzaphwanya Satana msanga pansi pa mapazi anu.

Chisomo cha Ambuye athu Yesu chikhale ndi inu.

21 Timoteyo, mtumiki mnzanga, akupereka moni. Nawonso, Lusio, Yasoni ndi Sosipatro, abale anga akutero.

22 Ine Tertio, amene ndalemba kalatayi, ndi kupereka moni mwa Ambuye.

23 Gayo, amene chifukwa cha chisamaliro chake, ine ndi mpingo wonse kuno tikusangalala, akupereka moni.

Erasto, amene ndi msungichuma wa mzinda wonse ndiponso mʼbale wathu Kwato, akupereka moni.

24 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse. Ameni.

25 Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, 26 koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, 27 kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni.

Personal Greetings

16 I commend(A) to you our sister Phoebe, a deacon[a][b] of the church in Cenchreae.(B) I ask you to receive her in the Lord(C) in a way worthy of his people(D) and to give her any help she may need from you, for she has been the benefactor of many people, including me.

Greet Priscilla[c] and Aquila,(E) my co-workers(F) in Christ Jesus.(G) They risked their lives for me. Not only I but all the churches of the Gentiles are grateful to them.

Greet also the church that meets at their house.(H)

Greet my dear friend Epenetus, who was the first convert(I) to Christ in the province of Asia.(J)

Greet Mary, who worked very hard for you.

Greet Andronicus and Junia, my fellow Jews(K) who have been in prison with me.(L) They are outstanding among[d] the apostles, and they were in Christ(M) before I was.

Greet Ampliatus, my dear friend in the Lord.

Greet Urbanus, our co-worker in Christ,(N) and my dear friend Stachys.

10 Greet Apelles, whose fidelity to Christ has stood the test.(O)

Greet those who belong to the household(P) of Aristobulus.

11 Greet Herodion, my fellow Jew.(Q)

Greet those in the household(R) of Narcissus who are in the Lord.

12 Greet Tryphena and Tryphosa, those women who work hard in the Lord.

Greet my dear friend Persis, another woman who has worked very hard in the Lord.

13 Greet Rufus,(S) chosen(T) in the Lord, and his mother, who has been a mother to me, too.

14 Greet Asyncritus, Phlegon, Hermes, Patrobas, Hermas and the other brothers and sisters with them.

15 Greet Philologus, Julia, Nereus and his sister, and Olympas and all the Lord’s people(U) who are with them.(V)

16 Greet one another with a holy kiss.(W)

All the churches of Christ send greetings.

17 I urge you, brothers and sisters, to watch out for those who cause divisions and put obstacles in your way that are contrary to the teaching you have learned.(X) Keep away from them.(Y) 18 For such people are not serving our Lord Christ,(Z) but their own appetites.(AA) By smooth talk and flattery they deceive(AB) the minds of naive people. 19 Everyone has heard(AC) about your obedience, so I rejoice because of you; but I want you to be wise about what is good, and innocent about what is evil.(AD)

20 The God of peace(AE) will soon crush(AF) Satan(AG) under your feet.

The grace of our Lord Jesus be with you.(AH)

21 Timothy,(AI) my co-worker, sends his greetings to you, as do Lucius,(AJ) Jason(AK) and Sosipater, my fellow Jews.(AL)

22 I, Tertius, who wrote down this letter, greet you in the Lord.

23 Gaius,(AM) whose hospitality I and the whole church here enjoy, sends you his greetings.

Erastus,(AN) who is the city’s director of public works, and our brother Quartus send you their greetings. [24] [e]

25 Now to him who is able(AO) to establish you in accordance with my gospel,(AP) the message I proclaim about Jesus Christ, in keeping with the revelation of the mystery(AQ) hidden for long ages past, 26 but now revealed and made known through the prophetic writings(AR) by the command of the eternal God, so that all the Gentiles might come to the obedience that comes from[f] faith(AS) 27 to the only wise God be glory forever through Jesus Christ! Amen.(AT)

Footnotes

  1. Romans 16:1 Or servant
  2. Romans 16:1 The word deacon refers here to a Christian designated to serve with the overseers/elders of the church in a variety of ways; similarly in Phil. 1:1 and 1 Tim. 3:8,12.
  3. Romans 16:3 Greek Prisca, a variant of Priscilla
  4. Romans 16:7 Or are esteemed by
  5. Romans 16:24 Some manuscripts include here May the grace of our Lord Jesus Christ be with all of you. Amen.
  6. Romans 16:26 Or that is