Add parallel Print Page Options

Mtendere ndi Chimwemwe

Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.

Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.

Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.

Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu

12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.

15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.

18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.

20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.

Peace and Hope

Therefore, since we have been justified(A) through faith,(B) we[a] have peace(C) with God through our Lord Jesus Christ,(D) through whom we have gained access(E) by faith into this grace in which we now stand.(F) And we[b] boast in the hope(G) of the glory of God. Not only so, but we[c] also glory in our sufferings,(H) because we know that suffering produces perseverance;(I) perseverance, character; and character, hope. And hope(J) does not put us to shame, because God’s love(K) has been poured out into our hearts through the Holy Spirit,(L) who has been given to us.

You see, at just the right time,(M) when we were still powerless,(N) Christ died for the ungodly.(O) Very rarely will anyone die for a righteous person, though for a good person someone might possibly dare to die. But God demonstrates his own love for us in this: While we were still sinners, Christ died for us.(P)

Since we have now been justified(Q) by his blood,(R) how much more shall we be saved from God’s wrath(S) through him! 10 For if, while we were God’s enemies,(T) we were reconciled(U) to him through the death of his Son, how much more, having been reconciled, shall we be saved through his life!(V) 11 Not only is this so, but we also boast in God through our Lord Jesus Christ, through whom we have now received reconciliation.(W)

Death Through Adam, Life Through Christ

12 Therefore, just as sin entered the world through one man,(X) and death through sin,(Y) and in this way death came to all people, because all sinned(Z)

13 To be sure, sin was in the world before the law was given, but sin is not charged against anyone’s account where there is no law.(AA) 14 Nevertheless, death reigned from the time of Adam to the time of Moses, even over those who did not sin by breaking a command, as did Adam,(AB) who is a pattern of the one to come.(AC)

15 But the gift is not like the trespass. For if the many died by the trespass of the one man,(AD) how much more did God’s grace and the gift that came by the grace of the one man, Jesus Christ,(AE) overflow to the many! 16 Nor can the gift of God be compared with the result of one man’s sin: The judgment followed one sin and brought condemnation, but the gift followed many trespasses and brought justification. 17 For if, by the trespass of the one man, death(AF) reigned through that one man, how much more will those who receive God’s abundant provision of grace and of the gift of righteousness reign in life(AG) through the one man, Jesus Christ!

18 Consequently, just as one trespass resulted in condemnation for all people,(AH) so also one righteous act resulted in justification(AI) and life(AJ) for all people. 19 For just as through the disobedience of the one man(AK) the many were made sinners,(AL) so also through the obedience(AM) of the one man the many will be made righteous.

20 The law was brought in so that the trespass might increase.(AN) But where sin increased, grace increased all the more,(AO) 21 so that, just as sin reigned in death,(AP) so also grace(AQ) might reign through righteousness to bring eternal life(AR) through Jesus Christ our Lord.

Footnotes

  1. Romans 5:1 Many manuscripts let us
  2. Romans 5:2 Or let us
  3. Romans 5:3 Or let us