Add parallel Print Page Options

Musayiwale Yehova

Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu. Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi. Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova. Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe. Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.

Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye. Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri, dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi; dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.

10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani. 11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, 12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo, 13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka, 14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo. 15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma. 16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino. 17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.” 18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.

19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu. 20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

Do Not Forget the Lord

Be careful to follow every command I am giving you today, so that you may live(A) and increase and may enter and possess the land the Lord promised on oath to your ancestors.(B) Remember how the Lord your God led(C) you all the way in the wilderness these forty years, to humble and test(D) you in order to know what was in your heart, whether or not you would keep his commands. He humbled(E) you, causing you to hunger and then feeding you with manna,(F) which neither you nor your ancestors had known, to teach(G) you that man does not live on bread(H) alone but on every word that comes from the mouth(I) of the Lord.(J) Your clothes did not wear out and your feet did not swell during these forty years.(K) Know then in your heart that as a man disciplines his son, so the Lord your God disciplines you.(L)

Observe the commands of the Lord your God, walking in obedience to him(M) and revering him.(N) For the Lord your God is bringing you into a good land(O)—a land with brooks, streams, and deep springs gushing out into the valleys and hills;(P) a land with wheat and barley,(Q) vines(R) and fig trees,(S) pomegranates, olive oil and honey;(T) a land where bread(U) will not be scarce and you will lack nothing;(V) a land where the rocks are iron and you can dig copper out of the hills.(W)

10 When you have eaten and are satisfied,(X) praise the Lord your God for the good land he has given you. 11 Be careful that you do not forget(Y) the Lord your God, failing to observe his commands, his laws and his decrees that I am giving you this day. 12 Otherwise, when you eat and are satisfied, when you build fine houses and settle down,(Z) 13 and when your herds and flocks grow large and your silver and gold increase and all you have is multiplied, 14 then your heart will become proud and you will forget(AA) the Lord your God, who brought you out of Egypt, out of the land of slavery. 15 He led you through the vast and dreadful wilderness,(AB) that thirsty and waterless land, with its venomous snakes(AC) and scorpions. He brought you water out of hard rock.(AD) 16 He gave you manna(AE) to eat in the wilderness, something your ancestors had never known,(AF) to humble and test(AG) you so that in the end it might go well with you. 17 You may say to yourself,(AH) “My power and the strength of my hands(AI) have produced this wealth for me.” 18 But remember the Lord your God, for it is he who gives you the ability to produce wealth,(AJ) and so confirms his covenant, which he swore to your ancestors, as it is today.

19 If you ever forget the Lord your God and follow other gods(AK) and worship and bow down to them, I testify against you today that you will surely be destroyed.(AL) 20 Like the nations(AM) the Lord destroyed before you, so you will be destroyed for not obeying the Lord your God.(AN)