Add parallel Print Page Options

Madalitso Akabwerera kwa Yehova

30 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino, pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani. Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso. Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu. Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo. Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani. Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino. Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu, 10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

Moyo kapena Imfa

11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali. 12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?” 13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?” 14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.

15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko. 16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.

17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza, 18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.

19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo. 20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.

Prosperity After Turning to the Lord

30 When all these blessings and curses(A) I have set before you come on you and you take them to heart wherever the Lord your God disperses you among the nations,(B) and when you and your children return(C) to the Lord your God and obey him with all your heart(D) and with all your soul according to everything I command you today, then the Lord your God will restore your fortunes[a](E) and have compassion(F) on you and gather(G) you again from all the nations where he scattered(H) you.(I) Even if you have been banished to the most distant land under the heavens,(J) from there the Lord your God will gather(K) you and bring you back.(L) He will bring(M) you to the land that belonged to your ancestors, and you will take possession of it. He will make you more prosperous and numerous(N) than your ancestors. The Lord your God will circumcise your hearts and the hearts of your descendants,(O) so that you may love(P) him with all your heart and with all your soul, and live. The Lord your God will put all these curses(Q) on your enemies who hate and persecute you.(R) You will again obey the Lord and follow all his commands I am giving you today. Then the Lord your God will make you most prosperous in all the work of your hands and in the fruit of your womb, the young of your livestock and the crops of your land.(S) The Lord will again delight(T) in you and make you prosperous, just as he delighted in your ancestors, 10 if you obey the Lord your God and keep his commands and decrees that are written in this Book of the Law(U) and turn to the Lord your God with all your heart and with all your soul.(V)

The Offer of Life or Death

11 Now what I am commanding you today is not too difficult for you or beyond your reach.(W) 12 It is not up in heaven, so that you have to ask, “Who will ascend into heaven(X) to get it and proclaim it to us so we may obey it?”(Y) 13 Nor is it beyond the sea,(Z) so that you have to ask, “Who will cross the sea to get it and proclaim it to us so we may obey it?”(AA) 14 No, the word is very near you; it is in your mouth and in your heart so you may obey it.(AB)

15 See, I set before you today life(AC) and prosperity,(AD) death(AE) and destruction.(AF) 16 For I command you today to love(AG) the Lord your God, to walk in obedience to him, and to keep his commands, decrees and laws; then you will live(AH) and increase, and the Lord your God will bless you in the land you are entering to possess.

17 But if your heart turns away and you are not obedient, and if you are drawn away to bow down to other gods and worship them, 18 I declare to you this day that you will certainly be destroyed.(AI) You will not live long in the land you are crossing the Jordan to enter and possess.

19 This day I call the heavens and the earth as witnesses against you(AJ) that I have set before you life and death, blessings and curses.(AK) Now choose life, so that you and your children may live 20 and that you may love(AL) the Lord your God, listen to his voice, and hold fast to him. For the Lord is your life,(AM) and he will give(AN) you many years in the land(AO) he swore to give to your fathers, Abraham, Isaac and Jacob.

Footnotes

  1. Deuteronomy 30:3 Or will bring you back from captivity