Add parallel Print Page Options

Kukhulupirika kwa Mulungu

Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.

Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,

“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula
    ndi kupambana pamene muweruza.”

Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.

Palibe Munthu Wolungama

Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10 Monga kwalembedwa kuti,

“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11     Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,
    palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Onse apatukira kumbali,
    onse pamodzi asanduka opandapake.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,
    palibe ngakhale mmodzi.”
13 “Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;
    ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”
“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14     “Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 “Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16     Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18     “Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”

19 Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20 Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.

Kulungama Mwachikhulupiriro

21 Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22 Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23 pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24 ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25 Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26 Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.

27 Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28 Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29 Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30 popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31 Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

God’s Faithfulness

What advantage, then, is there in being a Jew, or what value is there in circumcision? Much in every way!(A) First of all, the Jews have been entrusted with the very words of God.(B)

What if some were unfaithful?(C) Will their unfaithfulness nullify God’s faithfulness?(D) Not at all! Let God be true,(E) and every human being a liar.(F) As it is written:

“So that you may be proved right when you speak
    and prevail when you judge.”[a](G)

But if our unrighteousness brings out God’s righteousness more clearly,(H) what shall we say? That God is unjust in bringing his wrath on us? (I am using a human argument.)(I) Certainly not! If that were so, how could God judge the world?(J) Someone might argue, “If my falsehood enhances God’s truthfulness and so increases his glory,(K) why am I still condemned as a sinner?”(L) Why not say—as some slanderously claim that we say—“Let us do evil that good may result”?(M) Their condemnation is just!

No One Is Righteous

What shall we conclude then? Do we have any advantage?(N) Not at all! For we have already made the charge that Jews and Gentiles alike are all under the power of sin.(O) 10 As it is written:

“There is no one righteous, not even one;
11     there is no one who understands;
    there is no one who seeks God.
12 All have turned away,
    they have together become worthless;
there is no one who does good,
    not even one.”[b](P)
13 “Their throats are open graves;
    their tongues practice deceit.”[c](Q)
“The poison of vipers is on their lips.”[d](R)
14     “Their mouths are full of cursing and bitterness.”[e](S)
15 “Their feet are swift to shed blood;
16     ruin and misery mark their ways,
17 and the way of peace they do not know.”[f](T)
18     “There is no fear of God before their eyes.”[g](U)

19 Now we know that whatever the law says,(V) it says to those who are under the law,(W) so that every mouth may be silenced(X) and the whole world held accountable to God.(Y) 20 Therefore no one will be declared righteous in God’s sight by the works of the law;(Z) rather, through the law we become conscious of our sin.(AA)

Righteousness Through Faith

21 But now apart from the law the righteousness of God(AB) has been made known, to which the Law and the Prophets testify.(AC) 22 This righteousness(AD) is given through faith(AE) in[h] Jesus Christ(AF) to all who believe.(AG) There is no difference between Jew and Gentile,(AH) 23 for all have sinned(AI) and fall short of the glory of God, 24 and all are justified(AJ) freely by his grace(AK) through the redemption(AL) that came by Christ Jesus. 25 God presented Christ as a sacrifice of atonement,[i](AM) through the shedding of his blood(AN)—to be received by faith. He did this to demonstrate his righteousness, because in his forbearance he had left the sins committed beforehand unpunished(AO) 26 he did it to demonstrate his righteousness at the present time, so as to be just and the one who justifies those who have faith in Jesus.

27 Where, then, is boasting?(AP) It is excluded. Because of what law? The law that requires works? No, because of the law that requires faith. 28 For we maintain that a person is justified by faith apart from the works of the law.(AQ) 29 Or is God the God of Jews only? Is he not the God of Gentiles too? Yes, of Gentiles too,(AR) 30 since there is only one God, who will justify the circumcised by faith and the uncircumcised through that same faith.(AS) 31 Do we, then, nullify the law by this faith? Not at all! Rather, we uphold the law.

Footnotes

  1. Romans 3:4 Psalm 51:4
  2. Romans 3:12 Psalms 14:1-3; 53:1-3; Eccles. 7:20
  3. Romans 3:13 Psalm 5:9
  4. Romans 3:13 Psalm 140:3
  5. Romans 3:14 Psalm 10:7 (see Septuagint)
  6. Romans 3:17 Isaiah 59:7,8
  7. Romans 3:18 Psalm 36:1
  8. Romans 3:22 Or through the faithfulness of
  9. Romans 3:25 The Greek for sacrifice of atonement refers to the atonement cover on the ark of the covenant (see Lev. 16:15,16).