Add parallel Print Page Options

Osati Chifukwa cha Kulungama kwa Israeli

Mvera Israeli. Watsala pangʼono kuwoloka Yorodani ndi kukathamangitsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa iweyo, imene mizinda yake ndi ikuluikulu yokhala ndi makoma ofika mpaka kumwamba. Anthuwo ndi ataliatali, Aanaki! Ukudziwa za iwo ndipo unamvapo zikunenedwa kuti, “Ndani amene angalimbane ndi Aanaki?” Koma khulupirira lero kuti Yehova Mulungu wako amene ali patsogolo pako ali ngati moto wonyeketsa. Adzawononga iwowo ndipo adzawagonjetsa iweyo ukuona. Pamenepo udzawathamangitsa ndi kuwakantha mwamsanga, monga momwe Yehova wakulonjezera.

Yehova Mulungu wako akadzawapirikitsa pamaso pako, usadzanene mu mtima mwako kuti, “Yehova wandibweretsa kuno kudzalanda dziko lino chifukwa cha kulungama kwanga.” Ayi, koma ndi chifukwa cha kuyipa kwa anthu amene Yehova ati awapirikitse pamaso pako. Sukalowa ndi kutenga dziko lawolo chifukwa cha kulungama kwako kapena kukhulupirika kwako koma chifukwa cha kuyipa kwa anthuwo. Yehova Mulungu wako awapirikitsa pamaso pako kuti akwaniritse zimene analumbira kwa makolo ako Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Tsono zindikira kuti si chifukwa cha kulungama kwako kuti Yehova Mulungu wako akukupatsa dziko labwinoli kuti ulitenge popeza ndiwe wokanika.

Mwana Wangʼombe Wagolide

Kumbukirani izi ndipo musayiwale mmene munaputira mkwiyo wa Yehova Mulungu mʼchipululu muja. Kuyambira tsiku limene munatuluka mu Igupto mpaka pamene munafika kuno, mwakhala owukira Yehova. Ku Horebu munaputa mkwiyo wa Yehova, kotero kuti anakwiya kwambiri nafuna kukuwonongani. Nditakwera ku phiri kuti ndikalandire miyala iwiri ya malamulo, ya pangano limene Yehova anachita ndi inu, ndinakhala ku phiriko kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana, sindinadye buledi kapena kumwa madzi. 10 Yehova anandipatsa miyala iwiri yolembedwa ndi chala chake. Pa miyalapo panali malamulo onse amene Yehova analengeza kwa inu pa phiri kuchokera mʼmoto pa tsiku la msonkhano.

11 Pakutha pa masiku makumi anayi usiku ndi usana, Yehova anandipatsa miyala iwiri, miyala ya pangano. 12 Tsono Yehova anandiwuza, “Tsikako kuno msanga, chifukwa anthu ako aja unawatulutsa ku Iguptowa adziyipitsa. Iwo apatukapo mofulumira pa zimene ndinawalamulira ndipo adzipangira fano lachitsulo.”

13 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Anthu awa ndawaona ndipo ndi anthu okanikadi! 14 Ndilekeni ndiwawononge ndi kufafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi wochuluka kuposa iwo.”

15 Choncho ndinatembenuka ndi kutsika phiri moto ukanayakabe. Ndipo miyala iwiri ya pangano inali mʼmanja mwanga. 16 Ine poyangʼana ndinaona kuti inu munachimwira Yehova Mulungu wanu. Munadzipangira fano lowumbidwa ngati mwana wangʼombe. Inuyo munapatuka msanga kuchoka pa njira imene Yehova anakulamulirani. 17 Motero ine ndinaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwanga, ndi kuyiphwanya inu mukuona.

18 Tsono nthawi yomweyo ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana. Sindinadye buledi kapena kumwa madzi chifukwa cha machimo onse amene munawachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kumukwiyitsa kwambiri. 19 Ine ndinachita mantha ndi mkwiyo ndi ukali wa Yehova chifukwa anakwiya nanu kokwanira kukuwonongani. Koma Yehova anandimveranso. 20 Ndipo Yehova anakwiya ndi Aaroni ndipo akanamuwononga, koma ine ndinamupemphereranso Aaroniyo. 21 Ndiponso ndinatenga chinthu chanu choyipacho, mwana wangʼombe amene munapangayo, ndi kumuwotcha pa moto. Kenaka ndinamuphwanya ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi ndipo ndinawaza fumbilo mu mtsinje umene unkayenda kuchokera mʼphiri.

22 Inu munamukwiyitsanso Yehova ku Tabera, ku Masa ndi ku Kibiroti Hatava.

23 Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera. 24 Kuyambira pamene ndinakudziwani, mwakhala owukira Yehova.

