Add parallel Print Page Options

Malemba pa Khoma

Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo. Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo. Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo. Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.

Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba. Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.

Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”

Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu. Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.

10 Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike! 11 Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula. 12 Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”

13 Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda? 14 Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera. 15 Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera. 16 Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”

17 Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.

18 “Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu. 19 Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa. 20 Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake. 21 Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.

22 “Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi. 23 Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse. 24 Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.

25 “Mawu amene analembedwa ndi awa:

MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.

26 “Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:

Mene: Mulungu wawerenga masiku a ufumu wanu ndipo wauthetsa.
27 Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”

29 Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.

30 Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa, 31 ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

The Writing on the Wall

King Belshazzar(A) gave a great banquet(B) for a thousand of his nobles(C) and drank wine with them. While Belshazzar was drinking(D) his wine, he gave orders to bring in the gold and silver goblets(E) that Nebuchadnezzar his father[a] had taken from the temple in Jerusalem, so that the king and his nobles, his wives and his concubines(F) might drink from them.(G) So they brought in the gold goblets that had been taken from the temple of God in Jerusalem, and the king and his nobles, his wives and his concubines drank from them. As they drank the wine, they praised the gods(H) of gold and silver, of bronze, iron, wood and stone.(I)

Suddenly the fingers of a human hand appeared and wrote on the plaster of the wall, near the lampstand in the royal palace. The king watched the hand as it wrote. His face turned pale(J) and he was so frightened(K) that his legs became weak(L) and his knees were knocking.(M)

The king summoned the enchanters,(N) astrologers[b](O) and diviners.(P) Then he said to these wise(Q) men of Babylon, “Whoever reads this writing and tells me what it means will be clothed in purple and have a gold chain placed around his neck,(R) and he will be made the third(S) highest ruler in the kingdom.”(T)

Then all the king’s wise men(U) came in, but they could not read the writing or tell the king what it meant.(V) So King Belshazzar became even more terrified(W) and his face grew more pale. His nobles were baffled.

10 The queen,[c] hearing the voices of the king and his nobles, came into the banquet hall. “May the king live forever!”(X) she said. “Don’t be alarmed! Don’t look so pale! 11 There is a man in your kingdom who has the spirit of the holy gods(Y) in him. In the time of your father he was found to have insight and intelligence and wisdom(Z) like that of the gods.(AA) Your father, King Nebuchadnezzar, appointed him chief of the magicians, enchanters, astrologers and diviners.(AB) 12 He did this because Daniel, whom the king called Belteshazzar,(AC) was found to have a keen mind and knowledge and understanding, and also the ability to interpret dreams, explain riddles(AD) and solve difficult problems.(AE) Call for Daniel, and he will tell you what the writing means.(AF)

13 So Daniel was brought before the king, and the king said to him, “Are you Daniel, one of the exiles my father the king brought from Judah?(AG) 14 I have heard that the spirit of the gods(AH) is in you and that you have insight, intelligence and outstanding wisdom.(AI) 15 The wise men and enchanters were brought before me to read this writing and tell me what it means, but they could not explain it.(AJ) 16 Now I have heard that you are able to give interpretations and to solve difficult problems.(AK) If you can read this writing and tell me what it means, you will be clothed in purple and have a gold chain placed around your neck,(AL) and you will be made the third highest ruler in the kingdom.”(AM)

17 Then Daniel answered the king, “You may keep your gifts for yourself and give your rewards to someone else.(AN) Nevertheless, I will read the writing for the king and tell him what it means.

18 “Your Majesty, the Most High God gave your father Nebuchadnezzar(AO) sovereignty and greatness and glory and splendor.(AP) 19 Because of the high position he gave him, all the nations and peoples of every language dreaded and feared him. Those the king wanted to put to death, he put to death;(AQ) those he wanted to spare, he spared; those he wanted to promote, he promoted; and those he wanted to humble, he humbled.(AR) 20 But when his heart became arrogant and hardened with pride,(AS) he was deposed from his royal throne(AT) and stripped(AU) of his glory.(AV) 21 He was driven away from people and given the mind of an animal; he lived with the wild donkeys and ate grass like the ox; and his body was drenched with the dew of heaven, until he acknowledged that the Most High God is sovereign(AW) over all kingdoms on earth and sets over them anyone he wishes.(AX)

22 “But you, Belshazzar, his son,[d] have not humbled(AY) yourself, though you knew all this. 23 Instead, you have set yourself up against(AZ) the Lord of heaven. You had the goblets from his temple brought to you, and you and your nobles, your wives(BA) and your concubines drank wine from them. You praised the gods of silver and gold, of bronze, iron, wood and stone, which cannot see or hear or understand.(BB) But you did not honor the God who holds in his hand your life(BC) and all your ways.(BD) 24 Therefore he sent the hand that wrote the inscription.

25 “This is the inscription that was written:

mene, mene, tekel, parsin

26 “Here is what these words mean:

Mene[e]: God has numbered the days(BE) of your reign and brought it to an end.(BF)

27 Tekel[f]: You have been weighed on the scales(BG) and found wanting.(BH)

28 Peres[g]: Your kingdom is divided and given to the Medes(BI) and Persians.”(BJ)

29 Then at Belshazzar’s command, Daniel was clothed in purple, a gold chain was placed around his neck,(BK) and he was proclaimed the third highest ruler in the kingdom.(BL)

30 That very night Belshazzar,(BM) king(BN) of the Babylonians,[h] was slain,(BO) 31 and Darius(BP) the Mede(BQ) took over the kingdom, at the age of sixty-two.[i]

Footnotes

  1. Daniel 5:2 Or ancestor; or predecessor; also in verses 11, 13 and 18
  2. Daniel 5:7 Or Chaldeans; also in verse 11
  3. Daniel 5:10 Or queen mother
  4. Daniel 5:22 Or descendant; or successor
  5. Daniel 5:26 Mene can mean numbered or mina (a unit of money).
  6. Daniel 5:27 Tekel can mean weighed or shekel.
  7. Daniel 5:28 Peres (the singular of Parsin) can mean divided or Persia or a half mina or a half shekel.
  8. Daniel 5:30 Or Chaldeans
  9. Daniel 5:31 In Aramaic texts this verse (5:31) is numbered 6:1.