25 Ine ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku chifukwa Yehova ananena kuti akuwonongani. 26 Ndinapemphera kwa Ambuye ndi kuti, “Haa Yehova Wamkulukulu, musawawononge anthu anu, chuma chanuchanu chimene munachipulumutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ku Igupto ndi dzanja lanu la mphamvu. 27 Kumbukirani atumiki anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Musatengere kupulupudza, kuyipa ndi kuchimwa kwawo anthuwa. 28 Kupanda kutero, ndiye kuti anthu a ku dziko lija munatitulutsaku adzati, ‘Yehova anawatulutsa kuti akawaphe mʼchipululu popeza sanathe kukawalowetsa mʼdziko limene anawalonjeza ndipo anadana nawo.’ 29 Koma iwowa ndi anthu anu, chuma chanu chimene munachitulutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ndi mkono wanu wotambasuka.”

Not Because of Israel’s Righteousness

Hear, Israel: You are now about to cross the Jordan(A) to go in and dispossess nations greater and stronger than you,(B) with large cities(C) that have walls up to the sky.(D) The people are strong and tall—Anakites! You know about them and have heard it said: “Who can stand up against the Anakites?”(E) But be assured today that the Lord your God is the one who goes across ahead of you(F) like a devouring fire.(G) He will destroy them; he will subdue them before you. And you will drive them out and annihilate them quickly,(H) as the Lord has promised you.

After the Lord your God has driven them out before you, do not say to yourself,(I) “The Lord has brought me here to take possession of this land because of my righteousness.” No, it is on account of the wickedness(J) of these nations(K) that the Lord is going to drive them out before you. It is not because of your righteousness or your integrity(L) that you are going in to take possession of their land; but on account of the wickedness(M) of these nations,(N) the Lord your God will drive them out(O) before you, to accomplish what he swore(P) to your fathers, to Abraham, Isaac and Jacob.(Q) Understand, then, that it is not because of your righteousness that the Lord your God is giving you this good land to possess, for you are a stiff-necked people.(R)

The Golden Calf

Remember this and never forget how you aroused the anger(S) of the Lord your God in the wilderness. From the day you left Egypt until you arrived here, you have been rebellious(T) against the Lord.(U) At Horeb you aroused the Lord’s wrath(V) so that he was angry enough to destroy you.(W) When I went up on the mountain to receive the tablets of stone, the tablets of the covenant(X) that the Lord had made with you, I stayed on the mountain forty days(Y) and forty nights; I ate no bread and drank no water.(Z) 10 The Lord gave me two stone tablets inscribed by the finger of God.(AA) On them were all the commandments the Lord proclaimed to you on the mountain out of the fire, on the day of the assembly.(AB)

11 At the end of the forty days and forty nights,(AC) the Lord gave me the two stone tablets,(AD) the tablets of the covenant. 12 Then the Lord told me, “Go down from here at once, because your people whom you brought out of Egypt have become corrupt.(AE) They have turned away quickly(AF) from what I commanded them and have made an idol for themselves.”

13 And the Lord said to me, “I have seen this people(AG), and they are a stiff-necked people indeed! 14 Let me alone,(AH) so that I may destroy them and blot out(AI) their name from under heaven.(AJ) And I will make you into a nation stronger and more numerous than they.”

15 So I turned and went down from the mountain while it was ablaze with fire. And the two tablets of the covenant were in my hands.(AK) 16 When I looked, I saw that you had sinned against the Lord your God; you had made for yourselves an idol cast in the shape of a calf.(AL) You had turned aside quickly from the way that the Lord had commanded you. 17 So I took the two tablets and threw them out of my hands, breaking them to pieces before your eyes.

18 Then once again I fell(AM) prostrate before the Lord for forty days and forty nights; I ate no bread and drank no water,(AN) because of all the sin you had committed,(AO) doing what was evil in the Lord’s sight and so arousing his anger. 19 I feared the anger and wrath of the Lord, for he was angry enough with you to destroy you.(AP) But again the Lord listened to me.(AQ) 20 And the Lord was angry enough with Aaron to destroy him, but at that time I prayed for Aaron too. 21 Also I took that sinful thing of yours, the calf you had made, and burned it in the fire. Then I crushed it and ground it to powder as fine as dust(AR) and threw the dust into a stream that flowed down the mountain.(AS)

22 You also made the Lord angry(AT) at Taberah,(AU) at Massah(AV) and at Kibroth Hattaavah.(AW)

23 And when the Lord sent you out from Kadesh Barnea,(AX) he said, “Go up and take possession(AY) of the land I have given you.” But you rebelled(AZ) against the command of the Lord your God. You did not trust(BA) him or obey him. 24 You have been rebellious against the Lord ever since I have known you.(BB)

25 I lay prostrate before the Lord those forty days and forty nights(BC) because the Lord had said he would destroy you.(BD) 26 I prayed to the Lord and said, “Sovereign Lord, do not destroy your people,(BE) your own inheritance(BF) that you redeemed(BG) by your great power and brought out of Egypt with a mighty hand.(BH) 27 Remember your servants Abraham, Isaac and Jacob. Overlook the stubbornness(BI) of this people, their wickedness and their sin. 28 Otherwise, the country(BJ) from which you brought us will say, ‘Because the Lord was not able to take them into the land he had promised them, and because he hated them,(BK) he brought them out to put them to death in the wilderness.’(BL) 29 But they are your people,(BM) your inheritance(BN) that you brought out by your great power and your outstretched arm.(BO)